Masalimo 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 1:1-6

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Salimo 1

1Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 1:1-6

卷一: 詩篇1—41

第 1 篇

有福之人

1-2不從惡人的計謀,

不與罪人為伍,

不和輕慢上帝的人同流合污,

只喜愛耶和華的律法,

晝夜默誦,

這樣的人有福了!

3他就像溪水旁的樹木——

按時結果子,

葉子也不凋零。

他必凡事亨通。

4惡人的光景卻截然不同!

他們就像被風吹散的糠秕。

5惡人在審判之日必無法逃脫,

罪人在義人的聚會中必站不住腳。

6因為耶和華看顧義人的腳步,

惡人的道路必通向滅亡。