Marko 14 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 14:1-72

Yesu Adzozedwa ku Betaniya

1Tsopano panali patatsala masiku awiri okha kuti tsiku la Paska ndi Phwando la Buledi wopanda yisiti lifike, ndipo akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ankafunafuna mpata woti amugwire Yesu ndi kumupha. 2Iwo anati, “Koma osati nthawi yaphwando, chifukwa anthu angachite chiwawa.”

3Pamene Iye anali mʼBetaniya, atakhala pa tebulo akudya mʼnyumba ya munthu wodziwika kuti Simoni wakhate, anabwera mayi ndi botolo la mafuta onunkhira amtengo wapamwamba opangidwa ndi nadi. Anaphwanya botololo nakhuthula mafutawo pa mutu wa Yesu.

4Ena mwa iwo amene analipo, anakwiya nati kwa wina ndi mnzake, “Chifukwa chiyani akuwononga mafuta onunkhirawa? 5Akanatheka kugulitsidwa ndi ndalama zambiri zoposa malipiro a pa chaka ndipo ndalamazo ndi kupatsa osauka.” Ndipo anamudzudzula iye mwaukali.

6Yesu anati, “Musiyeni, chifukwa chiyani mukumuvutitsa? Wandichitira Ine chinthu chabwino. 7Anthu osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, ndipo mukhoza kuwathandiza nthawi iliyonse mungafune. Koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse. 8Wachita zimene akanatha. Wathira mafuta onunkhira pa thupi langa nthawi isanakwane kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda. 9Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”

10Kenaka Yudasi Isikarioti, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anapita kwa akulu a ansembe kuti akamupereke Yesu. 11Iwo anakondwa pakumva zimenezi ndipo analonjeza kumupatsa iye ndalama. Ndipo ankadikira mpata wabwino woti amupereke.

Mgonero wa Ambuye

12Pa tsiku loyamba la Phwando la Buledi wopanda yisiti, nthawi imene mwa mwambo inali ya kupha mwana wankhosa wa Paska, ophunzira a Yesu anafunsa Iye kuti, “Mufuna tipite kuti kumene tikakonzekere kuti mukadyere Paska?”

13Pamenepo anatumiza awiri mwa ophunzira ake, nawawuza kuti, “Pitani mu mzinda, ndipo mukakumana ndi mwamuna wonyamula mtsuko wa madzi. Kamutsatireni iye. 14Kawuzeni mwini nyumba imene iye akalowemo kuti, ‘Aphunzitsi akufunsa: kodi chili kuti chipinda changa cha alendo, kumene ndidyere Paska ndi ophunzira anga?’ 15Iye adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala kale ndi zonse ndi chokonzedwa kale. Katikonzereni ife Paska kumeneko.”

16Ophunzirawo anachoka, napita mu mzindawo ndipo anakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Choncho anakakonza Paska.

17Ndipo kutada Yesu anafika ndi khumi ndi awiriwo. 18Pamene ankadya pa tebulo Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka, mmodzi amene akudya ndi Ine.”

19Iwo anamva chisoni, ndipo mmodzi ndi mmodzi anati kwa Iye, “Kodi ndine?”

20Iye anayankha kuti, “Ndi mmodzi mwa khumi ndi awirinu, amene akusunsa buledi mʼmbale pamodzi ndi Ine. 21Mwana wa Munthu adzapita monga momwe zinalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene adzapereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”

22Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”

23Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo.

24Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri. 25Zoonadi, ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mphesa mpaka tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano mu ufumu wa Mulungu.”

26Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.

Yesu Aneneratu zakuti Petro Adzamukana

27Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:

“ ‘Kantha Mʼbusa,

ndipo nkhosa zidzabalalika.’

28Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”

29Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”

30Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”

31Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.

Mu Getsemani

32Ndipo anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Khalani pano pamene Ine ndi kupemphera.” 33Iye anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane, ndipo anayamba kumva chisoni kwambiri ndi kuvutika mu mtima. 34Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”

35Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi ndi kupemphera kuti ngati ndi kotheka oralo limupitirire. 36Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”

37Kenaka anabwerera kwa ophunzira ake ndipo anawapeza akugona, Iye anati kwa Petro, “Simoni, kodi uli mtulo? Kodi simukanatha kukhala maso kwa ora limodzi? 38Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”

39Kenakanso anachoka ndi kukapemphera chimodzimodzi. 40Iye atabwerera, anawapezanso akugona, chifukwa mʼmaso mwawo munadzaza tulo. Iwo sanadziwe choti anene kwa Iye.

41Atabweranso kachitatu, anawafunsa kuti, “Kodi mukugonabe ndi kupumula? Pakwana! Nthawi yafika. Taonani, Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa. 42Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”

Amugwira Yesu

43Iye akuyankhulabe, Yudasi, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anatulukira. Anali ndi gulu la anthu litanyamula malupanga ndi zibonga, otumidwa ndi akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo, ndi akuluakulu.

44Tsopano womupereka anapangana chizindikiro ndi iwo kuti: “Amene ndikapsompsone ndi iyeyo; mukamugwire ndi kumutenga ali womangidwa.” 45Atapita kwa Yesu nthawi yomweyo, Yudasi anati, “Aphunzitsi,” ndipo anapsompsona. 46Anthu anamugwira Yesu ndi kumumanga. 47Kenaka mmodzi wa iwo amene anayima pafupipo anatulutsa lupanga lake nakhapa wantchito wa wamkulu wa ansembe, nʼkudula khutu lake.

48Yesu anati, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira, kuti mubwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? 49Tsiku ndi tsiku ndinali ndi inu, kuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, koma inu simunandigwire. Koma malemba ayenera kukwaniritsidwa.” 50Pamenepo ophunzira ake onse anathawa namusiya yekha.

51Mnyamata wamngʼono amene anangofundira nsalu yokha, wopanda chovala ankamutsatira Yesu. Atamugwira, 52anathawa wamaliseche kusiya nsalu yake mʼmbuyo.

Yesu ku Bwalo la Milandu

53Anamutengera Yesu kwa mkulu wa ansembe, ndipo akulu a ansembe, akuluakulu ndi aphunzitsi amalamulo anasonkhana pamodzi. 54Petro anamutsatira ali patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Kumeneko anakhala pansi ndi alonda namawotha moto.

55Akulu a ansembe ndi onse olamulira a Ayuda ankafunafuna umboni womutsutsa Yesu kuti amuphe, koma sanapeze wina uliwonse. 56Ambiri anamunenera Iye maumboni abodza, koma maumboni awo sanagwirizane.

57Kenaka ena anayimirira namunenera umboni wonama womutsutsa Iye kunena kuti, 58“Tamumva akunena kuti, ‘Ndidzawononga Nyumba ya Mulungu iyi yopangidwa ndi anthu ndipo mʼmasiku atatu ndidzamanga ina, osati yopangidwa ndi munthu.’ ” 59Ngakhale iwonso umboni wawo sunagwirizane.

60Kenaka mkulu wa ansembe anayimirira pakati pawo namufunsa Yesu kuti, “Kodi suyankha? Kodi umboni uwu ndi wotani umene anthu akukuchitira?” 61Koma Yesu anakhala chete ndipo sanayankhe.

Mkulu wa ansembe anabwereza kumufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Khristu Mwana wa Wodalitsikayo?”

62Yesu anati, “Ndine, ndipo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera mʼmitambo ya kumwamba.”

63Mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zaunsembe zake. Iye anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani tikufuna mboni zinanso? 64Mwamva mwanowo. Muganiza chiyani?”

Onse anavomereza kuti ndi woyenera imfa. 65Kenaka ena anayamba kumulavulira malovu; anamumanga mʼmaso, namumenya ndi zibakera ndipo anati, “Nenera!” Ndipo asilikali anamutenga namumenya.

Petro Akana Yesu

66Petro ali chakumunsi kwa bwalo la milandu, mmodzi wa atsikana a ntchito a mkulu wa ansembe anabwera. 67Ataona Petro akuwotha moto, anamuyangʼanitsitsa.

Iye anati, “Iwenso unali pamodzi ndi Mnazareti, Yesu.”

68Koma iye anakana nati, “Sindikudziwa kapena kumvetsetsa zimene ukuyankhula.” Ndipo anachoka napita ku chipata.

69Pamene mtsikana wantchitoyo anamuona iye, anatinso kwa iwo amene anayimirira pomwepo, “Munthu uyu ndi mmodzi mwa iwo.” 70Anakananso kachiwiri.

Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pafupi anati kwa Petro, “Zoonadi ndiwe mmodzi wa iwo, pakuti ndiwe mu Galileya.”

71Iye anayamba kudzitemberera, nalumbira kuti, “Sindimudziwa munthu ameneyu.”

72Nthawi yomweyo tambala analira kachiwiri. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Yesu ananena anamuwuza kuti, “Tambala asanalire kawiri, iwe udzandikana katatu.” Ndipo iye anasweka mtima nayamba kulira.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Марк 14:1-72

Религиозные вожди замышляют убить Ису аль-Масиха

(Мат. 26:2-5; Лк. 22:1-2; Ин. 11:45-53)

1Через два дня наступал праздник Освобождения и праздник Пресных хлебов14:1 Праздник Освобождения – этот праздник отмечался в память об избавлении иудейского народа под руководством пророка Мусы из Египетского рабства (см. Исх. 12:1-14; Чис. 1:14; Втор. 16:1-8). Праздник Пресных хлебов – в этот праздник, шедший сразу же за праздником Освобождения и длившийся семь дней, предписывалось есть только пресный хлеб (см. Исх. 12:15-20; 13:3-10; Лев. 23:6-8; Чис. 28:17-25). Со временем оба эти праздника практически слились в один, и поэтому их названия стали взаимозаменяемы.. Главные священнослужители и учители Таурата искали удобного случая, чтобы хитростью схватить Ису и убить.

2– Только не во время праздника, – говорили они, – иначе народ может взбунтоваться.

Помазание Исы аль-Масиха дорогим ароматическим маслом

(Мат. 26:6-13; Лк. 7:37-38; Ин. 12:1-8)

3Иса в это время был в Вифании, в доме Шимона прокажённого14:3 Скорее всего, Шимон когда-то страдал от кожного заболевания и исцелился (ср. Лев. 13:45-46; Чис. 5:2), но прозвище «прокажённый» за ним осталось.. Он возлежал за столом, когда в дом вошла женщина с алебастровым кувшином очень дорогого ароматического масла, приготовленного из чистого нарда14:3 Нард – ароматическая жидкость, получаемая из определённого растения, которое произрастает только в Индии, на Гималаях, и поэтому доставка делала нард дорогостоящим товаром. Нард смешивали с другими веществами и продавали в алебастровых кувшинах в виде масла, мази или нардовой воды.. Отбив запечатанное горлышко, она вылила масло на голову Исы. 4Некоторые из присутствовавших возмутились.

– Зачем так тратить это дорогое ароматическое масло? 5Ведь его можно было продать больше чем за триста серебряных монет14:5 Букв.: «триста динариев»., а деньги раздать нищим, – упрекали они её.

6Но Иса сказал:

– Оставьте её, что вы её упрекаете? Она сделала для Меня доброе дело. 7Потому что нищие всегда с вами, и вы можете делать им добро, когда захотите, а Я не всегда буду с вами. 8Она сделала, что могла: заранее помазала Моё тело для погребения. 9Говорю вам истину: во всём мире, везде, где будет возвещена Радостная Весть, будут вспоминать об этой женщине и о том, что она сделала.

Иуда Искариот решает предать Ису аль-Масиха

(Мат. 26:14-16; Лк. 22:3-6)

10Иуда Искариот, один из двенадцати учеников, пошёл к главным священнослужителям, чтобы предать им Ису. 11Услышав, для чего он пришёл, они обрадовались и обещали заплатить ему. И Иуда стал искать удобного случая, чтобы предать Ису.

Приготовление учеников к празднику Освобождения

(Мат. 26:17-19; Лк. 22:7-13)

12В первый день праздника Пресных хлебов14:12 То есть праздника Освобождения, см. ст. 1 со сноской., когда иудеи закалывали ягнят в память об их освобождении, ученики спросили Ису:

– Куда нам пойти, чтобы приготовить Тебе праздничный ужин?

13И Он послал двух учеников, сказав им:

– Идите в город, там вы встретите человека, несущего кувшин воды, идите за ним. 14Скажите хозяину дома, куда этот человек войдёт: «Учитель спрашивает: где Моя комната, в которой Я буду есть праздничный ужин с Моими учениками?» 15Он покажет вам большую комнату наверху, приготовленную и убранную; там и приготовьте нам ужин.

16Ученики пошли, вошли в город; и всё произошло так, как им сказал Иса, и они приготовили праздничный ужин.

Последний ужин с учениками

(Мат. 26:20-29; Лк. 22:17-23; 1 Кор. 11:23-25)

17Вечером Иса пришёл туда с двенадцатью учениками. 18Когда они возлежали и ели, Иса сказал:

– Говорю вам истину: один из вас, кто сейчас ест со Мной, предаст Меня.

19Учеников это сильно опечалило, и один за другим они стали спрашивать Его:

– Но ведь это же не я?

20– Один из двенадцати, – ответил Иса, – тот, кто вместе со Мной обмакивает хлеб в блюдо. 21Да, Ниспосланный как Человек уходит так, как о Нём сказано в Писании, но горе тому человеку, который предаёт Его! Лучше бы ему вообще не родиться.

22Когда они ели, Иса взял хлеб и, благословив, разломил его, дал им и сказал:

– Возьмите, это Моё тело.

23Затем Он взял чашу, поблагодарил за неё Аллаха и подал им, и они все пили из неё.

24– Это Моя кровь священного соглашения14:24 Ср. Исх. 24:8; Евр. 9:18-20., проливаемая за многих, – сказал Иса. – 25Говорю вам истину: Я уже не буду пить от плода виноградного до того дня, когда Я буду пить новое14:25 Или: «снова». вино в Царстве Аллаха.

Предсказание об отречении Петира

(Мат. 26:30-35; Лк. 22:31-34; Ин. 13:37-38)

26Они спели песни из Забура14:26 Традиционно на этом празднике иудеи пели песни из Забура со 112 по 117 и 135. и пошли на Оливковую гору.

27– Вы все отступитесь от Меня, – сказал им Иса, – ведь написано:

«Я поражу пастуха,

и разбегутся овцы»14:27 Зак. 13:7..

28Но когда Я воскресну, то встречу вас в Галилее.

29Петир сказал Ему:

– Даже если все Тебя оставят, я никогда этого не сделаю.

30– Говорю тебе истину, – сказал ему Иса, – в эту ночь, прежде чем петух пропоёт два раза, ты трижды отречёшься от Меня.

31Но Петир уверял:

– Даже если мне придётся умереть с Тобой, я никогда не откажусь от Тебя.

И все ученики говорили то же.

Молитва в Гефсиманском саду

(Мат. 26:36-46; Лк. 22:39-46)

32Они пришли на место, называемое Гефсимания, и Иса сказал Своим ученикам:

– Посидите здесь, пока Я буду молиться.

33С Собой Он взял Петира, Якуба и Иохана. Его охватили ужас и тревога.

34Тогда Он сказал им:

– Душа моя объята смертельной печалью. Побудьте здесь и бодрствуйте.

35Отойдя немного, Он пал на землю и молился, чтобы, если возможно, этот час миновал Его.

36– Дорогой Отец! – сказал Он. – Ты всё можешь! Пронеси эту чашу страданий мимо Меня, но пусть всё будет не как Я хочу, а как Ты хочешь.

37Он возвратился к Своим ученикам и нашёл их спящими.

– Шимон, – спросил Он Петира, – ты спишь? Неужели ты не мог пободрствовать хоть один час? 38Бодрствуйте и молитесь, чтобы вам не поддаться искушению. Дух бодр, но тело слабо.

39Он снова ушёл и молился теми же словами. 40Когда Он вернулся, ученики опять спали, потому что их веки отяжелели; они не знали, что отвечать Исе. 41Возвратившись в третий раз, Иса сказал им:

– Вы всё спите и отдыхаете? Довольно! Время настало, и Ниспосланный как Человек предаётся в руки грешников. 42Вставайте, идём. Вот уже и Мой предатель приблизился.

Иса аль-Масих предан и арестован

(Мат. 26:47-56; Лк. 22:47-50; Ин. 18:3-11)

43Он ещё говорил, как появился Иуда, один из двенадцати учеников, и с ним толпа, вооружённая мечами и кольями. Их послали главные священнослужители, учители Таурата и старейшины. 44Предатель так условился с ними:

– Хватайте Того, Кого я поцелую, и уводите под стражей.

45Придя на место, Иуда сразу же подошёл к Исе и сказал:

– Учитель! – и поцеловал Его.

46Пришедшие с Иудой, схватив Ису, взяли Его под стражу. 47Один из стоявших рядом вытащил меч, ударил им раба главного священнослужителя и отсёк ему ухо.

48– Что Я, разбойник, что вы пришли с мечами и кольями, чтобы арестовать Меня? – спросил их Иса. – 49Каждый день Я был с вами в храме и учил, и вы не арестовывали Меня. Но пусть исполнится Писание.

50Все ученики оставили Его и убежали. 51За Исой пошёл лишь один молодой человек, завернувшись в покрывало на голое тело. Когда его схватили, 52он вырвался и убежал голый, оставив покрывало в руках у стражников.

На допросе у верховного священнослужителя Каиафы

(Мат. 26:57-68; Лк. 22:54-55, 63-71; Ин. 18:12-13, 19-24)

53Они привели Ису к верховному священнослужителю, где собрались все главные священнослужители, старейшины и учители Таурата. 54Петир следовал за Исой на некотором расстоянии и, пройдя во двор верховного священнослужителя, сел со стражниками греться у костра. 55Главные священнослужители и весь Высший Совет14:55 Высший Совет (букв.: «синедрион») – высший политический, религиозный и судебный орган иудеев. В состав Совета входил семьдесят один человек. искали показания против Исы, чтобы приговорить Его к смерти, но они ничего не могли найти. 56Выступало много лжесвидетелей, но их показания не совпадали. 57Нашлось несколько человек, которые встали и ложно заявили:

58– Мы слышали, как Он говорил: «Я разрушу этот храм, сотворённый руками людей, и в три дня построю другой, нерукотворный».

59Но и в этом их свидетельства не совпали. 60Потом верховный священнослужитель, встав посредине, спросил Ису:

– Тебе нечего ответить на эти свидетельства против Тебя?

61Но Иса молчал, не отвечая ни слова. Верховный священнослужитель опять спросил Его:

– Ты ли обещанный Масих, Сын Благословенного?

62– Я, – ответил Иса, – и вы увидите Ниспосланного как Человек сидящим по правую руку от могучего Бога и идущим на облаках небесных14:62 См. Заб. 109:1; Дан. 7:13..

63Разорвав в негодовании на себе одежду, верховный священнослужитель сказал:

– Какие нам ещё нужны свидетели?! 64Вы сами слышали Его кощунство! Каково ваше решение?

Все признали, что Он виновен и заслуживает смерти. 65Тогда некоторые начали плевать на Него; Исе закрывали лицо, били Его кулаками и говорили:

– Пророчествуй!

Потом Его стали избивать стражники.

Отречение Петира

(Мат. 26:69-75; Лк. 22:54-62; Ин. 18:15-18, 25-27)

66Петир же в это время был во дворе. Туда пришла одна из служанок верховного священнослужителя 67и, увидев Петира, гревшегося у костра, всмотрелась в него и сказала:

– Ты тоже был с Исой из Назарета.

68Но Петир отрицал это.

– Я вообще не знаю, о чём ты говоришь, – сказал он и вышел во внешний двор. И тут пропел петух. 69Служанка увидела Петира и там и опять стала говорить стоявшим рядом:

– Это один из них.

70Петир снова всё отрицал. Но спустя немного времени стоявшие там люди опять сказали ему:

– Точно, ты один из них, ты ведь галилеянин.

71Но Петир начал клясться, призывая на себя проклятия:

– Я не знаю Человека, о Котором вы говорите.

72И тотчас во второй раз пропел петух, и тогда Петир вспомнил слова Исы: «Прежде чем два раза пропоёт петух, ты трижды отречёшься от Меня». И он горько заплакал.