Masalimo 10 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 10:1-18

Salimo 10

1Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

2Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

3Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

4Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

5Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

6Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

7Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

8Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

9Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

10Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

11Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

12Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.

Musayiwale anthu opanda mphamvu.

13Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?

Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,

“Iye sandiyimba mlandu?”

14Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti

Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.

15Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;

muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake

zimene sizikanadziwika.

16Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;

mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

17Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;

mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.

18Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,

ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 10:1-18

Zabbuli 10

110:1 a Zab 22:1, 11 b Zab 13:1Lwaki otwekwese, Ayi Mukama?

Lwaki otwekwese mu biseera eby’emitawaana?

2Omubi, mu malala ge, ayigganya abanafu;

muleke agwe mu nkwe ezo z’asaze.

310:3 Zab 94:4Kubanga omubi yeewaana ng’anyumya ku bibi ebiri mu mutima gwe,

agabula aboomululu n’avuma Mukama.

410:4 Zab 14:1; 36:1Omubi mu malala ge

tanoonya Katonda.

5Buli ky’akola kimugendera bulungi.

Amateeka go tagafaako,

era n’abalabe be abanyooma.

610:6 Kub 18:7Ayogera mu mutima gwe nti, “Sikangibwa,

nzija kusanyuka emirembe gyonna.”

710:7 a Bar 3:14* b Zab 73:8 c Zab 140:3Mu kamwa ke mujjudde okukolima n’obulimba awamu n’okutiisatiisa;

ebigambo bye bya mutawaana era bibi.

810:8 Zab 94:6Yeekukuma mu byalo

okutemula abantu abataliiko musango.

Yeekweka ng’aliimisa b’anatta.

910:9 Zab 17:12; 59:3; 140:5Asooba mu kyama ng’empologoma,

ng’alindirira okuzinduukiriza abateesobola.

Abakwasa n’abatwalira mu kitimba kye.

10B’abonyaabonya bagwa wansi

ne babetentebwa ng’amaanyi g’omubi gabasukkiridde.

1110:11 Yob 22:13Ayogera mu mutima gwe nti, “Katonda yeerabidde, amaaso ge agakwese,

era takyaddayo kubiraba.”

1210:12 a Zab 17:7; Mi 5:9 b Zab 9:12Golokoka, Ayi Mukama, ozikirize omubi, Ayi Katonda;

abanaku tobeerabiranga.

13Omuntu omubi ayinza atya okukunyooma, Ayi Katonda,

n’agamba mu mutima gwe nti

“Sigenda kwennyonnyolako?”

1410:14 a Zab 22:11 b Zab 37:5 c Zab 68:5Naye ggwe, Ayi Katonda, ennaku zaabwe n’okubonaabona kwabwe obiraba

era ojja kubikolako.

Ateesobola yeewaayo mu mikono gyo,

kubanga gwe mubeezi w’abatalina bakitaabwe.

1510:15 Zab 37:17Malawo amaanyi g’omwonoonyi,

muyite abyogere ebyo

ebibadde bitajja kuzuulwa.

1610:16 a Zab 29:10 b Ma 8:20Mukama ye Kabaka emirembe n’emirembe.

Amawanga galizikirizibwa mu nsi ye.

1710:17 1By 29:18; Zab 34:15Mukama awulira okwetaaga kw’ababonyaabonyezebwa, ogumye emitima gyabwe;

otege okutu kwo obaanukule.

1810:18 a Zab 82:3 b Zab 9:9Olwanirira abataliiko bakitaabwe n’abajoogebwa;

omuntu obuntu ow’oku nsi n’ataddayo kubatiisa.