Maliro 4 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 4:1-22

1Haa! Golide wathimbirira,

golide wosalala wasinthikiratu!

Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika

pamphambano ponse pa mzinda.

2Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali

amene kale anali ngati golide,

tsopano ali ngati miphika ya dothi,

ntchito ya owumba mbiya!

3Ngakhale nkhandwe zimapereka bere

kuyamwitsa ana ake,

koma anthu anga asanduka ankhanza

ngati nthiwatiwa mʼchipululu.

4Lilime la mwana lakangamira kukhosi

chifukwa cha ludzu,

ana akupempha chakudya,

koma palibe amene akuwapatsa.

5Iwo amene kale ankadya zonona

akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda.

Iwo amene kale ankavala zokongola

tsopano akugona pa phulusa.

6Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu

kuposa anthu a ku Sodomu,

amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa

popanda owathandiza.

7Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana

ndi oyera kuposa mkaka.

Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi,

maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.

8Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye;

palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda.

Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo;

lawuma gwaa ngati nkhuni.

9Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa

amene anafa ndi njala;

chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda

iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.

10Amayi achifundo afika

pophika ana awo enieni,

ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu

anga anali kuwonongeka.

11Yehova wakwaniritsa ukali wake;

wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa.

Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni

kuti uwononge maziko ake.

12Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire,

kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse,

kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa

pa zipata za Yerusalemu.

13Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake

ndi mphulupulu za ansembe ake,

amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.

14Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda

ngati anthu osaona.

Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi

palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.

15Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!”

“Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!”

Akamathawa ndi kumangoyendayenda,

pakati pa anthu a mitundu yonse amati,

“Asakhalenso ndi ife.”

16Yehova mwini wake wawabalalitsa;

Iye sakuwalabadiranso.

Ansembe sakulandira ulemu,

akuluakulu sakuwachitira chifundo.

17Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana,

chithandizo chosabwera nʼkomwe,

kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu

wa anthu umene sukanatipulumutsa.

18Anthu ankalondola mapazi athu,

choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda.

Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka,

chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.

19Otilondola akuthamanga kwambiri

kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga;

anatithamangitsa mpaka ku mapiri

ndi kutibisalira mʼchipululu.

20Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo,

anakodwa mʼmisampha yawo.

Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake

pakati pa mitundu ya anthu.

21Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu.

Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi.

Koma iwenso chikho chidzakupeza;

udzaledzera mpaka kukhala maliseche.

22Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha;

Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo.

Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu,

ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Плач 4:1-22

Разрушенный Иерусалим

1О, как поблёкло золото!

Как потускнело золото наилучшее!

Драгоценные камни святилища разбросаны

по всем перекресткам улиц.

2Драгоценные сыны Иерусалима4:2 Букв.: «Сиона».

как чистейшее золото ценились,

а теперь они – что глиняная посуда,

изделие рук горшечника.

3Даже шакалы сосцы дают,

чтобы кормить своих детёнышей,

но мой народ стал жесток,

подобно страусам в пустыне4:3 Страусы откладывают свои яйца в песок и бросают их там, совершенно не заботясь о своём потомстве. См. Аюб 39:13-17..

4От жажды язык младенца

прилипает к нёбу его,

дети просят хлеба,

но никто им не даёт.

5Кто привык к изысканным яствам,

выброшен на улицу,

кто в роскоши4:5 Букв.: «на багрянице». Багряница – царское одеяние. воспитан,

копается в кучах мусора.

6Наказание народа моего

превышает наказание Содома4:6 Или: «Грех народа моего превышает грех Содома».,

который был разрушен мгновенно,

и руки человеческие даже не коснулись его4:6 См. Нач. 18:20–19:29..

7Вожди Иерусалима были чище снега,

белее молока,

тела их были румянее кораллов,

на вид были подобны сапфирам.

8А сейчас они чернее копоти,

их не узнают на улицах,

кожа их сморщилась на костях их,

иссохла, словно дерево.

9Те, кто погиб от меча,

счастливее умирающих от голода,

изнемогающих от недостатка полевых плодов.

10Своими руками любящие матери

варили собственных детей;

младенцы стали пищей

во время гибели моего народа.

11Вечный выплеснул всё негодование Своё,

Он излил пылающий гнев Свой

и зажёг в Иерусалиме4:11 Букв.: «на Сионе». огонь,

который пожрал основания его.

12Не верили ни цари земные,

ни все жители мира,

что неприятель войдёт

в ворота Иерусалима.

13Но это случилось из-за грехов его пророков

и беззаконий его священнослужителей,

которые проливали в нём

кровь праведников.

14Теперь они, как слепые, бродят по улицам,

осквернённые кровью,

так что никто не осмеливается прикоснуться к ним.

15«Уходите, нечистые! – кричат им. –

Уходите прочь, не прикасайтесь!»

И тогда они исчезают

и начинают скитаться между народами,

а им и там говорят:

«Вы не можете здесь оставаться».

16Вечный Сам рассеял их,

Он больше не смотрит за ними.

Священнослужителям не оказывают уважения,

и старцам – милости.

17Глаза наши утомились,

напрасно ожидая помощи;

с наших башен мы ожидали народ,

который не мог спасти нас4:17 Иудея ожидала от своего союзника Египта помощи в войне с Вавилоном, но эта помощь так и не пришла (см. Иер. 37:5-7)..

18На каждом шагу подстерегали нас,

так что мы не могли ходить по улицам нашим.

Приблизился наш конец,

число наших дней сочтено:

пришёл наш конец.

19Наши преследователи были

быстрее орлов в небе.

Они гонялись за нами по горам,

подкарауливали нас в пустыне.

20Дыхание нашей жизни –

царь наш, помазанник Вечного4:20 Вероятно, речь идёт о последнем правителе Иудеи, царе Цедекии (см. Иер. 39:4-7; 52:7-11)., –

пойман в их ловушки.

А мы говорили, что под его защитой4:20 Букв.: «под его тенью».

мы будем жить среди народов.

21Радуйся пока и веселись, дочь Эдома4:21 То есть народ Эдома.,

живущая в земле Уц!

Но и до тебя дойдёт чаша,

напьёшься допьяна и обнажишься.

22О дочь Сиона! Наказание твоё скоро закончится,

Вечный не продлит изгнание твоё.

А тебя, дочь Эдома, Он накажет за беззакония твои

и откроет все грехи твои.