Malaki 2 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 2:1-17

Chenjezo kwa Ansembe

1“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.” 2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”

3“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.” 4Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire. 5Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa. 6Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.

7“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse. 8Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. 9“Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”

Kusakhulupirika kwa Yuda

10Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?

11Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo. 12Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.

13China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu. 14Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.

15Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.

16Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.

Tsiku la Chiweruzo

17Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu.

Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?”

Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Малахия 2:1-17

Упрёк священнослужителям

1– Итак, священнослужители, вот повеление для вас: 2если вы не послушаетесь и не положите себе на сердце славить Моё имя, – говорит Вечный, Повелитель Сил, – Я пошлю на вас проклятие и прокляну ваши благословения; истинно, Я уже проклинаю их, потому что вы не положили этого себе на сердце.

3Из-за вас Я накажу ваших потомков. Я забросаю ваши лица навозом ваших праздничных жертв, и вас выбросят вместе с ним2:3 Или: «и прогоню вас от Себя».. 4Вы узнаете, что Я послал вам это повеление, чтобы Моё соглашение с Леви2:4 Род Леви был избран среди всех родов Исраила быть священнослужителями Аллаха (см. Чис. 3:11-13). осталось в силе, – говорит Вечный, Повелитель Сил. – 5Моё соглашение с ним было соглашением, обещавшим жизнь и благоденствие, и Я даровал их ему. Он должен был чтить Меня, и он чтил Меня и благоговел перед именем Моим. 6Он преподавал истинное учение и никогда не говорил лжи. Он жил предо Мной в мире и правде и многих отвратил от греха.

7Священнослужители, ваша обязанность – учить людей знанию Аллаха, и от вас люди должны получать наставление, ведь священнослужитель – посланец Вечного, Повелителя Сил. 8Но вы сами свернули с этого пути и своим учением сбили с него многих. Вы нарушили соглашение Леви, – говорит Вечный, Повелитель Сил, – 9и Я сделал вас презренными и унизил вас перед всем народом за то, что вы не хранили Моих путей и были пристрастны в делах Закона.

Осуждение за смешанные браки и развод

10Разве не один у всех нас Небесный Отец?2:10 Или: «…у всех нас отец». В этом случае здесь может говориться об Ибрахиме или Якубе. Разве не один Бог сотворил нас? Почему же мы вероломны по отношению друг к другу, нарушая соглашение наших предков?

11Иуда нарушил верность. Мерзость была совершена в Исраиле и в Иерусалиме: мужчины Иуды осквернили святилище Вечного, которое Он любит, женившись на женщинах, поклоняющихся чужим богам. 12Да исторгнет Вечный из шатров Якуба всякого поступающего так, кто бы он ни был2:12 Кто бы он ни был – букв.: «бодрствующего и отвечающего»., даже если он приносит жертвы Вечному, Повелителю Сил.

13Вот ещё что вы делаете: вы залили жертвенник Вечного слезами. Вы плачете и сетуете, потому что Он больше не смотрит на ваши дары и не принимает их из ваших рук с благосклонностью. 14Вы спрашиваете: «Почему?» Потому что Вечный – свидетель между тобой и твоей женой, на которой ты женился ещё в юности. Ты был ей неверен, хотя она твоя супруга, твоя законная жена.

15Не Аллах ли сделал их одним целым?2:15 См. Нач. 2:24. И плотью, и духом они принадлежат Ему2:15 Или: «И остаток духа принадлежит Ему».. Почему же Он хочет, чтобы они были едины? Из-за потомства, которое угодно Ему. Смотрите же за собой, и пусть никто не нарушает верности своей жене, на которой женился в юности.

16– Если кто ненавидит свою жену и разводится с ней, – говорит Вечный, Бог Исраила, – тот оскверняет себя2:16 Букв.: «тот покрывает свою одежду скверною».2:16 Или: «Я ненавижу развод, – говорит Вечный, Бог Исраила, – и того, кто виновен в насилии»., – говорит Вечный, Повелитель Сил. – Поэтому наблюдайте за собой и не поступайте вероломно в отношении жены.

Вечный придёт для суда

17Вы утомили Вечного словами.

«Чем же мы Его утомили?» – спрашиваете вы. Тем, что говорите: «Все, кто творит зло, хороши в глазах Вечного. Он доволен ими» – и спрашиваете: «Где же Бог правосудия?»