Machitidwe a Atumwi 4 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 4:1-37

Petro ndi Yohane ku Bwalo la Akulu

1Pamene Petro ndi Yohane amayankhula ndi anthu, kunabwera ansembe, mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndiponso Asaduki. 2Iwo anakhumudwa kwambiri chifukwa atumwiwo amaphunzitsa anthu ndi kumalalikira za kuuka kwa akufa mwa Yesu. 3Iwo anagwira Petro ndi Yohane, popeza kunali kutada, anawayika mʼndende mpaka mmawa mwake. 4Koma anthu ambiri amene anamva uthenga anakhulupirira, ndipo chiwerengero cha anthu chinakwana 5,000.

5Mmawa mwake olamulira, akulu ndi aphunzitsi a malamulo anasonkhana mu Yerusalemu. 6Panali Anasi, Mkulu wa ansembe, Kayafa, Yohane ndi Alekisandro ndi ana a banja la mkulu wa ansembe. 7Iwo anayimiritsa Petro ndi Yohane patsogolo pawo nayamba kuwafunsa kuti, “Kodi munachita zimenezi ndi mphamvu yanji kapena mʼdzina la yani?”

8Petro wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anawawuza kuti, “Inu olamulira ndi akulu! 9Ngati ife tikufunsidwa lero chifukwa cha ntchito yabwino imene yachitika pa munthu wolumala miyendo ndi mmene iye anachiritsidwira, 10tsono dziwani izi inu ndi aliyense mu Israeli: munthuyu akuyima pamaso panu, wochiritsidwa kwathunthu, ndi chifukwa cha dzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti amene munamupachika koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. 11Iye ndi

“ ‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana,

umenewo wasanduka mwala wa pa ngodya!’

12Chipulumutso sichipezeka mwa wina aliyense; pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo limene lapatsidwa kwa anthu limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.”

13Ataona kulimba mtima kwa Petro ndi Yohane ndi kuzindikira kuti anali osaphunzira, anthu wamba, anadabwa kwambiri ndipo anazindikira kuti anthuwa anakhala pamodzi ndi Yesu. 14Koma popeza iwo amamuona munthu amene anachiritsidwa atayima pamodzi ndi iwo, palibe chimene akananena. 15Chifukwa chake anawalamula kuti atuluke mʼbwalo la milandu ndipo akulu abwalowo anayamba kukambirana. 16Iwo anafunsana kuti, “Kodi anthuwa tichite nawo chiyani? Pakuti aliyense okhala mu Yerusalemu akudziwa kuti achita chodabwitsachi, ndipo ife sitingathe kukana. 17Koma kuti mbiriyi isapitirire kuwanda pakati pa anthu, ife tiwachenjeze anthu amenewa kuti asayankhulenso kwa wina aliyense mʼdzina la Yesu.”

18Pamenepo anawayitananso ndipo anawalamula kuti asayankhule kapena kuphunzitsa konse mʼdzina la Yesu. 19Koma Petro ndi Yohane anayankha kuti, “Weruzani nokha ngati nʼkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu. 20Ife sitingaleke kuyankhula za zimene tinaziona ndi kuzimva.”

21Atawonjeza kuwaopseza anawamasula. Sanathe kugwirizana njira yowalangira, chifukwa anthu onse amayamika Mulungu chifukwa cha zimene zinachitika. 22Ndipo munthu amene anachiritsidwayo anali ndi zaka makumi anayi.

Okhulupirira Apemphera

23Atamasulidwa Petro ndi Yohane anapita kwa anzawo ndipo anawafotokozera zonse zimene akulu a ansembe ndi akulu anawawuza. 24Anthu atamva zimenezi anafuwula ndi mtima umodzi napemphera kwa Mulungu. Iwo anati, “Ambuye wolamulira zonse, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndiponso zonse zili mʼmenemo. 25Inu munayankhula mwa Mzimu Woyera kudzera pakamwa pa Davide kholo lathu, mtumiki wanu kuti,

“ ‘Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu,

ndipo akonzekera kuchita zopandapake?

26Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.’

27Zoonadi, Herode ndi Pontiyo Pilato anasonkhana pamodzi ndi amitundu ndiponso Aisraeli, mu mzinda muno, kupanga zolimbana ndi mtumiki wanu woyera Yesu, amene Inu munamudzoza. 28Iwo anachita zimene munakonzeratu mwachifuniro chanu ndi mphamvu yanu kuti zichitike. 29Tsopano, Ambuye taonani kuti atiopseza, tithandizeni ife atumiki anu, kuti tiyankhule mawu anu molimba mtima. 30Tambasulani dzanja lanu kuchiritsa anthu ndipo kuti, zizindikiro zodabwitsa zichitike mʼdzina la mtumiki wanu woyera Yesu.”

31Iwo atatha kupemphera, malo amene anasonkhanapo anagwedezeka. Ndipo iwo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo anayankhula Mawu a Mulungu molimba mtima.

Okhulupirira Agawana Zinthu Zawo

32Okhulupirira onse anali a mtima umodzi, ndi maganizo amodzi. Palibe munthu amene amati zomwe anali nazo zinali zake zokha, koma amagawana chilichonse chimene anali nacho. 33Atumwi anapitirira kuchitira umboni mwa mphamvu zakuuka kwa Ambuye Yesu, ndipo pa iwo panali chisomo chochuluka. 34Panalibe anthu osowa kanthu pakati pawo. Pakuti amene anali ndi malo, kapena nyumba amagulitsa ndi kubweretsa ndalamazo 35ndi kuzipereka kwa atumwi, ndipo zimagawidwa kwa aliyense amene anali ndi chosowa.

36Yosefe, wa fuko la Levi, wochokera ku Kupro amene atumwi anamutcha Barnaba, kutanthauza kuti mwana wachilimbikitso, 37anagulitsa munda wake ndipo anadzapereka ndalamazo kwa atumwi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Деяния 4:1-37

Петрус и Иохан перед Высшим Советом

1Пока Петрус и Иохан говорили к народу, к ним подошли священнослужители, начальник храмовой стражи и саддукеи4:1 Саддукеи – аристократическая религиозная партия иудеев, члены которой отвергали идею воскресения мёртвых, не верили в ангелов и в духов. Саддукеи имели огромное влияние в Высшем Совете иудеев., 2которые были крайне возмущены тем, что посланники Масеха учат народ и проповедуют, что как Исо воскрес из мёртвых, так воскреснут и Его последователи4:2 Букв.: «проповедуют в Исо воскресение из мёртвых».. 3Они схватили Петруса и Иохана и, так как уже было поздно, заключили их до утра под стражу. 4Многие же из слышавших Весть поверили, и число братьев возросло примерно до пяти тысяч.

5На следующий день начальники, старейшины и учители Таврота собрались вместе в Иерусалиме. 6Там были верховный священнослужитель Ханан4:6 Ханан был тестем официального верховного священнослужителя Каиафы (18–36 гг.) и сам раньше занимал этот пост (6–15 гг.). Тем не менее Ханан пользовался таким авторитетом у иудеев, что негласно оставался верховным священнослужителем и при своём зяте., Каиафа, Иохан, Искандар и все члены рода верховного священнослужителя. 7Они поставили арестованных посередине и стали допрашивать их:

– Какой силой или от чьего имени вы всё это делаете?

8Тогда Петрус, исполненный Святого Духа, сказал им:

– Начальники народа и старейшины! 9Если вы сегодня требуете от нас ответа за добро, совершённое калеке, и спрашиваете нас, как он был исцелён, 10то знайте, вы и весь народ Исроила: этот человек сейчас стоит перед вами здоровым благодаря имени Исо Масеха из Назарета, Которого вы распяли и Которого Всевышний воскресил из мёртвых! 11Исо и есть тот

«Камень, Который был отвергнут вами, строителями,

и Который стал краеугольным»4:11 Заб. 117:22..

12Ни в ком другом спасения нет, потому что не дано людям никакого другого имени под небом, которым надлежало бы нам спастись4:12 Спастись – от пламени ада (см. Иуда 1:23), от гнева Всевышнего и Его судов (см. Рим. 5:9), от суетной жизни (см. 1 Пет. 1:18), от греха (см. Мат. 1:21) и от дьявола (см. 2 Тим. 2:26)..

13Всех удивляла смелость Петруса и Иохана, ведь было видно, что они люди неучёные и простые. В них узнавали спутников Исо. 14Видя же рядом с ними исцелённого, присутствующие ничего не могли им возразить. 15Тогда они приказали посланникам Масеха покинуть Высший Совет4:15 Высший Совет (букв.: «синедрион») – высший политический, религиозный и судебный орган иудеев. В состав Совета входил семьдесят один человек. и стали совещаться между собой.

16– Что нам делать с этими людьми? – говорили они. – Все жители Иерусалима знают, что они совершили великое чудо, и мы не можем это отрицать. 17Чтобы слух об этом не распространился ещё шире среди народа, давайте пригрозим им, чтобы они никому не говорили от имени Исо4:17 Букв.: «от этого имени». Не называя здесь Исо по имени, предводители иудеев тем самым выказывали своё неуважительное отношение к Нему. То же и в 5:28..

18Они опять велели ввести посланников Масеха и запретили им вообще говорить и учить от имени Исо. 19Но Петрус и Иохан ответили им:

– Посудите сами, справедливо ли перед Всевышним подчиняться вам больше, чем Всевышнему? 20Ведь не можем же мы молчать о том, что мы видели и слышали.

21Члены Высшего Совета, пригрозив посланникам Масеха ещё раз, отпустили их, не найдя возможности наказать, потому что весь народ славил Всевышнего за то, что произошло. 22Ведь человеку, с которым произошло это чудо исцеления, было больше сорока лет.

Молитва верующих

23Когда Петруса и Иохана отпустили, они вернулись к своим и рассказали им обо всём, что им говорили главные священнослужители и старейшины. 24Когда верующие об этом услышали, то они единодушно возвысили голос к Всевышнему и сказали:

– Владыка! Ты создал небо, землю, море и всё, что в них4:24 См. Исх. 20:11; Заб. 145:6.. 25Ты сказал Святым Духом через уста нашего отца и Твоего раба Довуда:

«Зачем гневаются народы,

и племена замышляют пустое?

26Восстают земные цари,

и правители собираются вместе

против Вечного

и против Его Помазанника»4:25-26 Заб. 2:1-2..

27Ведь действительно объединились в этом городе Ирод4:27 Это Ирод Антипа, сын Ирода Великого от сомарянки Малфаки. Он правил Галилеей и Переей с 4 г. до н. э. по 39 г. н. э. и Понтий Пилат с язычниками и с народом Исроила против Твоего святого Раба Исо, которого Ты помазал. 28Они сделали то, что предопределено было Твоей силой и волей. 29И сейчас, Вечный, взгляни на их угрозы и дай Твоим рабам смело возвещать Твоё слово. 30Протяни руку Твою и исцеляй больных, совершай знамения и чудеса именем Твоего святого Раба Исо!

31И когда они помолились, то место, где они находились, сотряслось, и они были исполнены Святого Духа и смело возвещали слово Всевышнего.

Единство и взаимопомощь верующих

32Всё множество уверовавших было едино сердцем и душой. Никто не считал, что его имущество принадлежит лично ему, но всё у них было общее. 33Посланники Масеха продолжали с огромной силой свидетельствовать о воскресении Повелителя Исо, и Всевышний проявлял к ним Свою милость в полной мере. 34Среди них не было ни одного нуждающегося, потому что те, у кого были земли и дома, продавали их, приносили вырученные деньги 35и клали у ног посланников Масеха. Эти деньги распределялись каждому по потребности. 36Например, Юсуф, которого посланники Масеха прозвали Варнавой (что значит «сын утешения»), левит с Кипра, 37владевший участком земли, продал своё поле, принёс деньги и положил у ног посланников Масеха.