Kubwera kwa Mzimu Woyera
1Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi. 2Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala. 3Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo. 4Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi. 6Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana. 7Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya? 8Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo? 9Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya, 10ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma, 11Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.” 12Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
Uthenga wa Petro
14Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena. 15Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa! 16Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17“ ‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza
ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse.
Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera,
anyamata anu adzaona masomphenya,
nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi,
ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo,
ndipo iwo adzanenera.
19Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga
ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano,
ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20Dzuwa lidzadetsedwa
ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi
lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21Ndipo aliyense amene adzayitana
pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa. 23Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda. 24Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa. 25Pakuti Davide ananena za Iye kuti,
“ ‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse.
Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja,
Ine sindidzagwedezeka.
26Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera;
thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda,
kapena kulekerera Woyerayo kuti awole.
28Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo;
Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino. 30Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu. 31Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. 32Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi. 33Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi. 34Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti,
“ ‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti:
Khala kudzanja langa lamanja
35mpaka nditasandutsa adani ako
kukhala chopondapo mapazi ako.’
36“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera. 39Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.” 41Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
Kuyanjana kwa Okhulupirira
42Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera. 43Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita. 44Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse. 45Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake. 46Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona. 47Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.
Сошествие Святого Духа
1Наступил день праздника Жатвы2:1 Праздник Жатвы – иудейский праздник сбора урожая праздновался на пятидесятый день после праздника Освобождения, поэтому он также называется Пятидесятницей., и все ученики были вместе. 2Вдруг с небес послышался звук, напоминающий шум ураганного ветра, который заполнил весь дом, где они сидели. 3Ученики увидели нечто похожее на огненные языки, которые разделились и остановились по одному на каждом из них. 4Все они исполнились Святого Духа и начали говорить на разных языках: эту способность давал им Дух.
5В Иерусалиме в это время находились благочестивые иудеи из разных стран мира. 6На шум собралось много народа; люди недоумевали, потому что каждый из них слышал, как те говорили на языке его страны. 7В большом изумлении они спрашивали:
– Разве все эти люди не галилеяне? 8Как же это каждый из нас слышит их говорящими на языках стран, в которых мы родились? 9Среди нас есть парфяне, мидяне, еламиты, жители Месопотамии, Иудеи и Каппадокии, Понта и провинции Азия2:9 Здесь имеется в виду не материк, а римская провинция на западе Малой Азии (часть территории современной Турции), которая позднее дала своё название материку., 10Фригии и Памфилии, Египта, окрестностей Ливии, прилегающих к городу Кирене, жители Рима, иудеи и обращённые в иудаизм, 11критяне и арабы. И все мы слышим, как они говорят о великих делах Аллаха на наших языках!
12Удивлённые и растерянные, они спрашивали друг друга:
– Что бы это могло значить?
13Некоторые же посмеивались:
– Они напились молодого вина!
Речь Петира перед народом
14Петир поднялся вместе с другими одиннадцатью посланниками аль-Масиха и, обращаясь к народу, громко сказал:
– Иудеи и все жители Иерусалима! Чтобы вам стало понятно, выслушайте внимательно, что я скажу. 15Люди эти не пьяны, как вы думаете: сейчас ведь всего девять часов утра. 16Но это исполняются слова пророка Иоиля:
17«В последние дни, – говорит Аллах, –
Я изолью Духа Моего на всех людей.
Ваши сыновья и дочери будут пророчествовать,
ваши юноши будут видеть видения,
и вашим старцам будут сниться пророческие сны.
18На рабов и на рабынь Моих
Я изолью в те дни Моего Духа,
и они будут пророчествовать.
19Я покажу чудеса в вышине небес
и знамения внизу на земле:
кровь, огонь и клубы дыма.
20Солнце превратится во тьму,
а луна – в кровь
перед тем, как наступит великий и славный день Вечного2:20 Вечный – греческим словом «кюриос», стоящим здесь в оригинальном тексте, в Инджиле переведено еврейское «Яхве». А так как в данном издании Священного Писания «Яхве» переведено как «Вечный», то и его греческий эквивалент переведён так же. Под именем «Яхве» Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь..
21И каждый, кто призовёт имя Вечного,
будет спасён»2:17-21 Иоиль 2:28-32..
22– Исраильтяне, выслушайте, что я вам скажу об Исе из Назарета: могущественные дела, чудеса и знамения Аллаха удостоверили вас в том, что это Он послал Ису. Как вы сами знаете, Аллах совершал всё это через Него у вас на глазах. 23Его, преданного по замыслу и предведению Аллаха, вы, пригвоздив руками беззаконников, убили. 24Но Аллах воскресил Его, освободив из плена смерти, и смерть была не в силах Его удержать.
25Давуд говорит о Нём:
«Всегда Я видел Вечного перед Собой:
Он по правую руку от Меня –
Я не поколеблюсь.
26Поэтому веселится сердце Моё,
и уста полны слов радости,
и даже тело Моё будет жить надеждой.
27Ведь Ты не оставишь Мою душу в мире мёртвых
и не дашь Верному Твоему увидеть тление.
28Ты показал Мне пути жизни;
Ты исполнишь меня радостью,
когда увижу лицо Твоё!»2:25-28 Заб. 15:8-11.
29– Братья, разрешите мне сказать вам прямо, что праотец Давуд умер и был похоронен. Его могила сохранилась у нас до сегодняшнего дня. 30Он был пророком, и, зная, что Аллах клятвенно обещал ему возвести на его престол одного из его потомков2:30 См. 2 Цар. 7:12-13; Заб. 88:4-5; 131:11., 31он, видя будущее, говорил о воскресении аль-Масиха, что Тот не был оставлен в мире мёртвых и Его тело не увидело тления2:31 См. Заб. 15:10.. 32И вот Аллах воскресил Ису, и мы все этому свидетели! 33Он был вознесён и посажен по правую руку от Аллаха и, получив от Небесного Отца обещанного Святого Духа, совершил то, что вы сейчас видите и слышите. 34Ведь Давуд не поднимался на небеса, но он сказал:
«Вечный сказал моему Повелителю:
сядь по правую руку от Меня,
35пока Я не повергну всех врагов Твоих
к ногам Твоим»2:34-35 Заб. 109:1..
36– Поэтому пусть весь дом Исраила будет уверен в том, что Этого Ису, Которого вы распяли, Аллах сделал и Повелителем, и аль-Масихом!
37Когда люди услышали это, их сердца стали терзаться муками совести. Они спрашивали Петира и других посланников аль-Масиха:
– Братья, что нам делать?
38Петир отвечал:
– Покайтесь и пусть каждый из вас пройдёт обряд погружения в воду2:38 Или: «обряд омовения»; также в ст. 41. Смысл обряда заключается в том, что человек оставляет путь греха и встаёт на путь служения Аллаху, войдя в общину последователей Исы аль-Масиха., призывая имя Исы аль-Масиха, для прощения ваших грехов, и вы получите в дар Святого Духа. 39Ведь это обещание относится к вам, вашим детям и к тем, кто вдали: ко всем, кто будет призван Вечным, нашим Богом.
40И многими другими словами Петир увещевал их, говоря:
– Спасайтесь от этого развращённого поколения.
41Те, кто принял его проповедь, прошли через обряд погружения в воду. В тот день к числу уверовавших присоединилось около трёх тысяч человек.
Жизнь верующих
42Верующие твёрдо держались учения посланников аль-Масиха, всегда пребывая в общении, в преломлении хлеба2:42 Имеется в виду участие последователей аль-Масиха в совместной трапезе, во время которой часто совершалось хлебопреломление в воспоминание о жертвенной смерти Исы аль-Масиха за наши грехи согласно Его повелению (см. Лк. 22:14-19). и в молитвах. 43Все были полны трепета перед Аллахом, потому что много чудес и знамений совершалось через посланников аль-Масиха.
44Все верующие были вместе, и всё у них было общее. 45Они продавали свои владения и имущество и раздавали всем, в зависимости от нужды каждого. 46Каждый день они собирались в храме, а по домам ежедневно преломляли хлеб и ели с радостью и искренностью в сердце, 47прославляя Аллаха и пользуясь добрым расположением всего народа. Вечный Повелитель ежедневно прибавлял к ним спасаемых.