Machitidwe a Atumwi 9 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 9:1-43

Kutembenuka Mtima kwa Saulo

1Pa nthawi imeneyi, Saulo ankaopsezabe okhulupirira Ambuye nafuna kuwapha. Iye anapita kwa mkulu wa ansembe, 2ndi kukapempha makalata a chilolezo kuti apite nawo ku masunagoge a ku Damasiko, kuti ngati atakapezeka ena kumeneko otsata Njirayo, kaya ndi amuna kapena amayi, akawamange ndi kuwatenga kubwera nawo ku Yerusalemu. 3Akuyandikira ku Damasikoku paulendo wake, mwadzidzidzi kuwala kochokera kumwamba kunamuzungulira iye. 4Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”

5Saulo anafunsa kuti, “Ndinu yani Ambuye?”

Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza.” 6“Tsopano dzuka, lowa mu mzindamo, ndipo udzawuzidwa zoyenera kuchita.”

7Anthu amene anali naye paulendo, anasowa chonena; iwo anamva mawu koma sanaone wina aliyense. 8Saulo anayimirira, ndipo pamene anatsekula maso ake sanathe kuona. Kotero anamugwira dzanja ndi kulowa naye mu Damasiko. 9Anakhala wosaona kwa masiku atatu ndiponso sanadye kapena kumwa kanthu kalikonse.

10Ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Hananiya. Ambuye anamuyitana mʼmasomphenya kuti, “Hananiya!”

Iye anayankha kuti, “Ine Ambuye.”

11Ambuye anamuwuza iye kuti, “Nyamuka, pita ku nyumba ya Yudasi imene ili pa Njira Yolunjika ndipo ukafunse za munthu wochokera ku Tarisisi dzina lake Saulo, pakuti akupemphera. 12Ndipo waona mʼmasomphenya munthu, dzina lake Hananiya atabwera ndi kumusanjika manja kuti aonenso.”

13Hananiya anayankha kuti, “Ambuye, ndinamva zambiri za munthu uyu ndi zonse zoyipa anachitira oyera mtima a ku Yerusalemu. 14Ndipo wabwera kuno ndi ulamuliro wa akulu ansembe kuti adzamange onse amene amayitana pa dzina lanu.”

15Koma Ambuye anati kwa Hananiya, “Pita! Munthu uyu ndi chida changa chosankhika chonyamulira dzina langa pamaso pa anthu a mitundu ina ndi mafumu awo ndiponso kwa anthu a Israeli. 16Ine ndidzamuonetsa zowawa zonse zimene ayenera kumva chifukwa cha dzina langa.”

17Pamenepo Hananiya ananyamuka ndi kukalowa mʼnyumbayo. Anamusanjika manja Sauloyo ndipo anati, “Mʼbale Saulo, Ambuye Yesu, amene anakuonekera pa msewu pamene umabwera kuno wandituma kuti uwonenso ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.” 18Nthawi yomweyo mʼmaso mwa Saulo munachoka zinthu zokhala ngati mamba ansomba, ndipo anayambanso kuona. Iye anayimirira nabatizidwa, 19ndipo atadya chakudya, anapezanso mphamvu.

Saulo Alalikira ku Damasiko

Saulo anakhala masiku angapo ndi ophunzira a ku Damasiko. 20Posakhalitsa anayamba kulalikira mʼsunagoge kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu. 21Onse amene anamva iye akulalikira anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene anayambitsa kuzunza okhulupirira ku mpingo wa ku Yerusalemu? Kodi siwabwera kuno kuti awamange ndi kuwapereka kwa akulu a ansembe?” 22Koma mphamvu za Saulo zinali kukulirakulira ndipo anathetsa nzeru Ayuda okhala ku Damasiko powatsimikizira kuti Yesu ndi Mpulumutsi.

23Patapita masiku ambiri, Ayuda anapangana zoti aphe Saulo, 24koma iye anadziwa za chiwembucho. Anthu ankadikirira usana ndi usiku pa zipata za mzindawo kuti amuphe. 25Koma ophunzira ake anamutenga usiku, namutsitsira kunja kwa mpandawo mʼdengu.

Saulo ku Yerusalemu

26Saulo atafika ku Yerusalemu, anayesetsa kulowa mʼgulu la ophunzira koma onse anamuopa chifukwa sanakhulupirire kuti anali wophunziradi. 27Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa. 28Kotero Saulo anakhala nawo nayendayenda mwaufulu mu Yerusalemu akulalikira molimba mtima mʼdzina la Ambuye. 29Anayankhula ndi kutsutsana ndi Ayuda a Chihelene, koma iwo ankafuna kumupha. 30Abale atadziwa zimenezi, anamutenga Saulo ndi kupita naye ku Kaisareya, ndipo anamutumiza ku Tarisisi.

31Pamenepo mpingo wa ku Yudeya konse, ku Galileya ndi ku Samariya unakhala pamtendere, unalimbikitsidwa; ndi kupatsidwa mphamvu ndi Mzimu Woyera, unakula mʼchiwerengero, ndi kukhala moopa Ambuye.

Eneya ndi Tabita

32Pamene Petro amayendera mpingo, anapita kukachezera oyera mtima a ku Luda. 33Kumeneko anakapeza munthu dzina lake Eneya, wofa ziwalo amene anagona pa mphasa kwa zaka zisanu ndi zitatu. 34Petro anati kwa iye, “Eneya, Yesu Khristu akukuchiritsa iwe, dzuka ndipo yalula mphasa yako.” Nthawi yomweyo Eneya anayimirira. 35Anthu onse amene anakhala ku Luda ndi ku Sharoni anamuona ndipo anatembenukira kwa Ambuye.

36Ku Yopa kunali wophunzira wina dzina lake Tabita (mʼChigriki amati Dorika) amene nthawi zonse ankachita zachifundo ndiponso kuthandiza osauka. 37Nthawi imeneyi anadwala ndipo anamwalira, anasambitsa thupi lake, namugoneka mʼchipinda chammwamba. 38Popeza ku Yopa kunali pafupi ndi Luda; pamene ophunzira anamva kuti Petro anali ku Luda, anatuma anthu awiri kuti akamudandaulire kuti, “Chonde bwerani kuno msanga!”

39Petro ananyamuka, napita nawo, ndipo atafika anamutengera ku chipinda chammwamba. Amasiye onse anayima momuzungulira akulira ndi kumuonetsa mwinjiro ndi zovala zina zimene Dorika ankapanga akanali moyo.

40Petro anatulutsa anthu onse mʼchipindamo; ndipo anagwada pansi ndi kupemphera. Anatembenukira mtembo uja nati, “Tabita, dzuka,” Tabita anatsekula maso ake, ndipo ataona Petro anakhala pansi. 41Petro anamugwira dzanja, namuyimiritsa. Ndipo anayitana okhulupirira ndi amasiye namupereka wamoyo. 42Zimenezi zinadziwika ku Yopa konse, ndipo anthu ambiri anakhulupirira Ambuye. 43Petro anakhala ku Yopa kwa masiku ambiri kwa munthu wina, dzina lake Simoni, mmisiri wa zikopa.

Knijga O Kristu

Djela Apostolska 9:1-43

Savlovo obraćenje

1A Savao, neprestano dišući prijetnjom ubojstva prema Gospodinovim učenicima, ode k velikom svećeniku. 2Zatraži od njega pisma za sinagoge u Damasku da može sve sljedbenike Puta, i muškarce i žene, na koje ondje naiđe, dovesti okovane u Jeruzalem.

3Kad se približio Damasku, odjednom ga obasja svjetlost s neba. 4Padne na zemlju. Začuje nato glas kako mu govori: “Savle, Savle! Zašto me progoniš?”

5“Tko si ti, Gospodine?” upita Savao.

“Ja sam Isus kojega ti progoniš”, odgovori glas. 6“Ustani i pođi u grad! Ondje će ti se reći što da činiš.”

7Savlovi su suputnici ostali bez riječi. Čuli su glas, ali nikoga nisu vidjeli. 8Savao ustane sa zemlje. Oči su mu bile otvorene, ali ništa nije vidio. Povedu ga zato za ruku i uvedu u Damask. 9Tri dana nije ništa vidio niti je jeo i pio.

10A u Damasku je živio vjernik9:10 U grčkome: učenik. U 9:19, 25, 26, 30 i 36 također. imenom Ananija. Njemu Gospodin reče u viđenju: “Ananija!”

“Molim, Gospodine?” odazove se on.

11Gospodin mu reče: “Idi u Ravnu ulicu, u Judinu kuću, i ondje potraži Savla iz Tarza. Eno ga ondje; moli se. 12U viđenju koje sam mu dao vidio je čovjeka imenom Ananija kako ulazi i polaže na njega ruke da progleda.”

13“Ali, Gospodine,” odgovori Ananija, “od tolikih sam čuo da je mnogo zla učinio tvojim svetima u Jeruzalemu! 14Ima punomoć od velikog svećenika da okuje u lance sve koji prizivaju tvoje ime.”

15Gospodin mu odgovori: “Idi i učini što ti kažem. Izabrao sam Savla da ponese moje ime poganima i kraljevima i izraelskome narodu. 16Pokazat ću mu koliko mora pretrpjeti zbog mojega imena.”

17Ananija ode onamo, položi ruke na Savla i reče: “Brate Savle, Gospodin Isus koji ti se ukazao na putu poslao me je da progledaš i da se napuniš Svetoga Duha.” 18Savlu s očiju odmah spadne nešto poput ljuski te progleda. Ustane zatim i krsti se. 19Onda nešto pojede i okrijepi se.

Savao u Damasku i Jeruzalemu

Savao je nekoliko dana ostao s vjernicima u Damasku. 20Smjesta je po sinagogama počeo propovijedati da je Isus Božji Sin.

21Svi koji su ga slušali bili su zaprepašteni. “Pa nije li ovo onaj isti koji je u Jeruzalemu istrebljivao Isusove sljedbenike?” pitali su. “Zar on nije došao ovamo zato da ih uhiti i okovane odvede pred velike svećenike?”

22Savlovo je propovijedanje bivalo sve silnije. Zbunjivao je Židove u Damasku dokazujući im da je Isus Mesija. 23Nakon podosta vremena, židovski ga vođe odluče pogubiti, 24ali Savao dozna za njihovu nakanu. Danonoćno su nadzirali gradska vrata ne bi li ga ubili. 25Zato ga vjernici noću spuste preko gradskoga zida u košari.

26Kad je Savao stigao u Jeruzalem, pokušao se sastati s vjernicima, ali svi su ga se bojali. Nisu vjerovali da je zaista vjernik. 27Tada ga Barnaba povede k apostolima te im ispriča da je Savao na putu u Damask vidio Gospodina i što mu je Gospodin rekao te kako je u Damasku hrabro propovijedao u Isusovo ime. 28Od tada se s njima slobodno družio po Jeruzalemu i hrabro je propovijedao u Gospodnje ime. 29Raspravljao je s nekim Židovima koji su govorili grčki pa ga oni nakane ubiti. 30Kad su vjernici za to čuli, odvedu ga u Cezareju i pošalju doma u Tarz.

31Crkva je u cijeloj Judeji, Galileji i Samariji živjela u miru. Izgrađivala se i napredovala. Vjernici su hodili u strahu Gospodnjemu i u utješeni Svetim Duhom.

Petar iscjeljuje Eneju i Tabitu

32Obilazeći svete posvuda, Petar je došao i k Božjemu narodu u gradu Lidi. 33Ondje upozna nekog čovjeka imenom Eneja, koji je osam godina ležao uzet u postelji. 34Petar mu reče: “Eneja, ozdravlja te Isus Krist! Ustani i namjesti postelju!” Čovjek smjesta ustane. 35Kad su to vidjeli svi žitelji Lide i Šarona, obrate se Gospodinu.

36U Jopi je živjela i vjernica imenom Tabita (što znači: “Košuta”). Život joj se sastojao u tomu da čini dobra i milosrdna djela. 37Upravo se tada ona razboli i umre. Pripremili su ju za pokop i položili ju u sobi na katu. 38Ali kad su čuli da je Petar blizu, u Lidi, pošalju k njemu dvojicu i zamole ga: “Odmah dođi k nama!”

39Petar zato odmah pođe s njima. Čim je stigao povedu ga u sobu na katu. Ondje ga okruže udovice plačući i pokazujući mu ogrtače i drugu odjeću koju im je Košuta izradila dok je bila s njima. 40Ali Petar ih sve pošalje iz sobe. Klekne i pomoli se, a zatim se okrene prema tijelu i reče: “Tabita, ustani!” Ona otvori oči, pogleda Petra i sjedne. 41On joj pruži ruku i pridigne ju. Zatim pozove udovice i svete pa im pokaže da je oživjela.

42Vijest se pronese cijelim gradom te mnogi povjeruju u Gospodina. 43Petar je neko vrijeme ostao u Jopi, u kući nekoga kožara Šimuna.