Machitidwe a Atumwi 21 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 21:1-40

Paulo Apita ku Yerusalemu

1Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara. 2Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka. 3Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko. 4Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu. 5Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera. 6Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.

7Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi. 8Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja. 9Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.

10Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu. 11Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’ ”

12Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu. 13Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.” 14Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”

15Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu. 16Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.

Paulo Afika ku Yerusalemu

17Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe. 18Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko. 19Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.

20Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose. 21Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo. 22Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera, 23tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu. 24Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo. 25Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”

26Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.

Agwira Paulo

27Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo, 28akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.” 29Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.

30Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata. 31Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka. 32Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.

33Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani. 34Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali. 35Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo. 36Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”

Paulo Ayankhula

37Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?”

Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki? 38Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”

39Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”

40Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.

Священное Писание

Деяния 21:1-40

Путешествие в Иерусалим

1Расставшись с ними, мы вышли в море и направились прямо на остров Кос. На следующий день мы прибыли на Родос и оттуда отправились в Патару. 2Там мы нашли корабль, направлявшийся в Финикию, сели на него и отправились дальше. 3Мы миновали Кипр, оставив его слева и держа курс на Сирию. Мы пристали к берегу в Тире, потому что там наш корабль должен был оставить груз. 4В Тире мы нашли учеников и пробыли у них семь дней. Они, получив откровение от Духа о предстоящем, начали убеждать Паула не ходить в Иерусалим, 5но когда подошло время, мы отправились дальше. Все ученики, их жёны и дети провожали нас из города, и на берегу мы преклонили колени и молились. 6Попрощавшись с ними, мы сели на корабль, а они возвратились домой.

7Продолжив плавание, мы из Тира прибыли в Птолемаиду. Там мы приветствовали братьев и провели с ними один день. 8А на следующий день мы отправились в путь и пришли в Кесарию и остановились в доме проповедника Радостной Вести Филиппа, одного из семи помощников21:8 См. 6:1-5.. 9У него были четыре незамужних дочери, пророчицы. 10После того как мы пробыли там много дней, из Иудеи пришёл пророк по имени Агав. 11Он подошёл к нам, взял пояс Паула, связал им себе ноги и руки и сказал:

– Святой Дух говорит: «Так иудеи в Иерусалиме свяжут и отдадут в руки язычников того, кому принадлежит этот пояс».

12Услышав это, и мы, и местные стали умолять Паула не ходить в Иерусалим. 13Но Паул на это ответил:

– Зачем вы плачете и разрываете мне сердце? Я готов не только быть связанным, но и умереть в Иерусалиме ради имени Повелителя Исы.

14Когда мы поняли, что он непоколебим в своём решении, мы умолкли, сказав только:

– Пусть свершится воля Вечного Повелителя.

15Затем мы собрались и отправились в Иерусалим. 16С нами пошли некоторые ученики из Кесарии. Они привели нас в дом киприота Мнасона, давнего ученика, у которого мы и остановились.

Паул у Якуба в Иерусалиме

17Когда мы явились в Иерусалим, братья радушно нас приняли. 18На следующий же день Паул вместе с нами пошёл к Якубу21:18 Якуб – единоутробный брат Исы Масиха (см. Мат. 13:55).. Там были все старейшины. 19Паул поприветствовал их и подробно рассказал о том, что Всевышний сделал среди язычников через его служение. 20Они выслушали его и прославили Всевышнего. Затем они сказали Паулу:

– Брат, ты видишь, сколько тысяч иудеев поверили в Ису, и все они ревнители Закона. 21А о тебе они слышали, что ты учишь иудеев, живущих среди язычников, отступлению от Закона Мусы и советуешь не обрезать своих сыновей и вообще не жить по нашим обычаям. 22Что же делать? Они, конечно, услышат о том, что ты пришёл. 23Поэтому сделай, что мы тебе скажем. Среди нас есть четыре человека, принявших обет21:23 Обет – вероятно, это был обет назорейства (см. Чис. 6:1-21).. 24Возьми их, пройди вместе с ними обряд очищения и заплати за них, чтобы они могли обрить головы. Тогда все увидят, что слухи о тебе неверны и что ты живёшь по Закону. 25Что же касается верующих из других народов, то мы написали им о нашем решении: они должны воздерживаться от пищи, принесённой в жертву идолам, от крови, от мяса удушенных животных и от разврата.

26На следующий день Паул взял с собой этих людей и прошёл вместе с ними обряд очищения. Затем он вошёл в храм и объявил, когда очищение будет окончено и когда за каждого из них будет принесена жертва.

Арест Паула

27На исходе семи дней21:27 То есть по окончании ритуального срока очищения (см., напр., Чис. 6:9). несколько иудеев из провинции Азия, увидев Паула в храме, возмутили всю толпу и схватили его 28с криком:

– Исраильтяне! Помогите! Это тот человек, который всех повсюду учит против нашего народа, нашего Закона и нашего храма. Сейчас он к тому же привёл в храм греков, чем и осквернил это святое место.

29До этого в городе они видели Паула вместе с эфесянином Трофимом и предположили, что Паул привёл его в храм.

30Весь город пришёл в смятение, сбежался народ. Паула схватили, выволокли из храма, и ворота храма сразу же были заперты. 31Они уже намеревались убить Паула, но весть о том, что весь Иерусалим охвачен волнением, дошла до командира римского полка. 32Он сразу же, взяв с собой солдат и офицеров, бросился к толпе. Когда иудеи увидели командира полка и его солдат, они перестали избивать Паула. 33Командир, подойдя, арестовал Паула и приказал связать его двумя цепями. Он спрашивал у народа, кто это такой и что он сделал. 34Одни в толпе кричали одно, другие – другое, и так как при таком шуме он не мог понять ничего определённого, то приказал отвести Паула в казармы. 35Когда они были уже на лестнице, толпа стала напирать так, что солдатам пришлось буквально нести Паула. 36Множество народа шло за ними, крича:

– Смерть ему!

Обращение Паула к народу

37Уже перед самым входом в казарму Паул сказал командиру римского полка:

– Можно мне сказать тебе кое-что?

– Ты говоришь по-гречески? – удивился тот. – 38Значит, ты не тот египтянин, который недавно поднял бунт и увёл за собой в пустыню четыре тысячи разбойников?

39Паул ответил:

– Я иудей из Тарса в Киликии, гражданин крупного города. Прошу тебя, разреши мне обратиться к народу.

40Получив разрешение, Паул стал на ступени и жестом призвал народ к тишине. Когда наступила тишина, он заговорил на языке иудеев21:40 То есть или на арамейском, или на древнееврейском языке. См. пояснительный словарь. То же в 26:14.: