Machitidwe a Atumwi 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 3:1-26

Petro Achiritsa Wolumala Miyendo

1Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera nthawi ya 3 koloko masana. 2Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku bwalo la Nyumbayo. 3Ataona Petro ndi Yohane ali pafupi kulowa anawapempha ndalama. 4Iwo anamuyangʼanitsitsa iye. Kenaka Petro anati, “Tiyangʼane!” 5Munthuyo anawayangʼanitsitsa kuyembekezera kuti alandira kanthu kuchokera kwa iwo.

6Petro anati kwa iye, “Ine ndilibe siliva kapena golide, koma chimene ndili nacho ndikupatsa. Mʼdzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti, yenda.” 7Ndipo anamugwira dzanja lamanja, namuthandiza kuti ayimirire ndipo nthawi yomweyo mapazi ake ndi akakolo ake analimba. 8Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka analowa nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu. 9Anthu onse atamuona akuyenda ndiponso kuyamika Mulungu, 10anamuzindikira kuti ndi yemwe uja ankakhala pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola, ndipo anazizwa ndi kudabwa ndi zimene zinamuchitikira.

Petro Ayankhula kwa Anthu

11Wopempha uja akuyenda pamodzi ndi Petro ndi Yohane, anthu onse anadabwa ndipo anawathamangira iwo kumalo wotchedwa Khonde la Solomoni. 12Petro ataona zimenezi anawawuza kuti, “Inu Aisraeli, chifukwa chiyani mukudabwa ndi zimene zachitikazi? Bwanji mukuyangʼana ife ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu yathu kapena chifukwa cha kupembedza kwathu? 13Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, wamulemekeza mtumiki wake Yesu. Amene inu munamukana pamaso pa Pilato ndi kumupereka Iye kuti aphedwe, ngakhale kuti Pilato anafuna kuti amumasule. 14Koma inu munamukana Woyera ndi Wolungamayo ndipo munapempha kuti akumasulireni munthu wakupha anthu. 15Inu munapha mwini moyo, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Ife ndife mboni za zimenezi. 16Mwachikhulupiriro mʼdzina la Yesu, munthu uyu amene mukumuona ndi kumudziwa analimbikitsidwa. Mʼdzina la Yesu ndi chikhulupiriro chimene chili mwa iye chamuchiritsa kwathunthu, monga nonse mukuona.

17“Tsopano abale ine ndikudziwa kuti inu munachita zimenezi mosadziwa, monga momwenso anachitira atsogoleri anu. 18Koma umu ndi mmene Mulungu anakwaniritsira zimene zinanenedwa kale ndi aneneri onse, kuti Khristu adzamva zowawa. 19Chifukwa chake, lapani, bwererani kwa Mulungu, kuti machimo anu afafanizidwe, kuti nthawi ya kutsitsimuka ibwere kuchokera kwa Ambuye, 20ndi kuti Iye atumize Yesu Khristu amene anasankhidwa chifukwa cha inu. 21Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. 22Pakuti Mose anati, ‘Ambuye Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri monga ine kuchokera pakati pa anthu anu; mumvere zonse zimene iye akuwuzeni. 23Aliyense amene sadzamvera mawu a mneneriyo, adzayenera kuchotsedwa pakati pa abale ake.’

24“Ndipo aneneri onse ambiri amene anayankhula kuyambira Samueli, ananeneratu za masiku ano. 25Inu ndinu ana a aneneri ndiponso ana apangano limene Mulungu anachita ndi makolo anu. Iye anati kwa Abrahamu, ‘Anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako.’ 26Pamene Mulungu anaukitsa mtumiki wake, anamutuma Iye poyamba kwa inu kuti akudalitseni pobweza aliyense wa inu ku zoyipa zake.”

New Russian Translation

Деяния 3:1-26

Петр исцеляет нищего калеку

1Однажды в девятый час3:1 То есть в три часа дня., во время молитвы3:1 Во время молитвы – т. е. во время иудейской молитвы «минха». В те времена иудеи трижды молились в определенное время в течение дня: в 9 утра (шахарит), в 3 часа пополудни (минха) и на закате солнца (маарив)., Петр и Иоанн шли в храм. 2В это время туда принесли человека, хромого от рождения. Его каждый день оставляли у ворот, которые назывались Прекрасными, и он просил милостыню у входящих в храм. 3Увидев Петра и Иоанна, которые хотели войти в храм, он попросил и у них. 4Петр и Иоанн пристально посмотрели на него, и Петр сказал:

– Взгляни на нас!

5Человек поднял глаза, ожидая получить от них что-нибудь. 6Но Петр сказал:

– Серебра и золота у меня нет, но то, что есть, я даю тебе. Во имя Иисуса Христа из Назарета – встань и ходи!

7Он взял его за правую руку, помог подняться, и в тот же миг ступни и лодыжки калеки окрепли. 8Он вскочил на ноги и начал ходить. Он вошел с ними в храм, ходил, прыгал и прославлял Бога. 9И все люди видели его ходящим и восхваляющим Бога. 10Они узнавали в нем того человека, который сидел и просил милостыню у Прекрасных ворот храма, и удивлялись тому, что с ним произошло.

Речь Петра в колоннаде Соломона

11Нищий держался за Петра и Иоанна, и весь народ в изумлении окружил их в той части храма, которая называлась колоннадой Соломона. 12Увидев это, Петр обратился к народу:

– Израильтяне, почему вас это так удивляет? Почему вы смотрите на нас так, будто это мы своими силами или благочестием сделали, что этот человек ходит? 13Бог Авраама, Исаака и Иакова, Бог наших отцов3:13 См. Исх. 3:6, 15., прославил Своего Слугу3:13 Слово, стоящее здесь в тексте оригинала, можно перевести и как «ребенок», и как «слуга». Но так как этот стих является аллюзией на Ис. 52:13, где стоит слово, переводимое только как «слуга», то соответственно и здесь должно стоять это слово. Иисуса, Которого вы предали и от Которого отреклись перед Пилатом, хотя тот хотел освободить Его. 14Но вы отреклись от Святого и Праведного и выпросили, чтобы вам освободили убийцу. 15Вы убили Начальника жизни, но Бог воскресил Его из мертвых, и мы этому свидетели. 16Имя Его укрепило этого человека, которого вы видите и знаете, и вера, которая от Него, исцелила его у вас на глазах.

17Братья, я понимаю, что вы и ваши начальники поступили по незнанию. 18Но именно так Бог исполнил то, что Он предсказывал через всех пророков, когда говорил, что Христу предстоят страдания.

19Итак, покайтесь и обратитесь к Богу, чтобы ваши грехи были стерты, 20чтобы от Господа пришли времена обновления и чтобы Он послал предназначенного вам Христа – Иисуса.

21Но Иисус должен оставаться на небесах, пока не наступит время, когда Бог восстановит все, время о котором Он давно возвещал через Своих святых пророков. 22Ведь Моисей сказал:

«Из ваших братьев

Господь, ваш Бог,

поставит вам Пророка, подобного мне.

Вы должны слушать Его во всем,

что бы Он ни сказал вам.

23И всякий, кто не послушает того Пророка,

будет искоренен из народа»3:22-23 См. Втор. 18:15, 18, 19..

24Да и все пророки, которые когда-либо говорили, начиная с Самуила, также предсказывали эти дни. 25Вы же – наследники пророков и наследники завета, который Бог заключил с вашими отцами. Он сказал Аврааму:

«Через твое потомство получат благословение

все народы на земле»3:25 См. Быт. 22:18..

26Когда Бог воскресил Своего Слугу, Он прежде всего послал Его к вам, чтобы благословить вас и призвать каждого из вас отвратиться от ваших злых дел.