Marko 1 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 1:1-45

Yohane Mʼbatizi Akonza Njira

1Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu, 2monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya:

“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu,

amene adzakonza njira yanu,”

3“Mawu a wofuwula mʼchipululu,

‘Konzani njira ya Ambuye,

wongolani njira zake.’ ”

4Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo. 5Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani. 6Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo. 7Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake. 8Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”

Kubatizidwa ndi Kuyesedwa kwa Yesu

9Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani. 10Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda. 11Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”

12Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu, 13ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.

Yesu Alengeza za Uthenga Wabwino

14Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati, 15“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

16Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi. 17Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 18Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

19Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo. 20Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

21Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa. 22Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo. 23Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti, 24“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

25Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!” 26Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.

27Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.” 28Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

29Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya. 30Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye. 31Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.

32Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda. 33Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo, 34Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.

Yesu Apemphera Kumalo a Yekha

35Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera. 36Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye, 37ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”

38Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.” 39Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.

Yesu Achiritsa Wakhate

40Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

41Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” 42Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.

43Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti, 44“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.” 45Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

King James Version

Mark 1:1-45

1The beginning of the gospel of Jesus Christ, the Son of God; 2As it is written in the prophets, Behold, I send my messenger before thy face, which shall prepare thy way before thee. 3The voice of one crying in the wilderness, Prepare ye the way of the Lord, make his paths straight. 4John did baptize in the wilderness, and preach the baptism of repentance for the remission of sins. 5And there went out unto him all the land of Judæa, and they of Jerusalem, and were all baptized of him in the river of Jordan, confessing their sins. 6And John was clothed with camel’s hair, and with a girdle of a skin about his loins; and he did eat locusts and wild honey; 7And preached, saying, There cometh one mightier than I after me, the latchet of whose shoes I am not worthy to stoop down and unloose. 8I indeed have baptized you with water: but he shall baptize you with the Holy Ghost. 9And it came to pass in those days, that Jesus came from Nazareth of Galilee, and was baptized of John in Jordan. 10And straightway coming up out of the water, he saw the heavens opened, and the Spirit like a dove descending upon him: 11And there came a voice from heaven, saying, Thou art my beloved Son, in whom I am well pleased. 12And immediately the Spirit driveth him into the wilderness. 13And he was there in the wilderness forty days, tempted of Satan; and was with the wild beasts; and the angels ministered unto him. 14Now after that John was put in prison, Jesus came into Galilee, preaching the gospel of the kingdom of God, 15And saying, The time is fulfilled, and the kingdom of God is at hand: repent ye, and believe the gospel. 16Now as he walked by the sea of Galilee, he saw Simon and Andrew his brother casting a net into the sea: for they were fishers. 17And Jesus said unto them, Come ye after me, and I will make you to become fishers of men. 18And straightway they forsook their nets, and followed him. 19And when he had gone a little further thence, he saw James the son of Zebedee, and John his brother, who also were in the ship mending their nets. 20And straightway he called them: and they left their father Zebedee in the ship with the hired servants, and went after him. 21And they went into Capernaum; and straightway on the sabbath day he entered into the synagogue, and taught. 22And they were astonished at his doctrine: for he taught them as one that had authority, and not as the scribes. 23And there was in their synagogue a man with an unclean spirit; and he cried out, 24Saying, Let us alone; what have we to do with thee, thou Jesus of Nazareth? art thou come to destroy us? I know thee who thou art, the Holy One of God. 25And Jesus rebuked him, saying, Hold thy peace, and come out of him. 26And when the unclean spirit had torn him, and cried with a loud voice, he came out of him. 27And they were all amazed, insomuch that they questioned among themselves, saying, What thing is this? what new doctrine is this? for with authority commandeth he even the unclean spirits, and they do obey him. 28And immediately his fame spread abroad throughout all the region round about Galilee. 29And forthwith, when they were come out of the synagogue, they entered into the house of Simon and Andrew, with James and John. 30But Simon’s wife’s mother lay sick of a fever, and anon they tell him of her. 31And he came and took her by the hand, and lifted her up; and immediately the fever left her, and she ministered unto them. 32And at even, when the sun did set, they brought unto him all that were diseased, and them that were possessed with devils. 33And all the city was gathered together at the door. 34And he healed many that were sick of divers diseases, and cast out many devils; and suffered not the devils to speak, because they knew him. 35And in the morning, rising up a great while before day, he went out, and departed into a solitary place, and there prayed. 36And Simon and they that were with him followed after him. 37And when they had found him, they said unto him, All men seek for thee. 38And he said unto them, Let us go into the next towns, that I may preach there also: for therefore came I forth. 39And he preached in their synagogues throughout all Galilee, and cast out devils. 40And there came a leper to him, beseeching him, and kneeling down to him, and saying unto him, If thou wilt, thou canst make me clean. 41And Jesus, moved with compassion, put forth his hand, and touched him, and saith unto him, I will; be thou clean. 42And as soon as he had spoken, immediately the leprosy departed from him, and he was cleansed. 43And he straitly charged him, and forthwith sent him away; 44And saith unto him, See thou say nothing to any man: but go thy way, shew thyself to the priest, and offer for thy cleansing those things which Moses commanded, for a testimony unto them. 45But he went out, and began to publish it much, and to blaze abroad the matter, insomuch that Jesus could no more openly enter into the city, but was without in desert places: and they came to him from every quarter.