Marko 6 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 6:1-56

Amupeputsa Yesu ku Nazareti

1Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake. 2Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa.

Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa! 3Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.

4Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.” 5Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa. 6Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo.

Yesu Atuma Ophunzira Khumi ndi Awiri

Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa. 7Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.

8Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama. 9Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera. 10Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo. 11Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”

12Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima. 13Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.

Yohane Mʼbatizi Adulidwa Mutu

14Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”

15Ena anati, “Iye ndi Eliya.”

Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”

16Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”

17Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira. 18Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.” 19Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero, 20chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.

21Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya. 22Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo.

Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.” 23Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”

24Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?”

Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”

25Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”

26Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza. 27Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende, 28nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake. 29Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

30Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa. 31Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”

32Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha. 33Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika. 34Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.

35Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo. 36Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”

37Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.”

Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”

38Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.”

Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”

39Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira. 40Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu. 41Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse. 42Onse anadya ndipo anakhuta, 43ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri. 44Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.

Yesu Ayenda pa Nyanja

45Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita. 46Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.

47Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda. 48Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira, 49koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula, 50pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha.

Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.” 51Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri, 52popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.

53Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko. 54Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu. 55Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye. 56Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

Священное Писание

Марк 6:1-56

Отвержение Исы Масиха в Его родном городе

(Мат. 13:54-58; Лк. 4:16-30)

1Иса вместе с учениками ушёл оттуда и пришёл в Свой родной город. 2Когда наступила суббота, Он начал учить в молитвенном доме. Многие, слушая Его, удивлялись:

– Откуда это у Него? Кто дал Ему такую мудрость? Как Он совершает такие чудеса? 3Разве Он не плотник, не сын Марьям и брат Якуба, Иосии, Иуды и Шимона? И разве не здесь, у нас, живут Его сёстры?

И они отвергли Его. 4Иса же сказал им:

– Пророка уважают везде, только не на его родине, не в его доме и не среди его родственников.

5И Он не мог совершить там ни одного чуда, лишь исцелил нескольких больных, возложив на них руки. 6Он удивлялся неверию этих людей.

Иса Масих посылает двенадцать учеников на служение

(Мат. 10:1, 9-14; Лк. 9:1-6)

Иса ходил по окрестным селениям и учил. 7Он созвал двенадцать учеников и начал посылать их по двое, дав им власть изгонять нечистых духов. 8Он повелел им ничего не брать с собой в дорогу, кроме посоха: ни хлеба, ни сумки, ни денег в поясе, 9лишь обуться в сандалии и не брать запасной одежды.

10– В какой бы дом вы ни вошли, – говорил Он им, – оставайтесь там до тех пор, пока не покинете это место. 11А если где-либо вас не примут и не захотят слушать, то, уходя, отряхните пыль с ваших ног6:11 Благочестивые иудеи отряхивали пыль со своих ног, когда возвращались из других стран, как бы очищаясь от ритуального осквернения. Делая же это по отношению к другим иудеям, они приравнивали их к язычникам., пусть это будет свидетельством против них.

12Ученики отправились в путь и проповедовали людям, призывая их к покаянию. 13Они изгнали много демонов, и многих больных помазали оливковым маслом и исцелили.

Царь Ирод убивает пророка Яхию

(Мат. 14:1-12; Лк. 9:7-9)

14Об Исе услышал царь Ирод6:14 Это Ирод Антипа, сын Ирода Великого от самарянки Малфаки. Он правил Галилеей и Переей с 4 г. до н. э. по 39 г. н. э., поскольку имя Исы становилось всё более известным, и некоторые говорили:

– Это пророк Яхия воскрес из мёртвых, и поэтому в Нём такая чудодейственная сила.

15Другие говорили, что это пророк Ильяс6:15 Ильяс – пророк, призывавший исраильский народ оставить грешный путь и вновь обратиться к признанию Всевышнего (см. 3 Цар. 17–4 Цар. 2).. А третьи утверждали, что Он пророк, подобный пророкам древности. 16Услышав эти разговоры, Ирод решил:

– Это Яхия, которого я обезглавил, он воскрес из мёртвых.

17В своё время Ирод приказал арестовать Яхию и бросить его в темницу из-за Иродиады, жены своего брата Филиппа6:17 Это Ирод Филипп I, сын Ирода Великого от Мариамны.. Ирод женился на ней, 18а Яхия говорил ему:

– Нельзя тебе жить с женой своего брата6:17-18 Женитьба Ирода на жене брата была нарушением Закона Всевышнего (см. Лев. 18:16; 20:21)..

19Иродиада затаила злобу на Яхию и хотела убить его. Однако она не могла ничего сделать, 20потому что Ирод боялся Яхию, зная, что это справедливый и святой человек, и берёг его. Слушая Яхию, Ирод приходил в смущение, но тем не менее ему нравилось его слушать. 21Наконец Иродиаде представился подходящий случай. Ирод в день своего рождения устроил пир для своих приближённых, военачальников и самых уважаемых людей Галилеи. 22Дочь Иродиады вошла к ним и танцевала, и так понравилась Ироду и возлежавшим за столом гостям, что царь сказал девушке:

– Проси у меня чего хочешь, и я дам тебе! – 23и поклялся ей: – Чего ни попросишь, всё дам тебе, хоть половину моего царства.

24Девушка пошла к матери за советом:

– Чего мне просить?

А та сказала:

– Проси голову пророка Яхии.

25Девушка сразу же поспешила к царю и попросила:

– Хочу, чтобы ты сейчас же подал мне на блюде голову пророка Яхии.

26Царь сильно опечалился, но не решился ей отказать, так как поклялся перед возлежавшими за столом гостями. 27Он немедленно послал палача и приказал ему принести голову Яхии. Тот пошёл в темницу, обезглавил Яхию 28и принёс его голову на блюде девушке, а та отдала её своей матери. 29Когда об этом услышали ученики Яхии, они пришли, забрали тело и похоронили его.

Насыщение более пяти тысяч человек

(Мат. 14:13-21; Лк. 9:10-17; Ин. 6:1-13)

30Посланники Исы возвратились к Нему и рассказали Ему обо всём, что они делали и чему учили народ. 31Иса сказал им:

– Давайте отправимся в безлюдное место, и там вы сможете немного отдохнуть, – ведь всё время приходило и уходило много народа, и у них даже не было времени поесть. 32И они отправились на лодке в пустынное место. 33Но люди видели, как они отплыли, причём многие их узнали и устремились туда посуху из всех городов, так что оказались на месте даже раньше лодки.

34Когда Иса сошёл на берег и увидел большую толпу, Он сжалился над людьми, потому что они были как овцы без пастуха6:34 См. Чис. 27:17; 3 Цар. 22:17; Езек. 34:5., и начал их учить многим вещам.

35Уже поздно вечером ученики подошли к Нему и сказали:

– Место здесь пустынное, и уже поздно. 36Отпусти народ, пусть пойдут в окрестные селения и посёлки и купят себе поесть.

37Но Иса ответил:

– Вы дайте им есть.

Ученики удивились:

– Неужели Ты хочешь, чтобы мы купили им всем еды? Но ведь это будет стоить примерно двести серебряных монет6:37 Букв.: «двести динариев». Динарий – римская монета, примерно равная дневному заработку наёмного работника (см. Мат. 20:2)., никак не меньше!

38– Сколько у вас хлеба? – спросил Иса. – Пойдите посмотрите.

Они пошли, узнали и ответили:

– Пять лепёшек и две рыбы.

39Иса велел рассадить народ группами на зелёной траве. 40Люди возлегли, расположившись группами по сто и по пятьдесят человек. 41Иса взял пять лепёшек и две рыбы и, подняв глаза к небу, благословил пищу. Затем Он стал разламывать лепёшки и давать их Своим ученикам, чтобы те раздавали народу, и две рыбы тоже разделил на всех. 42Все ели и насытились, 43а когда собрали куски лепёшек и рыбы, то их набралось двенадцать полных корзин. 44Одних только мужчин ело пять тысяч.

Хождение Исы Масиха по воде

(Мат. 14:22-33; Ин. 6:16-21)

45Сразу после этого Иса велел Своим ученикам сесть в лодку и переправиться на другую сторону озера, к Вифсаиде, а Сам Он оставался, пока не отпустил народ. 46Простившись с народом, Иса поднялся на гору помолиться. 47Когда наступила ночь, лодка была посреди озера, а Иса оставался один на берегу. 48Он увидел, что им приходится грести против ветра, и уже перед самым рассветом пошёл к ним, ступая по озеру. Он хотел уже приблизиться к ним6:48 Или: «Он хотел пройти мимо них»., 49но они, увидев Его идущим по воде, решили, что это призрак, и закричали, 50потому что они все видели Его и сильно испугались. Но Иса сразу же заговорил с ними:

– Успокойтесь, это Я, не бойтесь.

51Он вошёл к ним в лодку, и ветер утих. Ученики были поражены. 52Ведь они не поняли и чуда с лепёшками – их сердца были закрыты.

Исцеление больных в Генисарете

(Мат. 14:34-36)

53Переправившись на другую сторону озера, они пристали к берегу в Генисарете. 54Как только они вышли из лодки, люди сразу узнали Ису. 55Они обежали всю округу, рассказывая, где Он находится, и туда стали приносить на носилках больных. 56Где бы Он ни появлялся, в селениях, или в городах, или в деревнях, люди выносили на площади больных и просили Ису, чтобы Он позволил им прикоснуться хотя бы к кисточке на краю Его одежды6:56 К краям верхней мужской одежды иудеи пришивали кисточки, в которые обязательно вплетались голубые нити. Эти кисточки должны были напоминать иудеям о необходимости исполнять повеления Всевышнего (см. Чис. 15:38-40; Втор. 22:12).. И все, кто прикасался, выздоравливали.