Machitidwe a Atumwi 8 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 8:1-40

1Ndipo Saulo anavomerezana nawo pa imfa ya Stefano.

Kuzunzika kwa Mpingo

Tsiku lomwelo, mpingo wa mu Yerusalemu unayamba kuzunzidwa, ndipo onse, kupatulapo atumwi, anabalalikira ku madera onse a Yudeya ndi Samariya. 2Anthu okonda Mulungu anayika maliro a Stefano ndipo anamulira kwambiri. 3Koma Saulo anayamba kuwononga mpingo. Amapita nyumba ndi nyumba, ndipo amagwira amuna ndi amayi ndi kukawatsekera ku ndende.

Filipo ku Samariya

4Okhulupirira amene anabalalika amalalikira konse kumene amapita. 5Filipo anapita ku mzinda wa ku Samariya ndipo analalikira za Khristu kumeneko. 6Gulu la anthu litamva Filipo akulalikira komanso kuona zizindikiro zozizwitsa zimene ankazichita, onse anamvetsetsa zimene iye amanena. 7Mizimu yoyipa inatuluka mwa anthu ambiri ikufuwula kwambiri ndipo ambiri amene anali akufa ziwalo ndi olumala anachiritsidwa. 8Kotero munali chimwemwe chachikulu mu mzindawo.

Simoni Wamatsenga

9Koma mu mzindawo munali munthu dzina lake Simoni, amene amachita za matsenga ndi kudabwitsa anthu a mu Samariya. Iye amadzitamandira kuti ndi wopambana, 10ndipo anthu onse, aakulu ndi aangʼono anamumvera ndi kunena kuti, “Munthu uyu ndi mphamvu ya Mulungu yotchedwa Mphamvu yayikulu.” 11Anthu amamutsata chifukwa kwa nthawi yayitali amawadabwitsa ndi matsenga akewo. 12Koma atakhulupirira Filipo akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ndiponso dzina la Yesu Khristu, anthuwo anabatizidwa amuna ndi amayi. 13Nayenso Simoni anakhulupirira ndipo anabatizidwa, natsatira Filipo kulikonse, ndipo anadabwa kwambiri pamene anaona zizindikiro zazikulu ndi zozizwitsa.

14Atumwi a ku Yerusalemu atamva kuti anthu a ku Samariya analandira Mawu a Mulungu, anatumiza Petro ndi Yohane. 15Atafika anawapempherera kuti alandire Mzimu Woyera, 16chifukwa Mzimu Woyera anali asanafike pa wina aliyense wa iwo; anali atangobatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu. 17Ndipo Petro ndi Yohane anasanjika manja awo pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

18Simoni ataona kuti Mzimu anaperekedwa kwa iwo atumwi atawasanjika manja, iye anafuna kuwapatsa ndalama ndipo anati, 19“Inenso ndipatseni mphamvu imeneyi kuti aliyense amene ndimusanjika manja anga azilandira Mzimu Woyera.”

20Petro anayankha kuti, “Ndalama zako utayike nazo pamodzi, chifukwa unaganiza kuti ungathe kugula mphatso ya Mulungu ndi ndalama! 21Ulibe gawo kapena mbali pa utumikiwu, chifukwa mtima wako suli wolungama pamaso pa Mulungu. 22Lapa zoyipa zakozi ndipo upemphere kwa Ambuye. Mwina adzakukhululukira maganizo a mu mtima mwako. 23Pakuti ine ndikuona kuti ndiwe wowawidwa mtima ndiponso kapolo wa tchimo.”

24Ndipo Simoni anayankha, “Mundipempherere kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.”

25Atatha kuchitira umboni ndi kulalikira mawu a Ambuye, Petro ndi Yohane anabwerera ku Yerusalemu, atalalikira Uthenga Wabwino mʼmidzi yambiri ya Asamariya.

Filipo ndi Nduna ya Zachuma ya ku Etiopia

26Mngelo wa Ambuye anati kwa Filipo, “Nyamuka pita chakummwera, ku msewu wa ku chipululu wopita ku Gaza kuchokera ku Yerusalemu.” 27Ndipo ananyamuka napita, ndipo akuyenda anakumana ndi munthu wa ku Etiopia wa udindo waukulu woyangʼanira chuma cha Kandake, mfumu yayikazi ya ku Etiopia. Munthu ameneyu anapita ku Yerusalemu kukapembedza Mulungu, 28ndipo akubwerera kwawo atakwera pa galeta lake amawerenga buku la mneneri Yesaya. 29Mzimu anamuwuza Filipo kuti, “Pita pa galeta ilo ndipo ukakhale pafupi nalo.”

30Pamenepo Filipo anathamangira ku galeta ndipo anamva munthuyo akuwerenga buku la mneneri Yesaya. Filipo anamufunsa kuti, “Kodi mukumvetsa zimene mukuwerengazi?”

31Iye anayankha kuti, “Ndingamvetse bwanji popanda wina wondimasulira?” Ndipo iye anayitana Filipo kuti abwere ndikukhala naye mʼgaleta.

32Mawu amene ndunayo imawerenga anali awa:

“Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira,

kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta,

momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.

33Iye ananyozedwa ndipo panalibe chilungamo pa mlandu wake.

Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake

poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo?”

34Ndunayo inamufunsa Filipo kuti, “Chonde, uzeni, kodi mneneri akuyankhula za ndani, za iye mwini kapena za munthu wina?” 35Pamenepo Filipo anayambira pa malemba omwewo kumuwuza za Uthenga Wabwino wa Yesu.

36Akuyenda mu msewu anafika pamalo pamene panali madzi ndipo ndunayo inati, “Taonani madzi awa. Kodi pali chondiletsa kuti ndibatizidwe?” 37Filipo anati, “Ngati mukhulupirira ndi mtima wanu wonse mukhoza kubatizidwa.” Ndunayo inayankha kuti, “Ine ndikukhulupirira kuti Yesu Khristu ndi Mwana wa Mulungu.” 38Ndipo analamulira galeta kuti liyime. Onse awiriwo, Filipo ndi Ndunayo anatsika ndi kulowa mʼmadzi ndipo Filipo anamubatiza. 39Pamene iwo anatuluka mʼmadzimo, Mzimu wa Ambuye anamukwatula Filipo, ndipo Ndunayo sinamuonenso, koma inapitiriza ulendo wake ikusangalala. 40Koma Filipo anapezeka kuti ali ku Azoto ndipo anazungulira konse, kulalikira Uthenga Wabwino mʼmizinda yonse mpaka anakafika ku Kaisareya.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Деяния 8:1-40

1Шаул же одобрял это убийство.

Гонение и рассеяние верующих

С того дня началось большое гонение на иерусалимскую общину верующих, и все, кроме посланников аль-Масиха, рассеялись по Иудее и Самарии. 2Благочестивые люди похоронили Стефана и горько оплакивали его. 3А Шаул преследовал общину верующих. Он ходил из дома в дом, хватал мужчин и женщин и бросал их в темницу.

Служение Филиппа в Самарии

4Между тем, последователи аль-Масиха, изгнанные из своих мест, возвещали Радостную Весть везде, куда бы они ни приходили. 5Филипп пришёл в один из городов Самарии и возвещал там об аль-Масихе. 6Весь народ внимательно слушал то, что он говорил, и видел знамения, которые он совершал, 7потому что из многих одержимых выходили с громким криком нечистые духи, и многие парализованные и хромые получали исцеление. 8И в городе том была большая радость.

Колдун Шимон

9Был там один человек по имени Шимон, который раньше занимался в этом городе колдовством, изумляя жителей Самарии; сам он выдавал себя за кого-то великого. 10Все люди, и простые, и знатные, слушали его с восхищением, говоря:

– Этот человек – проявление всемогущего Бога, Которого называют Великим.

11А восхищались им потому, что он уже долгое время удивлял людей своим колдовством. 12Но когда жители этого города поверили Филиппу, возвещающему Радостную Весть о Царстве Аллаха и об имени Исы аль-Масиха, то многие мужчины и женщины прошли обряд погружения в воду8:12 Или: «обряд омовения»; также в ст. 13 и 16.. 13Шимон тоже поверил и прошёл обряд погружения. Он повсюду ходил за Филиппом, удивляясь знамениям и великим чудесам.

14Когда посланники аль-Масиха в Иерусалиме услышали о том, что в Самарии приняли слово Аллаха, они послали к ним Петира и Иохана. 15Те пришли и молились, чтобы новообращённые получили Святого Духа, 16потому что ни на кого из них Дух ещё не сошёл, они только прошли обряд погружения в воду в знак единения с Повелителем Исой8:16 Букв.: «во имя Повелителя Исы»; то же в 10:48; 19:5.. 17Затем Петир и Иохан возложили на них руки, и они приняли Святого Духа. 18Когда Шимон увидел, что Дух был дан через возложение рук посланников аль-Масиха, он предложил им деньги, 19говоря:

– Дайте и мне такую силу, чтобы тот, на кого я возложу руки, получал Святого Духа.

20Но Петир ответил:

– Пусть твои деньги погибнут вместе с тобой, раз ты думаешь, что можешь купить дар Аллаха за деньги! 21У тебя нет никакого права участвовать в этом служении, потому что сердце твоё не право перед Аллахом. 22Раскайся в этом зле и молись Вечному Повелителю, может быть, Он простит тебе такие мысли. 23Я вижу, что ты полон горькой желчи и скован цепями греха.

24Шимон ответил:

– Помолитесь обо мне Вечному Повелителю, чтобы со мной не приключилось ничего из сказанного вами.

25Посланники аль-Масиха свидетельствовали и возвещали там слово о Повелителе. Потом они пошли обратно в Иерусалим и по дороге возвещали Радостную Весть во многих самарийских селениях.

Уверование эфиопского евнуха

26Ангел от Вечного сказал Филиппу:

– Ступай на юг, на безлюдную дорогу8:26 Или: «Ступай, в полдень будь на безлюдной дороге»., что ведёт из Иерусалима в Газу.

27Филипп встал и пошёл. В это время там находился эфиопский евнух, придворный кандакии8:27 Кандакия – титул эфиопских цариц (как фараоны в Египте)., то есть царицы эфиопов, заведовавший всей её казной. Он приезжал на поклонение в Иерусалим 28и теперь возвращался домой. Сидя в своей колеснице, он читал пророка Исаию. 29Дух сказал Филиппу:

– Подойди к этой колеснице и иди рядом.

30Филипп подбежал к колеснице и услышал, что в ней читают пророка Исаию.

– Ты понимаешь то, о чём читаешь? – спросил Филипп.

31– Как же мне понять без объяснения? – ответил тот и пригласил Филиппа подняться и сесть с ним.

32А читал он следующее место из Писания:

«Как овца, Он был ведён на заклание,

и как ягнёнок перед стригущим безмолвен,

так и Он не открывал уст Своих.

33Он был унижен и лишён права на справедливый суд.

Кто может рассказать о Его потомках?

Ведь Его жизнь забирается от земли»8:32-33 Ис. 53:7-8..

34Евнух спросил Филиппа:

– Скажи мне, о ком здесь говорит пророк, о себе или о ком-то другом?

35Тогда Филипп стал объяснять, начав с этого места Писания, и рассказал ему Радостную Весть об Исе. 36-37Тем временем они приблизились к какой-то воде.

– Смотри, вот вода, – сказал евнух. – Что мешает мне пройти обряд погружения?8:36-37 Или: «обряд омовения»; также в ст. 38.8:36-37 Некоторые рукописи включают стих 37: «Филипп сказал: „Если ты веришь всем сердцем, то можно“. Евнух сказал: „Я верю, что Иса аль-Масих – Сын Всевышнего“».

38Он приказал остановить колесницу, оба они, Филипп и евнух, вошли в воду, и Филипп совершил над ним обряд погружения. 39А когда они вышли из воды, Дух Вечного Повелителя унёс Филиппа, и евнух его больше не видел. Радостный он продолжал свой путь. 40А Филипп оказался в городе Азоте. Он возвещал Радостную Весть во всех городах, пока не пришёл в Кесарию.