Malaki 1 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malaki 1:1-14

1Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.

Ndamukonda Yakobo, Ndamuda Esau

2Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’ ”

Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo, 3koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”

4Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.”

Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya. 5Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’

Nsembe Zosayenera

6“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’

7“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe.

“Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’

“Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka. 8Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

9“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.

10“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu. 11Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

12“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’ 13Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova. 14“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’ ”

Japanese Contemporary Bible

マラキ書 1:1-14

1

1これは、神が預言者マラキを通してイスラエルに与えたことばです。

主の愛を疑うイスラエル

2-3「わたしはあなたがたをとても愛してきた」と

主は言います。

ところが、あなたがたは問い返します。

「ほんとうですか。いつ、そうしてくださいましたか。」

主は答えます。

「わたしは、

あなたがたの先祖ヤコブを愛することによって、

あなたがたに対する愛を示した。

そうする理由などなかったのに。

わたしは、ヤコブの兄エサウを退け、

エサウの住む山々と相続地を荒廃させ、

荒野のジャッカルに与えた。

4エサウの子孫が、『廃墟を建て直そう』と言うなら、

全能の主はこう言う。

『建て直したいのなら、建て直すがいい。

わたしは再びそれを打ち壊す。』

彼らの国は『悪の地』と呼ばれ、

彼ら住民も

『神に赦されない者たち』と呼ばれるからだ。」

5さあ、イスラエルよ、目を上げて、

神が世界中でしていることを見なさい。

その時、あなたがたはこう言うようになります。

「ほんとうに神の大いなる御力は、

私たちの国境をはるかに越えている。」

汚れたいけにえによって契約を破る

6「子は父を敬い、召使は主人を敬うものだ。

わたしはあなたがたの父であり、また主人なのに、

あなたがたはわたしを少しも敬わない。

ああ、祭司たちよ、

あなたがたはわたしの名をさげすんでいる。」

「私たちがあなたを?

いつあなたの名をさげすんだというのですか。」

7「わたしの祭壇に、汚れたいけにえをささげるときだ。」

「汚れたいけにえですって?

私たちがいつ、そんなことをしましたか。」

「いつも、あなたがたは言っている。

『わざわざ高価なものを主にささげる必要はない。』

8あなたがたは人々に教えている。

『主の祭壇に足の悪い動物をささげてもよい。

病気の動物や目の見えない動物でもよい。』

これを悪いことではないと言い張るのか。

あなたがたの総督に、同じことをしてみるがよい。

同じような贈り物を贈ってみるがよい。

総督がそれを喜んで受け取るだろうか。

9あなたがたは唱える。

『神よ、あわれんでください。恵みをお与えください。』

しかし、そのようなささげ物を持って来る者に、

どうして好意を示せるというのか。

10ああ、あなたがたの中に、神殿の扉を閉ざして、

このようないけにえを拒絶する祭司が、

一人でもいればいいのだが。

わたしはあなたがたに喜びを感じない。

あなたがたのささげ物は受け取らない。」

主は言います。

11「わたしの名は、外国人の間で

朝から晩まであがめられるようになる。

世界中で人々がわたしの名をあがめ、

かぐわしい香りと、

きよいささげ物をささげるようになる。

国々の間で、わたしの名が大いに高められるからだ。」

主は言います。

12「しかし、あなたがたはわたしをあがめず、

祭壇など大切ではないと言って、

病気にかかった弱々しい動物を

神にささげるよう、人々に教えている。」

主は言います。

13「『ああ、神に仕え、

神の言うとおりにしなければならないとは、

なんとやっかいなことだろう』とあなたがたは言う。

そして神が与え、守るように言われた規則を

気にもかけない。

どういうことなのか。

盗んだ動物や、足の悪い動物や病気の動物を

神へのささげ物とするとは。

わたしはそのようなささげ物を

受け入れなければならないというのか。」

主は問います。

14「神へのいけにえとして、

自分の群れの中から上等の雄羊をささげると

約束しながら、

病気の雄羊を神にささげる者はのろわれよ。

わたしは大いなる王だから。」

全能の主は語ります。

「わたしの名は異邦人の間で、

大いに尊ばれるようになるからだ。」