Malaki 4 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 4:1-6

Tsiku la Yehova

1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi. 2Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola. 3Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.

5“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova. 6Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”

Japanese Contemporary Bible

マラキ書 4:1-6

4

さばきと契約の更新

1全能の主はこう宣言します。

「さあ、見よ。

審判の日がくる。かまどのように燃えながら。

高ぶる者、悪を行う者は、わらのように燃えつき、

木のように根も枝もすべて焼き払われる。

2だが、わたしの名を恐れるあなたがたには、

正義の太陽が昇る。その翼によって癒やされる。

あなたがたは自由にされ、

牧場に放された子牛のように喜んで跳びはねる。

3その時あなたがたは、灰を踏みつけるように、

悪者どもを踏みつける。」

全能の主は語ります。

4「わたしがホレブ山(シナイ山)で、

わたしのしもべモーセを通して

全イスラエルに与えた律法を守ることを

忘れてはならない。

5見よ。

わたしは、神の大いなる恐るべき審判の日がくる前に、

エリヤのような預言者を遣わす。

6彼の宣教によって、再び父と子が結び合わされ、

一つ心、一つ思いとされる。

彼らは、もし悔い改めないならわたしが来て、

この地を完全に打ち滅ぼすことを知るからだ。」