Machitidwe a Atumwi 24 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 24:1-27

Felike Amva Mlandu wa Paulo

1Patapita masiku asanu mkulu wa ansembe Hananiya, pamodzi ndi akuluakulu ena ndi katswiri woyankhulira anthu pa milandu wotchedwa Tertuliyo anapita ku Kaisareya ndipo anafotokoza mlandu wa Paulo kwa Bwanamkubwayo. 2Atamuyitana Paulo, ndipo Tertuliyo anafotokozera Felike nkhani yonse ya Paulo. Iye anati, “Wolemekezeka, ife takhala pamtendere nthawi yayitali chifukwa cha inu, ndipo utsogoleri wanu wanzeru wabweretsa kusintha mʼdziko lino. 3Wolemekezeka Felike ife timazilandira zimenezi moyamika kwambiri ponseponse ndi mwa njira iliyonse. 4Koma kuti tisakuchedwetseni, ndikupempha kuti mwa kuleza mtima kwanu mutimvere ife.

5“Ife tapeza kuti munthu uyu amayambitsa mavuto ndi kuwutsa mapokoso pakati pa Ayuda onse a dziko lonse lapansi. Iyeyu ndi mtsogoleri wa mpatuko wa Anazareti. 6Anayesera ngakhale kudetsa Nyumba ya Mulungu wathu. Ndiye ife tinamugwira. 7Koma, mkulu wa asilikali Lusiya anafika mwamphamvu namuchotsa mʼmanja mwathu. 8Ndipo Lusiya analamula kuti amene anali naye ndi mlandu abwere kwa inu. Mukamufunsa ameneyu kwa nokha mudzadziwa choonadi cha zimene ife tikumunenera.”

9Ayuda anavomereza nanenetsa kuti zimenezi zinali zoona.

10Bwanamkubwayo atakodola Paulo ndi kulola kuti ayankhule, Pauloyo anati, “Ine ndikudziwa kuti inu mwakhala mukuweruza dziko lino zaka zambiri, kotero ndikukondwera kuti ndikudziteteza ndekha pamaso panu. 11Inu mukhoza kupeza umboni wake. Sipanapite masiku khumi ndi awiri chipitireni changa ku Yerusalemu kukapembedza. 12Amene akundiyimba mlanduwa sanandipeze mʼNyumba ya Mulungu ndi kutsutsana ndi wina aliyense kapena kuyambitsa chisokonezo mʼsunagoge kapena pena paliponse mu mzindamo. 13Ndipo sangathe kupereka umboni wa mlandu umene akundiyimba inewu. 14Komatu ine ndikuvomera kuti ndimapembedza Mulungu wa makolo athu, monga wotsatira wa Njirayo, imene iwo akuyitchula mpatuko. Ine ndimakhulupirira chilichonse chimene chimagwirizana ndi malamulo ndiponso zimene zinalembedwa ndi Aneneri. 15Ine ndili nacho chiyembekezo chomwecho chimene iwo ali nacho mwa Mulungu, kuti kudzakhala kuuka kwa akufa kwa olungama ndiponso kwa ochimwa. 16Kotero ine ndimayesetsa kuti ndikhale ndi chikumbumtima chosanditsutsa pamaso pa Mulungu ndi anthu onse.

17“Patapita zaka zambiri, ndinabwera ku Yerusalemu kudzapereka mphatso kwa anthu osauka a mtundu wanga komanso kudzapereka nsembe. 18Pamene ndinkachita zimenezi, iwo anandipeza mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nditachita mwambo wodziyeretsa. Panalibe gulu la anthu kapena kuti ndimachita za chisokonezo chilichonse. 19Koma pali Ayuda ena ochokera ku Asiya, amene amayenera kukhala pano pamaso panu, kundiyimba mlandu ngati ali ndi kalikonse konditsutsa ine. 20Kapena awa amene ali panowa anene mlandu umene anapeza mwa ine, pamene ndinayima pamaso pa Bwalo lawo Lalikulu. 21Koma cholakwa changa chingathe kukhala chokhachi chakuti, nditayima pamaso pawo ndinafuwula kuti, ‘Mukundiweruza ine lero chifukwa ndimakhulupirira kuti akufa adzauka.’ ”

22Kenaka Felike, amene amadziwa bwino za Njirayo, anayamba wayimitsa mlanduwo, nati, “Ndidzagamula mlandu wako akabwera mkulu wa asilikali Lusiya.” 23Iye analamulira woyangʼanira asilikali 100 kuti alondere Paulo, koma azimupatsako ufulu ndiponso kulola abwenzi ake kuti adzimusamalira.

24Patapita masiku angapo Felike anabwera pamodzi ndi mkazi wake Drusila, amene anali Myuda. Anayitana Paulo ndipo anamvetsera zimene amayankhula za chikhulupiriro mwa Khristu Yesu. 25Paulo atayankhula za chilungamo, za kudziretsa ndiponso za chiweruzo chimene chikubwera, Felike anachita mantha ndipo anati, “Basi tsopano! Pita. Tidzakuyitanitsa tikadzapeza mpata.” 26Pa nthawi imeneyi amayembekeza kuti Paulo adzamupatsa ndalama, nʼchifukwa chake amamuyitanitsa kawirikawiri ndi kumayankhula naye.

27Patapita zaka ziwiri, Porkiyo Festo analowa mʼmalo mwa Felike, koma anamusiya Paulo mʼndende, chifukwa amafuna kuti Ayuda amukonde.

New Russian Translation

Деяния 24:1-27

Обвинение против Павла

1Пять дней спустя первосвященник Анания с некоторыми старейшинами и юристом Тертуллом пришел в Кесарию, чтобы представить наместнику обвинение против Павла. 2Когда Павла ввели, Тертулл представил обвинение против него:

3– Достопочтеннейший Феликс! Мы всегда и повсюду с глубокой признательностью принимаем твои реформы на благо этого народа и благодарим тебя за тот прочный мир, который установился при твоем разумном правлении. 4Чтобы тебя более не утруждать, я попрошу тебя с твоей обычной добротой выслушать нашу короткую просьбу. 5Мы находим этого человека нарушителем спокойствия, он – зачинщик мятежей среди иудеев по всему миру. Он главарь назорейской секты24:5 Назорейская секта – так противники называли последователей Иисуса, Который был из Назарета. 6и пытался даже осквернить храм. Поэтому мы его арестовали и хотели судить по нашему Закону. 7Но командир римского полка Лисий силой забрал его из наших рук, 8велев его обвинителям идти к тебе24:6-8 Слова «и хотели судить … идти к тебе» отсутствуют в наиболее авторитетных рукописях Писания.. Когда ты допросишь его, ты и сам узнаешь обо всем, в чем мы обвиняем его.

9Прибывшие с ним иудеи поддержали обвинение, заверив, что все сказанное истинно.

Защитная речь Павла перед Феликсом

10Наместник подал знак Павлу, и тот начал защитную речь:

– Мне известно, что ты уже много лет судишь этот народ, и я рад, что мне предоставляется возможность высказаться перед тобой в свою защиту. 11Тебе нетрудно будет удостовериться в том, что не больше двенадцати дней тому назад я пришел на поклонение в Иерусалим. 12Мои обвинители не видели, чтобы я спорил с кем-либо в храме или же возмущал народ в синагогах или в каком-либо другом месте города. 13Они не могут доказать обвинений, которые сейчас выдвигают против меня. 14Но я признаю, что поклоняюсь Богу наших отцов24:14 См. Исх. 3:15. и следую Пути, который мои обвинители называют сектой. Я верю всему, что записано в Законе и у Пророков, 15и у меня такая же надежда на Бога, как и у этих людей – надежда на то, что будет воскресение как праведных, так и неправедных. 16Поэтому я стараюсь, чтобы моя совесть была всегда чиста перед Богом и перед людьми.

17После нескольких лет отсутствия я прибыл в Иерусалим, чтобы передать моему народу пожертвования для бедных и принести жертвы. 18Меня застали в храме, когда я совершал обрядовое очищение. Но там не было никакой толпы и никаких беспорядков, 19пока не пришли несколько иудеев из провинции Азия, которым и следовало бы представить здесь свои обвинения, если у них есть, в чем меня обвинить. 20Или же пусть присутствующие здесь скажут, какую вину они нашли за мной, когда меня допрашивал Высший Совет. 21Может быть, я виновен в том, что выкрикнул там: «Меня судят сегодня перед вами за надежду на воскресение мертвых»?

22Феликс, который был довольно хорошо знаком с Путем, прервал слушание.

– Я вынесу решение по вашему вопросу, когда придет командир полка Лисий, – сказал он.

23Он приказал сотнику содержать Павла под стражей, но предоставить ему некоторую свободу и разрешить его друзьям заботиться о его нуждах.

24Спустя несколько дней Феликс пришел со своей женой – иудеянкой по имени Друзилла – и послал за Павлом, чтобы послушать о его вере в Иисуса Христа. 25Павел говорил о праведности, воздержании и будущем суде. Феликса это испугало, и он сказал:

– Довольно на сегодня! Ступай, но при случае я тебя позову.

26Он также надеялся, что Павел предложит ему взятку, и поэтому часто приказывал привести его и беседовал с ним.

27Прошло два года, и Феликса сменил Порций Фест. Феликс, желая заслужить благосклонность предводителей иудеев, оставил Павла в темнице.