Marko 16 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 16:1-20

Kuuka kwa Yesu

1Litapita tsiku la Sabata, Mariya Magadalena, ndi amayi ake a Yakobo, ndi Salome anagula zonunkhiritsa ndi cholinga chakuti apite akadzoze thupi la Yesu. 2Mmamawa, tsiku loyamba la Sabata, dzuwa litangotuluka kumene, anali pa ulendo wopita ku manda 3ndipo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi akatikugudubuzira mwala pa khomo la manda ndani?”

4Koma atakweza maso awo, anaona kuti mwala umene unali waukulu kwambiri wagubuduzidwa kale. 5Atalowa mʼmanda, anaona mnyamata atavala mwinjiro woyera atakhala ku mbali ya kumanja, ndipo iwo anachita mantha.

6Iye anati, “Musaope. Kodi mukufuna Yesu wa ku Nazareti, amene anapachikidwa? Wauka! Sali muno. Onani malo amene anamugonekapo. 7Koma pitani, kawuzeni ophunzira ake ndi Petro kuti, ‘Iye watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona Iye monga momwe anakuwuzirani.’ ”

8Akunjenjemera ndi kudabwa, amayiwo anatuluka ndipo anathawa ku mandako. Sananene china chilichonse kwa aliyense, chifukwa anachita mantha.

[Mipukutu yoyambirira ndi maumboni akale mulibe vesi 9 mpaka 20.]

Yesu Aonekera kwa Mariya Magadalena

9Yesu atauka kwa akufa mmawa pa tsiku loyamba la Sabata, anayamba kuonekera kwa Mariya Magadalena, amene anatulutsa mwa iye ziwanda zisanu ndi ziwiri. 10Iye anapita ndi kukawawuza amene anali ndi Yesu, amene ankakhuza maliro ndi kulira. 11Atamva kuti Yesu ali moyo ndikuti amuona, iwo sanakhulupirire.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira Awiri

12Zitatha izi Yesu anaonekera mʼmaonekedwe ena kwa awiri a iwo amene anali ku dera la ku mudzi. 13Iwo anabwerera ndi kudzawawuza enawo; koma iwo sanakhulupirirebe.

Yesu Ayankhula kwa Ophunzira Khumi ndi Mmodzi

14Pambuyo pake Yesu anaonekera kwa khumi ndi mmodziwo pamene ankadya; anawadzudzula chifukwa chopanda chikhulupiriro ndi kukanitsitsa kwawo kuti akhulupirire amene anamuona Iye atauka.

15Anati kwa iwo, “Pitani mʼdziko lonse lapansi ndipo mukalalikire Uthenga Wabwino kwa zolengedwa zonse. 16Aliyense amene akakhulupirire nabatizidwa adzapulumuka, koma amene sakakhulupirira adzalangidwa. 17Tsono zizindikiro izi zidzawatsata amene adzakhulupirira: Mʼdzina langa adzatulutsa ziwanda; adzayankhula malilime atsopano; 18adzanyamula njoka ndi manja awo; ndipo pamene adzamwa mankhwala akupha, sadzawapweteka nʼpangʼonongʼono pomwe; adzasanjika manja awo pa anthu odwala ndipo odwalawo adzachira.”

Yesu Apita Kumwamba

19Ambuye Yesu atatha kuyankhulana nawo, anatengedwa kupita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu. 20Pamenepo ophunzira aja anapita ndi kukalalikira ponseponse, ndipo Ambuye anagwira nawo ntchito pamodzi, ndipo anatsimikizira mawuwo ndi zizindikiro zimene ankachita.

New Russian Translation

Марка 16:1-20

Воскресение Иисуса из мертвых

(Мат. 28:1-8; Лк. 24:1-10; Ин. 20:1-18)

1Когда прошла суббота16:1 Суббота, религиозный день отдыха иудеев, начавшись вечером предыдущего дня, завершалась с закатом солнца., Мария Магдалина, Мария, мать Иакова, и Саломия купили благовония, чтобы пойти и помазать Его. 2Рано утром в первый день недели16:2 У иудеев неделя начиналась с воскресенья., едва лишь взошло солнце, они пришли к гробнице. 3По дороге они говорили друг другу:

– Кто же откатит нам камень от входа в гробницу?

4Но когда они пришли, то увидели, что камень уже отвален, а он был очень большим. 5Они вошли в гробницу и увидели юношу, одетого в белое, он сидел справа от входа. Женщины испугались. 6А он сказал им:

– Не бойтесь. Вы ищете распятого Иисуса из Назарета? Он воскрес! Его здесь нет. Посмотрите на место, где Его положили. 7Идите и скажите Его ученикам, включая Петра, что Он отправился прежде вас в Галилею. Там вы Его увидите, как Он вам и говорил.

8Женщины вышли и побежали от гробницы, испуганные и изумленные. Они ничего никому не сказали, так сильно они испугались.

Иисус является Марии Магдалине

9Воскреснув рано утром в первый день недели, Иисус явился сначала Марии Магдалине, из которой Он когда-то изгнал семь демонов. 10Она пошла и сообщила тем, кто был с Ним, горевавшим и плакавшим. 11Когда они услышали, что Иисус жив и что она Его видела, они не поверили.

12Потом Иисус явился в другом облике двоим из них, когда они шли из города. 13Эти двое возвратились и рассказали остальным, но и им не поверили. 14Позже Иисус явился одиннадцати ученикам, когда те возлежали за столом. Он упрекнул их за неверие и упрямство, потому что они не поверили тем, кто видел Его воскресшим.

Великое поручение и вознесение Иисуса

(Мат. 28:18-20; Лк. 24:36-53; Ин. 20:19-23; Деян. 1:7-12)

15Он сказал им:

– Идите по всему миру и возвещайте Радостную Весть всем людям16:15 Букв.: «всему творению».. 16Тот, кто поверит и примет крещение, будет спасен, а тот, кто не поверит, будет осужден. 17Уверовавших будут сопровождать знамения: они будут Моим именем изгонять демонов, говорить на новых языках; 18они будут брать в руки змей, и если даже выпьют смертельную отраву, это не повредит им; они будут возлагать руки на больных, и те будут выздоравливать.

19Когда Господь Иисус сказал им все это, Он вознесся на небеса и сел по правую руку от Бога16:19 См. Пс. 109:1.. 20А ученики пошли и повсюду проповедовали, и Господь содействовал им, подтверждая их слово знамениями.