Maliro 3 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 3:1-66

1Ine ndine munthu amene ndaona masautso

ndi ndodo ya ukali wake.

2Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa

mu mdima osati mʼkuwala;

3zoonadi anandikantha ndi dzanja lake

mobwerezabwereza tsiku lonse.

4Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga,

ndipo waphwanya mafupa anga.

5Wandizinga ndi kundizungulira

ndi zowawa ndi zolemetsa.

6Wandikhazika mu mdima

ngati amene anafa kale.

7Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe,

wandimanga ndi maunyolo.

8Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo,

amakana pemphero langa.

9Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema;

ndipo wakhotetsa tinjira tanga.

10Wandidikirira ngati chimbalangondo,

wandibisalira ngati mkango.

11Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba,

ndipo wandisiya wopanda thandizo.

12Wakoka uta wake

ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.

13Walasa mtima wanga

ndi mivi ya mʼphodo mwake.

14Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse;

amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.

15Wandidyetsa zowawa

ndipo wandimwetsa ndulu.

16Wathyola mano anga ndi miyala;

wandiviviniza mʼfumbi;

17Wandichotsera mtendere;

ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.

18Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka

ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”

19Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala,

zili ngati zowawa ndi ndulu.

20Ine ndikuzikumbukira bwino izi,

ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.

21Komabe ndimakumbukira zimenezi,

nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.

22Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu,

ndi chifundo chake ndi chosatha.

23Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse;

kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.

24Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse;

motero ndimamuyembekezera.”

25Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye,

kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;

26nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha

Yehova modekha.

27Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli

pamene ali wamngʼono.

28Akhale chete pa yekha,

chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.

29Abise nkhope yake mʼfumbi

mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.

30Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye,

ndipo amuchititse manyazi.

31Chifukwa Ambuye satayiratu

anthu nthawi zonse.

32Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo,

chifukwa chikondi chake ndi chosatha.

33Pakuti sabweretsa masautso mwadala,

kapena zowawa kwa ana a anthu.

34Kuphwanya ndi phazi

a mʼndende onse a mʼdziko,

35kukaniza munthu ufulu wake

pamaso pa Wammwambamwamba,

36kumana munthu chiweruzo cholungama—

kodi Ambuye saona zonsezi?

37Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika

ngati Ambuye sanavomereze?

38Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka

mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?

39Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula

akalangidwa chifukwa cha machimo ake?

40Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu,

ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.

41Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu

kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:

42“Ife tachimwa ndi kuwukira

ndipo inu simunakhululuke.

43“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo

mwatitha mopanda chifundo.

44Mwadzikuta mu mtambo

kotero mapemphero athu sakukufikani.

45Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala

pakati pa mitundu ya anthu.

46“Adani anthu atitsekulira pakamwa.

47Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje,

tapasuka ndi kuwonongedwa.”

48Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe

chifukwa anthu anga akuwonongedwa.

49Misozi idzatsika kosalekeza,

ndipo sidzasiya,

50mpaka Yehova ayangʼane pansi

kuchokera kumwamba ndi kuona.

51Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi

chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.

52Akundisaka ngati mbalame,

amene anali adani anga, popanda chifukwa.

53Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje

ndi kundiponya miyala;

54madzi anamiza mutu wanga

ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.

55Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova,

kuchokera mʼdzenje lozama.

56Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere

kulira kwanga kopempha thandizo.”

57Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani,

ndipo munati, “Usaope.”

58Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga;

munapulumutsa moyo wanga.

59Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira.

Mundiweruzire ndinu!

60Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo,

chiwembu chawo chonse pa ine.

61Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo,

chiwembu chawo chonse pa ine,

62manongʼonongʼo a adani anga

ondiwukira ine tsiku lonse.

63Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira,

akundinyoza mu nyimbo zawo.

64Inu Yehova, muwabwezere chowayenera,

chifukwa cha zimene manja awo achita.

65Phimbani mitima yawo,

ndipo matemberero anu akhale pa iwo!

66Muwalondole mwaukali ndipo

muwawonongeretu pa dziko lapansi.

New International Version

Lamentations 3:1-66

This chapter is an acrostic poem; the verses of each stanza begin with the successive letters of the Hebrew alphabet, and the verses within each stanza begin with the same letter. 1I am the man who has seen affliction

by the rod of the Lord’s wrath.

2He has driven me away and made me walk

in darkness rather than light;

3indeed, he has turned his hand against me

again and again, all day long.

4He has made my skin and my flesh grow old

and has broken my bones.

5He has besieged me and surrounded me

with bitterness and hardship.

6He has made me dwell in darkness

like those long dead.

7He has walled me in so I cannot escape;

he has weighed me down with chains.

8Even when I call out or cry for help,

he shuts out my prayer.

9He has barred my way with blocks of stone;

he has made my paths crooked.

10Like a bear lying in wait,

like a lion in hiding,

11he dragged me from the path and mangled me

and left me without help.

12He drew his bow

and made me the target for his arrows.

13He pierced my heart

with arrows from his quiver.

14I became the laughingstock of all my people;

they mock me in song all day long.

15He has filled me with bitter herbs

and given me gall to drink.

16He has broken my teeth with gravel;

he has trampled me in the dust.

17I have been deprived of peace;

I have forgotten what prosperity is.

18So I say, “My splendor is gone

and all that I had hoped from the Lord.”

19I remember my affliction and my wandering,

the bitterness and the gall.

20I well remember them,

and my soul is downcast within me.

21Yet this I call to mind

and therefore I have hope:

22Because of the Lord’s great love we are not consumed,

for his compassions never fail.

23They are new every morning;

great is your faithfulness.

24I say to myself, “The Lord is my portion;

therefore I will wait for him.”

25The Lord is good to those whose hope is in him,

to the one who seeks him;

26it is good to wait quietly

for the salvation of the Lord.

27It is good for a man to bear the yoke

while he is young.

28Let him sit alone in silence,

for the Lord has laid it on him.

29Let him bury his face in the dust—

there may yet be hope.

30Let him offer his cheek to one who would strike him,

and let him be filled with disgrace.

31For no one is cast off

by the Lord forever.

32Though he brings grief, he will show compassion,

so great is his unfailing love.

33For he does not willingly bring affliction

or grief to anyone.

34To crush underfoot

all prisoners in the land,

35to deny people their rights

before the Most High,

36to deprive them of justice—

would not the Lord see such things?

37Who can speak and have it happen

if the Lord has not decreed it?

38Is it not from the mouth of the Most High

that both calamities and good things come?

39Why should the living complain

when punished for their sins?

40Let us examine our ways and test them,

and let us return to the Lord.

41Let us lift up our hearts and our hands

to God in heaven, and say:

42“We have sinned and rebelled

and you have not forgiven.

43“You have covered yourself with anger and pursued us;

you have slain without pity.

44You have covered yourself with a cloud

so that no prayer can get through.

45You have made us scum and refuse

among the nations.

46“All our enemies have opened their mouths

wide against us.

47We have suffered terror and pitfalls,

ruin and destruction.”

48Streams of tears flow from my eyes

because my people are destroyed.

49My eyes will flow unceasingly,

without relief,

50until the Lord looks down

from heaven and sees.

51What I see brings grief to my soul

because of all the women of my city.

52Those who were my enemies without cause

hunted me like a bird.

53They tried to end my life in a pit

and threw stones at me;

54the waters closed over my head,

and I thought I was about to perish.

55I called on your name, Lord,

from the depths of the pit.

56You heard my plea: “Do not close your ears

to my cry for relief.”

57You came near when I called you,

and you said, “Do not fear.”

58You, Lord, took up my case;

you redeemed my life.

59Lord, you have seen the wrong done to me.

Uphold my cause!

60You have seen the depth of their vengeance,

all their plots against me.

61Lord, you have heard their insults,

all their plots against me—

62what my enemies whisper and mutter

against me all day long.

63Look at them! Sitting or standing,

they mock me in their songs.

64Pay them back what they deserve, Lord,

for what their hands have done.

65Put a veil over their hearts,

and may your curse be on them!

66Pursue them in anger and destroy them

from under the heavens of the Lord.