Malaki 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 3:1-18

1Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”

2Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa. 3Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo, 4ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”

Kuba za Mulungu

6“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe. 7Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’

8“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’

“Pa zakhumi ndi pa zopereka. 9Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera. 10Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo. 11Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. 12“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

13Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine.

“Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’

14“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse? 15Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’ ”

16Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.

17Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira. 18Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”

New Russian Translation

Малахия 3:1-18

1– Вот, Я посылаю вестника Моего, и он приготовит путь предо Мной, и внезапно придет в храм Свой Владыка, Которого вы ищете, и Вестник завета, Которого вы желаете. Вот Он идет, – говорит Господь Сил3:1 Эти слова являются пророчеством об Иисусе Христе. По мнению многих толкователей, первый вестник, о котором здесь идет речь, – это Иоанн Креститель (см. Мат. 3; 11:7-15; Лк. 7:24-28)..

2Но кто выдержит день Его прихода? Кто устоит, когда Он явится? Он будет как расплавляющий огонь и как очищающий щелок. 3Он сядет подобно плавильщику, очищающему серебро, очистит левитов и переплавит их, как золото и серебро. Тогда у Господа будут люди, которые станут приносить дары в праведности, 4и дары Иуды с Иерусалимом станут угодны Господу, как в прежние дни, как в минувшие годы.

5– Я приду к вам для суда. Я не замедлю принести свидетельство против чародеев, нарушителей супружеской верности и клятвопреступников, против тех, кто удерживает у батраков заработанное, кто притесняет вдов и сирот, лишает чужеземцев правосудия и не боится Меня, – говорит Господь Сил.

Крадущие у Бога

6– Я, Господь, не изменяюсь. Поэтому и вы, потомки Иакова, не исчезли. 7Со времен ваших отцов вы отворачивались от Моих установлений и не соблюдали их. Вернитесь ко Мне, и Я вернусь к вам, – говорит Господь Сил. – Но вы говорите: «Как нам вернуться?»

8Станет ли человек обкрадывать Бога? А вы обкрадываете Меня. Вы говорите: «Как мы обкрадываем Тебя?» Десятинами и приношениями3:8 По Закону Богу принадлежала десятая часть от всех доходов израильтян. Десятины шли на поддержку левитов и на расходы по содержанию храма (см. Лев. 27:30-33; Чис. 18:21-23; Втор. 14:22-29).. 9Прокляты вы – весь ваш народ – за то, что обкрадываете Меня. 10Принесите десятину в хранилища целиком, чтобы в Моем доме была пища. Испытайте Меня в этом, – говорит Господь Сил, – и посмотрите, не отворю ли Я вам окон неба и не изолью ли благословения на вас так щедро, что у вас не хватит места их вместить? 11Я не дам вредителям пожирать ваш урожай, и с виноградных лоз на ваших полях не опадут плоды, – говорит Господь Сил. – 12Тогда все народы назовут вас счастливыми, потому что ваша земля будет прекрасной, – говорит Господь Сил.

Награда праведным

13Вы произносили жестокие слова против Меня, – говорит Господь. – Но вы говорите: «Что мы сказали против Тебя?» 14Вы говорили: «Служение Богу тщетно. Что мы выгадали, исполняя Его уставы и ходя со скорбными лицами перед Господом Сил? 15Теперь мы считаем счастливыми гордецов. Злодеи не только преуспевают, но и остаются невредимыми, даже когда бросают вызов Богу».

16В то время боящиеся Господа говорили друг с другом. Господь внимал и слушал, и записывалась перед Ним памятная книга о тех, кто боится Господа и размышляет о Его имени.

17– Они будут Моими, – говорит Господь Сил, – Моим драгоценным достоянием в тот день, когда Я буду действовать. Я пощажу их, как отец щадит сына, который ему служит. 18Тогда вы снова увидите разницу между праведником и злодеем, между тем, кто служит Богу, и тем, кто Ему не служит.