Maliro 2 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 2:1-22

1Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni

ndi mtambo wa mkwiyo wake!

Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli

kuchoka kumwamba.

Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso

popondapo mapazi ake.

2Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;

mu mkwiyo wake anagwetsa

malinga a mwana wamkazi wa Yuda.

Anagwetsa pansi mochititsa manyazi

maufumu ndi akalonga ake.

3Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola

nyanga iliyonse ya Israeli.

Anabweza dzanja lake lamanja

pamene mdani anamuyandikira.

Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa

umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.

4Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;

wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,

ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.

Ukali wake ukuyaka ngati moto

pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.

5Ambuye ali ngati mdani;

wawonongeratu Israeli;

wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu

ndipo wawononga malinga ake.

Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira

kwa mwana wamkazi wa Yuda.

6Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;

wawononga malo ake a msonkhano.

Yehova wayiwalitsa Ziyoni

maphwando ake oyikika ndi masabata ake.

Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza

mfumu ndi wansembe.

7Ambuye wakana guwa lake la nsembe

ndipo wasiya malo ake opatulika.

Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu

kwa mdani wake;

adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova

ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.

8Yehova anatsimikiza kugwetsa

makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.

Anawayesa ndi chingwe

ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.

Analiritsa malinga ndi makoma;

onse anawonongeka pamodzi.

9Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;

wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.

Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,

palibenso lamulo,

ndipo aneneri ake sakupeza

masomphenya kuchokera kwa Yehova.

10Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni

akhala chete pansi;

awaza fumbi pa mitu yawo

ndipo avala ziguduli.

Anamwali a Yerusalemu

aweramitsa mitu yawo pansi.

11Maso anga atopa ndi kulira,

ndazunzika mʼmoyo mwanga,

mtima wanga wadzaza ndi chisoni

chifukwa anthu anga akuwonongeka,

chifukwa ana ndi makanda akukomoka

mʼmisewu ya mu mzinda.

12Anawo akufunsa amayi awo kuti,

“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”

pamene akukomoka ngati anthu olasidwa

mʼmisewu ya mʼmizinda,

pamene miyoyo yawo ikufowoka

mʼmanja mwa amayi awo.

13Ndinganene chiyani za iwe?

Ndingakufanizire ndi chiyani,

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?

Kodi ndingakufanizire ndi yani

kuti ndikutonthoze,

iwe namwali wa Ziyoni?

Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,

kodi ndani angakuchiritse?

14Masomphenya a aneneri ako

anali abodza ndi achabechabe.

Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo

poyika poyera mphulupulu zako.

Mauthenga amene anakupatsa

anali achabechabe ndi osocheretsa.

15Onse oyenda mʼnjira yako

akukuwombera mʼmanja;

akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola

iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:

“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa

wokongola kotheratu,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”

16Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;

iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,

ndipo akuti, “Tamumeza.

Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;

tili ndi moyo kuti tilione.”

17Yehova wachita chimene anakonzeratu;

wakwaniritsa mawu ake,

amene anatsimikiza kale lomwe.

Wakuwononga mopanda chifundo,

walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,

wakweza mphamvu za adani ako.

18Mitima ya anthu

ikufuwulira Ambuye.

Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,

misozi yako itsike ngati mtsinje

usana ndi usiku;

usadzipatse wekha mpumulo,

maso ako asaleke kukhetsa misozi.

19Dzuka, fuwula usiku,

pamene alonda ayamba kulondera;

khuthula mtima wako ngati madzi

pamaso pa Ambuye.

Kweza manja ako kwa Iye

chifukwa cha miyoyo ya ana ako,

amene akukomoka ndi njala

mʼmisewu yonse ya mu mzinda.

20Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:

kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?

Kodi amayi adye ana awo,

amene amawasamalira?

Kodi ansembe ndi aneneri awaphere

mʼmalo opatulika a Ambuye?

21Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi

pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;

anyamata anga ndi anamwali anga

aphedwa ndi lupanga.

Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;

mwawapha mopanda chifundo.

22Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,

chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.

Pa tsiku limene Yehova wakwiya

palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;

mdani wanga wawononga

onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Lamentaciones 2:1-22

Álef

Este capítulo es un poema acróstico, que sigue el orden del alfabeto hebreo. 1¡Ay, el Señor ha eclipsado a la bella Sión

con la nube de su furor!2:1 ¡Ay … furor! Alt. ¡Cómo el Señor, en su enojo, / ha tratado con reproches a la hija de Sión!

Desde el cielo echó por tierra

el esplendor de Israel;

en el día de su ira se olvidó

del estrado de sus pies.

Bet

2Sin compasión el Señor ha destruido

todas las moradas de Jacob;

en su furor ha derribado

los baluartes de la bella Judá

y ha puesto su honra por los suelos

al derrocar a su rey y a sus príncipes.

Guímel

3Dio rienda suelta a su furor

y deshizo todo el poder2:3 todo el poder. Lit. todo cuerno. de Israel.

Nos vimos frente al enemigo,

y el Señor nos negó su ayuda.2:3 nos negó su ayuda. Lit. retiró su mano derecha.

Ardió en Jacob como un fuego encendido

que consumía cuanto le rodeaba.

Dálet

4Como enemigo, tensó el arco;

lista estaba su mano derecha.

Como enemigo, eliminó

a nuestros seres queridos.

Como fuego, derramó su ira

sobre las tiendas de la bella Sión.

He

5El Señor se porta como enemigo:

ha destruido a Israel.

Ha destruido todos sus palacios

y derribado sus baluartes.

Ha multiplicado el luto y los lamentos

por la bella Judá.

Vav

6Ha desolado su morada como a un jardín;

ha derribado su lugar de reunión.

El Señor ha hecho que Sión olvide

sus fiestas solemnes y sus sábados;

se desató su furia contra el rey

y dejó de lado al sacerdote.

Zayin

7El Señor ha rechazado su altar;

ha abandonado su santuario.

Ha puesto en manos del enemigo

las murallas de sus palacios.

¡Lanzan gritos en la casa del Señor

como en día de fiesta!

Jet

8El Señor decidió derribar

la muralla que rodea a la bella Sión.

Tomó la vara y midió;

destruyó sin compasión.

Hubo lamentos en rampas y muros;

todos ellos se derrumbaron.

Tet

9Las puertas se han desplomado;

él rompió por completo sus cerrojos.

Su rey y sus príncipes

andan entre las naciones;

ya no hay ley ni profetas,

ni visiones de parte del Señor.

Yod

10En la bella Sión, los ancianos

se sientan silenciosos en el suelo;

se echan ceniza sobre la cabeza

y se visten de luto.

Postradas yacen en el suelo

las jóvenes de Jerusalén.

Caf

11El llanto me consume los ojos;

siento una profunda agonía.2:11 siento … agonía. Lit. mis entrañas se agitan.

Estoy con el ánimo2:11 Estoy con el ánimo. Lit. Mi hígado está derramado. por los suelos

porque mi pueblo ha sido destruido.

Niños e infantes desfallecen

por las calles de la ciudad.

Lámed

12«¿Dónde hay pan y vino?»,

preguntan a sus madres

mientras caen por las calles

como heridos de muerte,

mientras en los brazos maternos

exhalan el último suspiro.

Mem

13¿Qué puedo decir de ti, bella Jerusalén?

¿A qué te puedo comparar?

¿Qué ejemplo darte como consuelo,

virginal ciudad de Sión?

Profundas como el mar son tus heridas.

¿Quién podría devolverte la salud?

Nun

14Tus profetas te anunciaron

visiones falsas y engañosas.

No denunciaron tu maldad;

no evitaron tu cautiverio.

Los mensajes que te anunciaban

eran patrañas.

Sámej

15Cuantos pasan por el camino

aplauden burlones al verte.

Ante ti, bella Jerusalén, hacen muecas,

y entre silbidos preguntan:

«¿Es esta la ciudad de belleza perfecta?

¿Es esta la alegría de toda la tierra?»

Pe

16Todos tus enemigos abren la boca

para hablar mal de ti;

rechinando los dientes, declaran burlones:

«Nos la hemos comido viva.

Llegó el día tan esperado;

¡hemos vivido para verlo!»

Ayin

17El Señor ha llevado a cabo sus planes;

ha cumplido su palabra,

que decretó hace mucho tiempo.

Sin piedad, te echó por tierra;

dejó que el enemigo se burlara de ti,

y enalteció el poder2:17 poder. Lit. cuerno. de tus oponentes.

Tsade

18El corazón de la gente

clama al Señor con angustia.

Bella Sión amurallada,

¡deja que día y noche

corran tus lágrimas como un río!

¡No te des un momento de descanso!

¡No retengas el llanto de tus ojos!2:18 no retengas … ojos. Lit. no acalles a la niña de tus ojos.

Qof

19Levántate y clama por las noches,

cuando empiece la vigilancia nocturna.

Deja correr el llanto de tu corazón

como ofrenda derramada ante el Señor.

Eleva tus manos a Dios en oración

por la vida de tus hijos,

que desfallecen de hambre

y quedan tendidos por las calles.

Resh

20«Mira, Señor, y ponte a pensar:

¿A quién trataste alguna vez así?

¿Habrán de comerse las mujeres

a sus hijos, fruto de sus entrañas?

¿Habrán de matar a sacerdotes y profetas

en el santuario del Señor?

Shin

21»Jóvenes y ancianos por igual

yacen en el polvo de las calles;

mis jóvenes y mis doncellas

cayeron a filo de espada.

En tu enojo les quitaste la vida;

¡los masacraste sin piedad!

Tav

22»Como si invitaras a una fiesta solemne,

enviaste contra mí terror de todas partes.

En el día de la ira del Señor,

nadie pudo escapar, nadie quedó con vida.

A mis seres queridos, a los que eduqué,

los aniquiló el enemigo».