1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,
umene kale unali wodzaza ndi anthu!
Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!
Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.
Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,
tsopano wasanduka kapolo.
2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,
misozi ili pa masaya pake.
Mwa abwenzi ake onse,
palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.
Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;
onse akhala adani ake.
3Yuda watengedwa ku ukapolo,
kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.
Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;
ndipo alibe malo opumulira.
Onse omuthamangitsa iye amupitirira,
ndipo alibe kwina kothawira.
4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,
chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.
Zipata zake zonse zili pululu,
ansembe akubuwula.
Anamwali ake akulira,
ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5Adani ake asanduka mabwana ake;
odana naye akupeza bwino.
Yehova wamubweretsera mavuto
chifukwa cha machimo ake ambiri.
Ana ake atengedwa ukapolo
pamaso pa mdani.
6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni
wachokeratu.
Akalonga ake ali ngati mbawala
zosowa msipu;
alibe mphamvu zothawira
owathamangitsa.
7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,
Yerusalemu amakumbukira chuma chonse
chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.
Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,
panalibe aliyense womuthandiza.
Adani ake ankamuyangʼana
ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8Yerusalemu wachimwa kwambiri
ndipo potero wakhala wodetsedwa.
Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,
chifukwa aona umaliseche wake.
Iye mwini akubuwula
ndipo akubisa nkhope yake.
9Uve wake umaonekera pa zovala zake;
iye sanaganizire za tsogolo lake.
Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;
ndipo analibe womutonthoza.
“Inu Yehova, taonani masautso anga,
pakuti mdani wapambana.”
10Adani amulanda
chuma chake chonse;
iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,
amene Inu Mulungu munawaletsa
kulowa mu msonkhano wanu.
11Anthu ake onse akubuwula
pamene akufunafuna chakudya;
asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya
kuti akhale ndi moyo.
“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,
chifukwa ine ndanyozeka.”
12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?
Yangʼanani ndipo muone.
Kodi pali mavuto ofanana ndi
amene andigwerawa,
amene Ambuye anandibweretsera
pa tsiku la ukali wake?
13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,
unalowa mpaka mʼmafupa anga.
Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga
ndipo anandibweza.
Anandisiya wopanda chilichonse,
wolefuka tsiku lonse.
14“Wazindikira machimo anga onse
ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.
Machimowa afika pakhosi panga,
ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.
Iye wandipereka
kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15“Ambuye wakana
anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:
wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,
kuti litekedze anyamata anga;
mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza
anamwali a Yuda.
16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira
ndipo maso anga adzaza ndi misozi.
Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,
palibe aliyense wondilimbitsa mtima.
Ana anga ali okhaokha
chifukwa mdani watigonjetsa.
17“Ziyoni wakweza manja ake,
koma palibe aliyense womutonthoza.
Yehova walamula kuti abale ake
a Yakobo akhale adani ake;
Yerusalemu wasanduka
chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18“Yehova ndi wolungama,
koma ndine ndinawukira malamulo ake.
Imvani inu anthu a mitundu yonse;
onani masautso anga.
Anyamata ndi anamwali anga
agwidwa ukapolo.
19“Ndinayitana abwenzi anga
koma anandinyenga.
Ansembe ndi akuluakulu anga
anafa mu mzinda
pamene ankafunafuna chakudya
kuti akhale ndi moyo.
20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21“Anthu amva kubuwula kwanga,
koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
ndipo mtima wanga walefuka.”
Álef
Lm 1 Este capítulo es un poema acróstico, que sigue el orden del alfabeto hebreo. 1¡Cuán solitaria se encuentra
la que fue ciudad populosa!
¡Tiene apariencia de viuda
la que fue grande entre las naciones!
¡Hoy es esclava de las provincias
la que fue gran señora entre ellas!
Bet
2Amargamente llora por la noche;
corren las lágrimas por sus mejillas.
No hay entre sus amantes
uno solo que la consuele.
Todos sus amigos la traicionaron;
se volvieron sus enemigos.
Guímel
3En aflicción y con trabajos forzados
Judá marchó al exilio.
Habita entre las naciones
sin encontrar reposo.
Todos sus perseguidores la acosan,
la ponen en aprietos.
Dálet
4Los caminos a Sión están de duelo;
ya nadie asiste a sus fiestas solemnes.
Las puertas de la ciudad se ven desoladas:
sollozan sus sacerdotes,
se turban sus doncellas,
¡toda ella es amargura!
He
5Sus enemigos se volvieron sus amos;
tranquilos se ven sus adversarios.
El Señor la ha acongojado
por causa de sus muchos pecados.
Sus hijos marcharon al cautiverio,
arrastrados por sus enemigos.
Vav
6La hija de Sión ha perdido
todo su esplendor.
Sus príncipes parecen ciervos
que vagan en busca de pastos.
Exhaustos, se dan a la fuga
frente a sus perseguidores.
Zayin
7Jerusalén trae a la memoria los tristes días de su peregrinaje;
se acuerda de todos los tesoros
que en el pasado fueron suyos.
Cuando su pueblo cayó en manos enemigas
nadie acudió en su ayuda.
Sus enemigos vieron su caída
y se burlaron de ella.
Jet
8Grave es el pecado de Jerusalén;
por eso se ha vuelto impura.
Los que antes la honraban ahora la desprecian,
pues han visto su desnudez.
Ella misma gime
y no se atreve a dar la cara.
Tet
9Sus vestidos están llenos de inmundicia;
no tomó en cuenta lo que le esperaba.
Su caída fue sorprendente;
no hubo nadie que la consolara.
«¡Mira, Señor, mi aflicción!
¡El enemigo ha triunfado!».
Yod
10El enemigo se adueñó
de todos sus tesoros.
Ella vio naciones paganas
entrar en su santuario,
a las que tú prohibiste
entrar en tu asamblea.
Caf
11Todo su pueblo solloza
y anda en busca de pan;
para mantenerse con vida
cambian por comida sus tesoros.
«¡Mira, Señor, date cuenta
de cómo me han despreciado!».
Lámed
12«Fíjense ustedes, los que pasan por el camino:
¿Acaso no les importa?
Miren si hay un sufrimiento comparable al mío,
como el que el Señor me ha hecho padecer,
como el que el Señor lanzó sobre mí
en el día de su furor.
Mem
13»Desde lo alto él envió un fuego
que penetró en mis huesos.
A mi paso tendió una trampa
y me hizo retroceder.
Me abandonó por completo;
a todas horas me sentía desfallecer.
Nun
14»Mis pecados fueron atados a un yugo;
sus manos los ataron juntos.1:14 a un yugo; … juntos. Texto de difícil traducción.
Me los ha colgado al cuello,
y ha debilitado mis fuerzas.
Me ha entregado en manos de gente
a la que no puedo ofrecer resistencia.
Sámej
15»En mi ciudad el Señor ha rechazado
a todos los guerreros.
Convocó un ejército contra mí,
para despedazar1:15 Convocó … despedazar. Alt. ha establecido mi tiempo, / cuando él despedazará. a mis jóvenes.
El Señor ha pisado como en un lagar
a la virginal hija de Judá.
Ayin
16»Todo esto me hace llorar;
mis ojos se inundan de lágrimas.
No tengo cerca a nadie que me consuele;
no tengo a nadie que me reanime.
Mis hijos quedaron abandonados
porque el enemigo salió victorioso».
Pe
17Sión clama pidiendo ayuda,1:17 clama pidiendo ayuda. Lit. extiende las manos.
pero no hay quien la consuele.
Por decreto del Señor
los vecinos de Jacob son ahora sus enemigos;
Jerusalén ha llegado a ser
inmundicia en medio de ellos.
Tsade
18«El Señor es justo,
pero yo me rebelé contra su palabra.
Escuchen, todos los pueblos,
y vean mi sufrimiento.
Mis doncellas y mis jóvenes
han marchado al destierro.
Qof
19»Llamé a mis amantes,
pero ellos me traicionaron.
Mis sacerdotes y mis ancianos
perecieron en la ciudad,
mientras buscaban alimentos
para mantenerse con vida.
Resh
20»¡Mírame, Señor, que me encuentro angustiada!
¡Siento una profunda agonía!1:20 ¡Siento … agonía! Lit. Mis entrañas se agitan.
Mi corazón se agita dentro de mí,
pues he sido muy rebelde.
Allá afuera, la espada me deja sin hijos;
dentro de la casa hay ambiente de muerte.
Shin
21»La gente ha escuchado mi gemir,
pero no hay quien me consuele.
Todos mis enemigos conocen mi pesar
y se alegran de lo que has hecho conmigo.
¡Manda ya tu castigo anunciado,
para que sufran lo que he sufrido!
Tav
22»¡Que llegue a tu presencia
toda su maldad!
¡Trátalos como me has tratado a mí
por causa de todos mis pecados!
Son muchos mis quejidos,
y mi corazón desfallece».