Masalimo 10 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 10:1-18

Salimo 10

1Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

2Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

3Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

4Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

5Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

6Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

7Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

8Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

9Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

10Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

11Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

12Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.

Musayiwale anthu opanda mphamvu.

13Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?

Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,

“Iye sandiyimba mlandu?”

14Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti

Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.

15Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;

muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake

zimene sizikanadziwika.

16Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;

mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

17Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;

mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.

18Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,

ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.

Nueva Versión Internacional

Salmo 10:1-18

Salmo 10

Lámed

1¿Por qué, Señor, te mantienes distante?

¿Por qué te escondes en momentos de angustia?

2Con arrogancia persigue el malvado al indefenso,

pero quedará atrapado en sus propias artimañas.

3El malvado hace alarde de su propia codicia;

alaba al ambicioso y menosprecia al Señor.

4El malvado, con su nariz en alto, no busca a Dios.

No hay lugar para él en sus pensamientos.

5Todas sus empresas son siempre exitosas;

tan altas y alejadas de él están tus leyes

que se burla de todos sus enemigos.

6Y se dice a sí mismo: «Nada me hará caer jamás.

Nadie me hará daño».

Pe

7Llena está su boca de maldiciones,

de mentiras y amenazas;

bajo su lengua esconde maldad y violencia.

8Se pone al acecho en las aldeas,

se esconde en espera de sus víctimas

y asesina en emboscada al inocente.

Ayin

9Cual león que acecha en su guarida,

listo para atrapar al indefenso;

le cae encima y lo arrastra en su red.

10Bajo el peso de su poder,

sus víctimas son abatidas y caen desechas.

11Se dice a sí mismo: «Dios se ha olvidado.

Se cubre el rostro. Nunca ve nada».

Qof

12¡Levántate, Señor!

¡Levanta, oh Dios, tu brazo!

¡No te olvides de los indefensos!

13¿Por qué te ha de menospreciar el malvado?

¿Por qué ha de pensar que no lo llamarás a cuentas?

Resh

14Pero tú ves la maldad y la aflicción,

las tomas en cuenta y te harás cargo de ellas.

Las víctimas se encomiendan a ti;

tú eres la ayuda de los huérfanos.

Shin

15¡Rómpeles el brazo al malvado y al impío!

¡Pídeles cuentas de su maldad

hasta que desaparezca!

16El Señor es Rey eterno;

los paganos serán borrados de su tierra.

Tav

17Tú, Señor, escuchas el deseo de los indefensos,

les infundes aliento y atiendes a su clamor.

18Tú defiendes al huérfano y al oprimido,

para que el hombre, hecho de tierra,

no siga ya sembrando el terror.