Maliro 5 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 5:1-22

1Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;

yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.

2Apereka cholowa chathu kwa obwera,

nyumba zathu kwa alendo.

3Takhala amasiye ndi wopanda abambo,

amayi athu ali ngati akazi amasiye.

4Tiyenera kugula madzi amene timamwa,

nkhuni zathunso nʼzogula.

5Otilondola atigwira pakhosi;

tafowoka ndipo sakutilola kupumula.

6Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya

kuti tipeze chakudya.

7Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,

koma chilango chawo chili pa ife.

8Akapolo akutilamulira,

ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.

9Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe

chifukwa cha lupanga mʼchipululu.

10Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,

chifukwa cha kuwawa kwa njala.

11Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,

ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.

12Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,

akuluakulu sakuwalemekeza.

13Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;

anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.

14Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;

achinyamata aleka nyimbo zawo.

15Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;

kuvina kwathu kwasanduka maliro.

16Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.

Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!

17Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,

chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,

18pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,

nkhandwe zikungoyendayendapo.

19Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;

mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.

20Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?

Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?

21Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;

mukonzenso masiku athu akhale monga akale,

22pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,

ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Плач 5:1-22

Молитва об избавлении

1Вспомни, о Вечный, что случилось с нами,

взгляни и посмотри на бесчестие наше.

2Наследие наше досталось чужим,

дома наши – иноземцам.

3Мы стали сиротами – отца лишились,

матери наши овдовели.

4Воду свою мы пьём за плату,

отдаём деньги за наши же дрова.

5Преследуют нас по пятам,

мы измучены и не находим покоя.

6Мы протягивали руку к Египту и Ассирии,

прося у них хлеба.

7Наши отцы грешили – их уже нет,

а мы несём наказание за их беззакония.

8Рабы господствуют над нами,

и некому вызволить нас из их рук.

9Рискуя своей жизнью, мы добываем хлеб свой,

потому что меч подстерегает нас в пустыне.

10Кожа наша раскалилась от сильного голода,

как будто побывала в печи.

11Женщин бесчестят в Иерусалиме5:11 Букв.: «на Сионе».,

девушек – в городах иудейских.

12Вожди повешены руками захватчиков,

старцев они не уважают.

13Юноши трудятся за жерновами,

и мальчики падают под ношами дров.

14Старцы перестали сидеть у городских ворот,

юноши больше не поют.

15Радость покинула наши сердца,

танцы наши сменились плачем.

16Упал венец с головы нашей;

горе нам, согрешившим!

17Слабеют из-за этого сердца наши,

и мрак затмевает глаза.

18Опустела гора Сион,

и шакалы бродят по ней.

19Ты, о Вечный, – Царь навеки,

престол Твой – из поколения в поколение.

20Почему же Ты до сих пор не вспомнил нас?

Почему оставляешь нас на столь долгое время?

21Верни нас к Себе, Вечный, и мы возвратимся,

обнови наши дни подобно дням, давно миновавшим.

22Или Ты полностью отверг нас,

и гневу Твоему нет меры?