Masalimo 10 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 10:1-18

Salimo 10

1Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

2Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

3Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

4Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

5Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

6Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

7Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

8Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

9Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

10Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

11Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

12Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.

Musayiwale anthu opanda mphamvu.

13Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?

Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,

“Iye sandiyimba mlandu?”

14Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti

Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.

15Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;

muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake

zimene sizikanadziwika.

16Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;

mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

17Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;

mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.

18Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,

ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 10:1-18

第 10 篇

求上帝懲治惡人

1耶和華啊,你為何遠遠站著?

為何在我遭難時隱藏起來?

2惡人狂妄地追逼窮苦人,

願他們落入自己所設的圈套。

3惡人誇耀自己的貪慾,

貪婪的人憎恨、咒詛耶和華。

4他們狂傲自大,心中沒有上帝,

從不尋求耶和華。

5他們凡事順利,

對你的審判不屑一顧,

對所有的仇敵嗤之以鼻。

6他們自以為可以屹立不倒,

世世代代永不遭殃。

7他們滿口咒詛、謊話和恐嚇之言,

舌頭沾滿禍害和邪惡。

8他們埋伏在村莊,

暗中監視受害者,殺害無辜。

9他們像獅子埋伏在暗處,

獵取無助的人,

用網羅拖走他們。

10不幸的人被擊垮,

倒在他們的暴力下。

11他們自言自語:「上帝忘記了,

祂掩面不理這些事!」

12耶和華啊,求你起來!

上帝啊,求你舉手施罰,

不要忘記無助的人!

13惡人為何輕視上帝,

以為上帝不會追究呢?

14但你已看到世人的疾苦,

隨時伸出援手。

困苦無助的人投靠你,

你是孤兒的幫助。

15求你打斷惡人的臂膀,

徹底追究他們的罪惡。

16耶和華永永遠遠是君王,

列邦必從祂的土地上滅亡。

17耶和華啊,

你知道困苦人的願望,

你必垂聽他們的呼求,

安慰他們。

18你為孤兒和受欺壓的人伸冤,

使渺小的世人不能再恐嚇他們。