Malaki 4 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 4:1-6

Tsiku la Yehova

1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi. 2Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola. 3Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.

5“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova. 6Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”

Thai New Contemporary Bible

มาลาคี 4:1-6

วันแห่งองค์พระผู้เป็นเจ้า

1พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสว่า “วันนั้นจะมาถึงอย่างแน่นอน วันที่เผาผลาญดั่งเตาหลอม ทุกคนที่เย่อหยิ่งและทุกคนที่ทำชั่วจะเป็นตอข้าว วันที่จะมาถึงนั้นจะเผาผลาญเขาทั้งหมดไม่ให้เหลือแม้แต่รากหรือกิ่งสักกิ่งเดียว 2แต่พวกเจ้าที่ยำเกรงนามของเรา ดวงตะวันแห่งความชอบธรรมจะขึ้นมาพร้อมด้วยปีกแห่งการบำบัดรักษา และเจ้าจะโลดแล่นออกไปเหมือนลูกวัวที่ถูกปล่อยออกจากคอก 3แล้วเจ้าจะเหยียบย่ำคนชั่ว พวกเขาจะเป็นเหมือนขี้เถ้าใต้ฝ่าเท้าของเจ้าในวันที่เราลงมือทำสิ่งเหล่านี้” พระยาห์เวห์ผู้ทรงฤทธิ์ตรัสดังนั้น

4“จงระลึกถึงบทบัญญัติของโมเสสผู้รับใช้ของเรา คือกฎหมายและบทบัญญัติต่างๆ ซึ่งเรามอบให้โมเสสบนภูเขาโฮเรบสำหรับชนชาติอิสราเอลทั้งปวง

5“ดูเถิด เราจะส่งผู้เผยพระวจนะเอลียาห์มาหาพวกเจ้าก่อนวันอันยิ่งใหญ่น่ากลัวขององค์พระผู้เป็นเจ้าจะมาถึง 6เขาจะหันจิตใจของพ่อมาหาลูกและหันจิตใจของลูกมาหาพ่อ มิฉะนั้นเราจะมาห้ำหั่นดินแดนนี้ด้วยคำสาปแช่ง”