Marko 16 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 16:1-20

Kuuka kwa Yesu

1Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu. 2Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda 3ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”

4Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale. 5Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.

6Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo. 7Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’ ”

8Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.

[Mipukutu yoyambirira ndi maumboni akale mulibe vesi 9 mpaka 20.]

Yesu Aonekera kwa Mariya Magadalena

9Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri. 10Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira. 11Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira Awiri

12Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi. 13Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.

Yesu Ayankhula kwa Ophunzira Khumi ndi Mmodzi

14Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.

15Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse. 16Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa. 17Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano; 18adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”

Yesu Apita Kumwamba

19Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu. 20Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.

Persian Contemporary Bible

مَرقُس 16:1‏-20

عيسی زنده می‌شود

1‏-2عصر روز شنبه، در پايان روز استراحت، مريم مجدليه، سالومه و مريم مادر يعقوب داروهای معطر خريدند تا مطابق رسم يهود، جسد مرده را با آن معطر سازند.

روز بعد كه يكشنبه بود، صبح زود پيش از طلوع آفتاب، دارو را به سر قبر بردند. 3در بين راه تمام گفتگويشان دربارهٔ اين بود كه چگونه آن سنگ بزرگ را از جلو در قبر جابه‌جا كنند.

4وقتی بر سر قبر رسيدند، ديدند كه سنگ بزرگ جابه‌جا شده و درِ قبر باز است! 5پس داخل قبر كه مثل يک غار بود شدند و ديدند فرشته‌ای با لباس سفيد در طرف راست قبر نشسته است. زنان لرزيدند.

6ولی فرشته به ايشان گفت: «نترسيد. مگر به دنبال عيسای ناصری نمی‌گرديد كه روی صليب كشته شد؟ او اينجا نيست. عيسی دوباره زنده شده است! نگاه كنيد، اين هم جايی كه جسدش را گذاشته بودند! 7اكنون برويد و به شاگردان او و پطرس مژده دهيد كه او پيش از شما به جليل می‌رود تا شما را در آنجا ببيند، درست همانطور كه پيش از مرگ به شما گفته بود.»

8زنان پا به فرار گذاشتند و از ترس می‌لرزيدند به طوری که نتوانستند با كسی صحبت كنند.

9عيسی روز يكشنبه صبح زود زنده شد. اولين كسی كه او را ديد مريم مجدليه بود، كه عيسی از وجود او هفت روح ناپاک بيرون كرده بود. 10‏-11او نيز رفت و به شاگردان عيسی كه گريان و پریشانحال بودند، مژده داد كه عيسی را زنده ديده است! اما ايشان سخن او را باور نكردند. 12تا اينكه عصر همان روز، عيسی خود را به دو نفر از ايشان نشان داد. آنان از شهر اورشليم به طرف دهی می‌رفتند. ابتدا او را نشناختند، چون ظاهر خود را عوض كرده بود. 13سرانجام وقتی او را شناختند، با عجله به اورشليم بازگشتند و به ديگران خبر دادند. ولی باز هیچکس حرفشان را باور نكرد.

14در آخر عيسی به آن يازده شاگرد، وقتی كه شام می‌خوردند ظاهر شد و ايشان را به خاطر بی‌ايمانی و سماجتشان سرزنش كرد، زيرا گفته‌های كسانی را كه او را بعد از مرگ زنده ديده بودند، باور نكرده بودند.

15سپس به ايشان گفت: «حال بايد به سراسر دنيا برويد و پيغام انجيل را به مردم برسانيد. 16كسانی كه ايمان بياورند و غسل تعميد بگيرند، نجات می‌يابند، اما كسانی كه ايمان نياورند، داوری خواهند شد.

17«كسانی كه ايمان می‌آورند، با قدرت من، ارواح پليد را از مردم بيرون خواهند كرد و به زبانهای تازه سخن خواهند گفت. 18مارها را برخواهند داشت و در امان خواهند بود، و اگر زهر كشنده‌ای بخورند صدمه‌ای نخواهند ديد، دست بر بيماران خواهند گذاشت و ايشان را شفا خواهند داد.»

19چون عيسای خداوند سخنان خود را به پايان رساند، به آسمان صعود كرد و به دست راست خدا نشست.

20شاگردان به همه جا رفته، پيغام انجيل را به همه رساندند. خداوند نيز با ايشان كار می‌كرد و با معجزاتی كه عطا می‌نمود، پيغام ايشان را ثابت می‌كرد.