1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
2Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa. 3Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo, 4ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
5Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
Kuba za Mulungu
6“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe. 7Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
8“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera.
“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’
“Pa zakhumi ndi pa zopereka. 9Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera. 10Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo. 11Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. 12“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
13Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine.
“Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
14“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse? 15Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’ ”
16Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
17Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira. 18Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
1خداوند قادر متعال میفرمايد: «قاصد خود را میفرستم تا راه را برای من آماده كند. سپس خداوندی كه انتظارش را میكشيد ناگهان به خانهٔ خود خواهد آمد. آن رسولی كه شما مشتاق ديدارش هستيد خواهد آمد و عهد مرا به شما اعلان خواهد كرد.»
2اما كيست كه يارای ايستادن در مقابل او را داشته باشد؟ و كيست كه بتواند آمدنش را تحمل كند؟ زيرا او همچون آتش سوزانی است كه فلز را تصفيه میكند و مثل صابونی است كه كثيفترين لباسها را پاک میكند. 3او مانند كسی كه فلز را تصفيه میكند كاهنان را همچون طلا و نقره پاک خواهد كرد تا آنها با دل پاک هدايا را به خداوند تقديم كنند. 4آنگاه مثل گذشته، خداوند از هدايايی كه مردم يهودا و اورشليم برايش میآورند خشنود خواهد شد.
5خداوند قادر متعال میفرمايد: «من برای داوری به ميان شما خواهم آمد و بر ضد بدكاران شهادت خواهم داد يعنی بر ضد جادوگران، زناكاران و دروغگويان، بر ضد تمام كسانی كه حق كارگران خود را نمیدهند، و كسانی كه به بيوهزنان، يتيمان و غريبان ظلم میكنند و از من نمیترسند.»
دزدی از خدا
6خداوند قادر متعال میفرمايد: «من خداوندی تغييرناپذير هستم. به همين دليل است كه شما، ای نسل يعقوب، تا به حال از بين نرفتهايد. 7هر چند شما هم مثل پدران خود از احكام من سرپيچی نموده، آنها را به جا نياوردهايد، ولی اينک به سوی من بازگشت نماييد و من شما را خواهم بخشيد. میگوييد: مگر ما چه كردهايم كه بايد بازگشت كنيم؟
8«آيا كسی از خدا دزدی میكند؟ ولی شما از من دزدی كردهايد!
«میپرسيد: مقصودت چيست؟
«مقصودم دهيکها و هداياست. 9ای قوم اسرائيل، همهٔ شما ملعون هستيد، زيرا از مال من میدزديد. 10ده يک دارايی خود را به طور كامل به خانهٔ من بياوريد تا خوراک كافی در آنجا باشد. به اين ترتيب مرا امتحان كنيد و ببينيد چگونه روزنههای آسمان را باز میكنم و شما را از بركات خود لبريز میسازم! 11من حشرات و آفات را از زمين شما دور میكنم تا محصولتان از بين نرود و تاكستانهايتان ميوهٔ فراوان بدهند. 12همهٔ قومها شما را خوشبخت خواهند خواند، زيرا صاحب سرزمينی با صفا خواهيد بود.»
13خداوند میفرمايد كه شما بر ضد او سخنان دروغ گفتهايد؛ ولی شما به او میگوييد: «بر ضد تو چه گفتهايم؟»
14-15گفتهايد: «عبادت خدا و اطاعت از او بیفايده است. چرا برای اعمالمان بايد به حضور خداوند برويم و اظهار پشيمانی كنيم؟ ببينيد چطور آدمهای متكبر خوشبخت زندگی میكنند و بدكاران كامياب میشوند و با وجود اينكه مرتكب اعمال زشت میشوند خدا آنها را مجازات نمیكند!»
16آنگاه كسانی كه ترس خداوند را در دل داشتند، با يكديگر به گفتگو نشستند و خداوند به گفتگوی آنان گوش داد و سخنان ايشان را شنيد. سپس در كتابی كه در حضور خداوند بود اسامی كسانی كه ترس خداوند را در دل داشتند و نام او را گرامی میداشتند، نوشته شد. 17خداوند قادر متعال میفرمايد: «در آن روزی كه من تعيين كردهام، آنها قوم خاص من خواهند بود و همانطور كه يک پدر، پسر مطيع خود را میبخشد، من نيز ايشان را خواهم بخشيد. 18آنگاه خواهيد ديد كه خدا با اشخاص خوب و بد، با خدمتگزاران خود و آنانی كه او را خدمت نمیكنند، چگونه رفتار میكند.»