Maliro 1 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 1:1-22

1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,

umene kale unali wodzaza ndi anthu!

Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!

Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.

Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,

tsopano wasanduka kapolo.

2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,

misozi ili pa masaya pake.

Mwa abwenzi ake onse,

palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.

Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;

onse akhala adani ake.

3Yuda watengedwa ku ukapolo,

kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.

Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;

ndipo alibe malo opumulira.

Onse omuthamangitsa iye amupitirira,

ndipo alibe kwina kothawira.

4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,

chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.

Zipata zake zonse zili pululu,

ansembe akubuwula.

Anamwali ake akulira,

ndipo ali mʼmasautso woopsa.

5Adani ake asanduka mabwana ake;

odana naye akupeza bwino.

Yehova wamubweretsera mavuto

chifukwa cha machimo ake ambiri.

Ana ake atengedwa ukapolo

pamaso pa mdani.

6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni

wachokeratu.

Akalonga ake ali ngati mbawala

zosowa msipu;

alibe mphamvu zothawira

owathamangitsa.

7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,

Yerusalemu amakumbukira chuma chonse

chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.

Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,

panalibe aliyense womuthandiza.

Adani ake ankamuyangʼana

ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

8Yerusalemu wachimwa kwambiri

ndipo potero wakhala wodetsedwa.

Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,

chifukwa aona umaliseche wake.

Iye mwini akubuwula

ndipo akubisa nkhope yake.

9Uve wake umaonekera pa zovala zake;

iye sanaganizire za tsogolo lake.

Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;

ndipo analibe womutonthoza.

“Inu Yehova, taonani masautso anga,

pakuti mdani wapambana.”

10Adani amulanda

chuma chake chonse;

iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,

amene Inu Mulungu munawaletsa

kulowa mu msonkhano wanu.

11Anthu ake onse akubuwula

pamene akufunafuna chakudya;

asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya

kuti akhale ndi moyo.

“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,

chifukwa ine ndanyozeka.”

12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?

Yangʼanani ndipo muone.

Kodi pali mavuto ofanana ndi

amene andigwerawa,

amene Ambuye anandibweretsera

pa tsiku la ukali wake?

13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,

unalowa mpaka mʼmafupa anga.

Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga

ndipo anandibweza.

Anandisiya wopanda chilichonse,

wolefuka tsiku lonse.

14“Wazindikira machimo anga onse

ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.

Machimowa afika pakhosi panga,

ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.

Iye wandipereka

kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15“Ambuye wakana

anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:

wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,

kuti litekedze anyamata anga;

mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza

anamwali a Yuda.

16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira

ndipo maso anga adzaza ndi misozi.

Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,

palibe aliyense wondilimbitsa mtima.

Ana anga ali okhaokha

chifukwa mdani watigonjetsa.

17“Ziyoni wakweza manja ake,

koma palibe aliyense womutonthoza.

Yehova walamula kuti abale ake

a Yakobo akhale adani ake;

Yerusalemu wasanduka

chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18“Yehova ndi wolungama,

koma ndine ndinawukira malamulo ake.

Imvani inu anthu a mitundu yonse;

onani masautso anga.

Anyamata ndi anamwali anga

agwidwa ukapolo.

19“Ndinayitana abwenzi anga

koma anandinyenga.

Ansembe ndi akuluakulu anga

anafa mu mzinda

pamene ankafunafuna chakudya

kuti akhale ndi moyo.

20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!

Ndikuzunzika mʼkati mwanga,

ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa

chifukwa ndakhala osamvera.

Mʼmisewu anthu akuphedwa,

ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21“Anthu amva kubuwula kwanga,

koma palibe wonditonthoza.

Adani anga onse amva masautso anga;

iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.

Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija

kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;

muwalange

ngati mmene mwandilangira ine

chifukwa cha machimo anga onse.

Ndikubuwula kwambiri

ndipo mtima wanga walefuka.”

Nueva Versión Internacional

Lamentaciones 1:1-22

Álef

Lm 1 Este capítulo es un poema acróstico, que sigue el orden del alfabeto hebreo. 1¡Cuán solitaria se encuentra

la que fue ciudad populosa!

¡Tiene apariencia de viuda

la que fue grande entre las naciones!

¡Hoy es esclava de las provincias

la que fue gran señora entre ellas!

Bet

2Amargamente llora por la noche;

corren las lágrimas por sus mejillas.

No hay entre sus amantes

uno solo que la consuele.

Todos sus amigos la traicionaron;

se volvieron sus enemigos.

Guímel

3En aflicción y con trabajos forzados

Judá marchó al exilio.

Habita entre las naciones

sin encontrar reposo.

Todos sus perseguidores la acosan,

la ponen en aprietos.

Dálet

4Los caminos a Sión están de duelo;

ya nadie asiste a sus fiestas solemnes.

Las puertas de la ciudad se ven desoladas:

sollozan sus sacerdotes,

se turban sus doncellas,

¡toda ella es amargura!

He

5Sus enemigos se volvieron sus amos;

tranquilos se ven sus adversarios.

El Señor la ha acongojado

por causa de sus muchos pecados.

Sus hijos marcharon al cautiverio,

arrastrados por sus enemigos.

Vav

6La hija de Sión ha perdido

todo su esplendor.

Sus príncipes parecen ciervos

que vagan en busca de pastos.

Exhaustos, se dan a la fuga

frente a sus perseguidores.

Zayin

7Jerusalén trae a la memoria los tristes días de su peregrinaje;

se acuerda de todos los tesoros

que en el pasado fueron suyos.

Cuando su pueblo cayó en manos enemigas

nadie acudió en su ayuda.

Sus enemigos vieron su caída

y se burlaron de ella.

Jet

8Grave es el pecado de Jerusalén;

por eso se ha vuelto impura.

Los que antes la honraban ahora la desprecian,

pues han visto su desnudez.

Ella misma gime

y no se atreve a dar la cara.

Tet

9Sus vestidos están llenos de inmundicia;

no tomó en cuenta lo que le esperaba.

Su caída fue sorprendente;

no hubo nadie que la consolara.

«¡Mira, Señor, mi aflicción!

¡El enemigo ha triunfado!».

Yod

10El enemigo se adueñó

de todos sus tesoros.

Ella vio naciones paganas

entrar en su santuario,

a las que tú prohibiste

entrar en tu asamblea.

Caf

11Todo su pueblo solloza

y anda en busca de pan;

para mantenerse con vida

cambian por comida sus tesoros.

«¡Mira, Señor, date cuenta

de cómo me han despreciado!».

Lámed

12«Fíjense ustedes, los que pasan por el camino:

¿Acaso no les importa?

Miren si hay un sufrimiento comparable al mío,

como el que el Señor me ha hecho padecer,

como el que el Señor lanzó sobre mí

en el día de su furor.

Mem

13»Desde lo alto él envió un fuego

que penetró en mis huesos.

A mi paso tendió una trampa

y me hizo retroceder.

Me abandonó por completo;

a todas horas me sentía desfallecer.

Nun

14»Mis pecados fueron atados a un yugo;

sus manos los ataron juntos.1:14 a un yugo; … juntos. Texto de difícil traducción.

Me los ha colgado al cuello,

y ha debilitado mis fuerzas.

Me ha entregado en manos de gente

a la que no puedo ofrecer resistencia.

Sámej

15»En mi ciudad el Señor ha rechazado

a todos los guerreros.

Convocó un ejército contra mí,

para despedazar1:15 Convocó … despedazar. Alt. ha establecido mi tiempo, / cuando él despedazará. a mis jóvenes.

El Señor ha pisado como en un lagar

a la virginal hija de Judá.

Ayin

16»Todo esto me hace llorar;

mis ojos se inundan de lágrimas.

No tengo cerca a nadie que me consuele;

no tengo a nadie que me reanime.

Mis hijos quedaron abandonados

porque el enemigo salió victorioso».

Pe

17Sión clama pidiendo ayuda,1:17 clama pidiendo ayuda. Lit. extiende las manos.

pero no hay quien la consuele.

Por decreto del Señor

los vecinos de Jacob son ahora sus enemigos;

Jerusalén ha llegado a ser

inmundicia en medio de ellos.

Tsade

18«El Señor es justo,

pero yo me rebelé contra su palabra.

Escuchen, todos los pueblos,

y vean mi sufrimiento.

Mis doncellas y mis jóvenes

han marchado al destierro.

Qof

19»Llamé a mis amantes,

pero ellos me traicionaron.

Mis sacerdotes y mis ancianos

perecieron en la ciudad,

mientras buscaban alimentos

para mantenerse con vida.

Resh

20»¡Mírame, Señor, que me encuentro angustiada!

¡Siento una profunda agonía!1:20 ¡Siento … agonía! Lit. Mis entrañas se agitan.

Mi corazón se agita dentro de mí,

pues he sido muy rebelde.

Allá afuera, la espada me deja sin hijos;

dentro de la casa hay ambiente de muerte.

Shin

21»La gente ha escuchado mi gemir,

pero no hay quien me consuele.

Todos mis enemigos conocen mi pesar

y se alegran de lo que has hecho conmigo.

¡Manda ya tu castigo anunciado,

para que sufran lo que he sufrido!

Tav

22»¡Que llegue a tu presencia

toda su maldad!

¡Trátalos como me has tratado a mí

por causa de todos mis pecados!

Son muchos mis quejidos,

y mi corazón desfallece».