Machitidwe a Atumwi 19 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 19:1-41

Paulo ku Efeso

1Apolo ali ku Korinto, Paulo anadutsa mʼmayiko a ku mtunda ndipo anafika ku Efeso. Kumeneko anapeza ophunzira ena. 2Iye anawafunsa kuti, “Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupirira?”

Iwo anayankha kuti, “Ayi, ife sitinamvepo kuti kuli Mzimu Woyera.”

3Tsono Paulo anawafunsa kuti, “Nanga munabatizidwa ndi ubatizo wotani?”

Iwo anati, “Ubatizo wa Yohane.”

4Paulo anati, “Ubatizo wa Yohane unali wa kutembenuka mtima. Iye anawuza anthu kuti akhulupirire amene amabwera, ameneyo ndiye Yesu.” 5Atamva zimenezi, anabatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu. 6Pamene Paulo anawasanjika manja, Mzimu Woyera anadza pa iwo ndipo anayankhula mʼmalilime ndipo ananenera. 7Anthu onsewo analipo khumi ndi awiri.

8Paulo analowa mʼsunagoge ndipo anayankhula molimba mtima kwa miyezi itatu, kuwatsutsa mowakopa za ufumu wa Mulungu. 9Koma ena anawumitsa mitima; anakana kukhulupirira ndipo ananyoza Njirayo pa gulu la anthu. Kotero Paulo anawasiya. Iye anatenga ophunzirawo ndipo amakambirana tsiku ndi tsiku mʼsukulu ya Turano. 10Izi zinachitika kwa zaka ziwiri, kotero kuti Ayuda onse ndi Agriki amene amakhala ku Asiya anamva Mawu a Ambuye.

11Mulungu anachita zodabwitsa zapadera kudzera mwa Paulo. 12Kotero kuti mipango yopukutira thukuta ndi yovala pogwira ntchito, zomwe zinakhudza thupi la Paulo amapita nazo kwa odwala ndipo amachiritsidwa ndiponso mizimu yoyipa mwa iwo imatuluka.

Za Ana a Skeva

13Ayuda ena amene ankayendayenda kutulutsa mizimu yoyipa anayesa kugwiritsa ntchito dzina la Ambuye Yesu pa amene anali ndi ziwanda. Iwo popemphera amati, “Ine ndikulamulira utuluke, mʼdzina la Yesu amene Paulo amamulalikira.” 14Amene ankachita zimenezi anali ana asanu ndi awiri a Skeva, mkulu wa ansembe wa Chiyuda. 15Tsiku lina mzimu woyipa unawayankha kuti, “Yesu ndimamudziwa ndiponso Paulo ndimamudziwa, nanga inu ndinu ndani?” 16Pamenepo munthu amene anali ndi mzimu woyipa anawalumphira nawagwira onse. Iye anawamenya kwambiri, kotero kuti anathawa mʼnyumbamo ali maliseche, akutuluka magazi.

17Ayuda ndi Agriki okhala ku Efeso atamva zimenezi, anachita mantha, ndipo anthu anachitira ulemu dzina la Ambuye Yesu koposa. 18Ambiri a iwo amene tsopano anakhulupirira anafika ndi kuvomereza poyera ntchito zawo zoyipa. 19Ambiri amene amachita za matsenga anasonkhanitsa mabuku awo pamodzi nawatentha pamaso pa anthu onse. Atawonkhetsa mtengo wa mabukuwo, unakwanira ndalama zasiliva 50,000. 20Kotero Mawu a Ambuye anapitirira kufalikira ndipo anagwira ntchito mwamphamvu.

21Zonsezi zitachitika Paulo anatsimikiza zopita ku Yerusalemu kudzera ku Makedoniya ndi ku Akaya. Iye anati, “Kuchokera kumeneko, ndiyenera kukafikanso ku Roma.” 22Iye anatuma anthu awiri amene amamuthandiza, Timoteyo ndi Erasto ku Makedoniya, pamene iye anakhalabe ku Asiya kwa kanthawi.

Chipolowe ku Efeso

23Pa nthawi yomweyo panachitika chipolowe chachikulu chifukwa cha Njira ya Ambuye. 24Mmisiri wantchito zasiliva, dzina lake Demetriyo, amene amapanga mafano asiliva a Atemi ankabweretsa phindu lalikulu kwa amisiri a kumeneko. 25Iye anasonkhanitsa pamodzi amisiriwo, pamodzinso ndi anthu ena ogwira ntchito yomweyo ndipo anati, “Anthu inu, mukudziwa kuti ife timapeza chuma chathu kuchokera pa ntchito imeneyi. 26Ndipo inu mukuona ndi kumva kuti munthu uyu Paulo wakopa ndi kusokoneza anthu ambiri a ku Efeso ndiponso pafupifupi dziko lonse la Asiya. Iye akunena kuti milungu yopangidwa ndi anthu si milungu ayi. 27Choopsa ndi chakuti sikungowonongeka kwa ntchito yathu yokha ayi, komanso kuti nyumba ya mulungu wamkulu wamkazi Atemi idzanyozedwa ndipo mulungu wamkazi weniweniyo amene amapembedzedwa ku Asiya konse ndi dziko lapansi, ukulu wake udzawonongekanso.”

28Atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anayamba kufuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi.” 29Nthawi yomweyo mu mzinda wonse munabuka chipolowe. Anthu anagwira Gayo ndi Aristariko, anzake a Paulo a ku Makedoniya, ndipo anathamangira nawo ku bwalo la masewero. 30Paulo anafuna kulowa pakati pa gulu la anthu, koma ophunzira anamuletsa. 31Ngakhale olamulira ena aderalo, amene anali abwenzi a Paulo, anatumiza uthenga kumuletsa kuti asayesere kulowa mʼbwalomo.

32Munali chisokonezo mʼbwalomo pakuti ena amafuwula zina, enanso zina. Anthu ambiri sanadziwe ngakhale chomwe anasonkhanira. 33Ayuda anamukankhira Alekisandro kutsogolo, ndipo ena anafuwula kumulangiza iye. Iye anatambasula dzanja kuti anthu akhale chete kuti afotokozere anthu nkhaniyo. 34Koma pamene anthuwo anazindikira kuti ndi Myuda, onse pamodzi kwa maora awiri anafuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi wa ku Efeso!”

35Mlembi wa mzindawo anakhazikitsa bata gulu la anthuwo ndipo anati, “Anthu a ku Efeso, kodi ndani pa dziko lonse lapansi amene sadziwa kuti mzinda wa Efeso umayangʼanira nyumba ya mulungu wamkulu Atemi ndi fanizo lake, limene linagwa kuchokera kumwamba? 36Chifukwa chake popeza zinthu izi palibe amene angazikane, inu mukuyenera kukhala chete osachita kanthu kalikonse mofulumira. 37Inu mwabweretsa anthu awa pano, ngakhale kuti iwo sanabe mʼnyumba zathu zamapemphero kapena kunenera chipongwe mulungu wathu wamkazi. 38Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri anzake ali ndi nkhani ndi munthu wina aliyense, mabwalo a milandu alipo, oweruza aliponso. Akhoza kukapereka nkhaniyo kwa oweruza milanduwo. 39Ngati mukufuna kubweretsa kanthu kali konse, ziyenera kukatsimikizidwa ndi bwalo lovomerezeka. 40Monga mmene zililimu, ife titha kuzengedwa mlandu woyambitsa chipolowe chifukwa cha zimene zachitika lerozi. Motero ife sitingathe kufotokoza za chipolowechi popeza palibe nkhani yake.” 41Iye atatha kunena zimenezi anawuza gulu la anthulo kuti libalalike.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

使徒行傳 19:1-41

保羅在以弗所傳道

1亞波羅哥林多時,保羅已取道內陸重回以弗所,在那裡遇見幾個門徒。 2保羅問他們:「你們信的時候有沒有領受聖靈?」

他們說:「沒有!我們從來沒有聽過聖靈的事。」

3保羅說:「那麼,你們受的是什麼洗禮呢?」

他們說:「是約翰的洗禮。」

4保羅說:「約翰的洗禮是悔改的洗禮,約翰告訴百姓要信在他以後來的那位——耶穌。」

5他們聽後,立刻奉主耶穌的名受了洗。 6保羅把手按在他們身上時,聖靈便降在他們身上,他們就說方言,講上帝的信息。 7這次共有十二個人。

8保羅一連三個月勇敢地在會堂裡傳道,與人辯論上帝國的事,勸導他們。 9可是有些人仍然頑固不信,還當眾毀謗上帝的道。保羅便帶著門徒離開他們,天天在推喇奴的學堂辯論。 10這樣持續了兩年,亞細亞全境的居民,無論是猶太人還是希臘人,都聽見了主的道。 11上帝又藉著保羅的手行了一些非凡的神蹟, 12甚至只要將保羅身上的手帕或圍裙放在病人身上,病人就痊癒了,邪靈也會離開所附的人。

13那時,有幾個走江湖的猶太術士也想用耶穌的名趕鬼,他們向那些被邪靈附身的人說:「我奉保羅所傳講的耶穌之名,命令你們出來!」 14做這事的有猶太祭司長士基瓦的七個兒子。

15邪靈回答說:「耶穌,我認識;保羅,我也知道。但你們是誰?」 16被邪靈附身的人隨即撲向他們,攻擊他們,制伏了他們,使他們赤著身子帶著傷從屋裡逃走了。

17以弗所猶太人和希臘人知道了這件事,都驚懼不已。主耶穌的名因此大受尊崇。 18許多已經信耶穌的人都前來認罪,公開承認自己的惡行。 19又有許多行邪術的人把他們的書堆在一起,當眾焚燒。根據當時的估價,這些書約值五萬銀幣。 20主的道就這樣傳開了,大大興旺起來。

21這些事以後,保羅決定經過馬其頓亞該亞回到耶路撒冷。他說:「到了那裡之後,我必須去羅馬看看。」 22於是,他派提摩太以拉都兩位同工先去馬其頓,自己暫時留在亞細亞

以弗所的騷亂

23就在這時,由於主的道,以弗所又起了很大的騷亂。 24一個名叫底米丟的銀匠以製造亞底米女神銀龕為業,使從事這門生意的工匠獲利豐厚。 25他召集了工匠和同行的人,說:「各位都知道我們靠這一行發財, 26可是你們都看到了,也聽見了,那個保羅以弗所亞細亞全境說服、誤導了許多人,說什麼人手所造的不是神。 27這樣下去,不但我們的行業會遭人貶抑,連亞底米女神廟也會被人輕看,甚至全亞細亞及普世尊崇的女神也會威嚴掃地!」

28眾人聽後,怒氣填胸,高聲喊叫:「以弗所人的亞底米女神真偉大!」 29全城陷入一片混亂。眾人抓住保羅的兩個同伴——馬其頓該猶亞里達古,拖著他們衝進戲院。 30保羅想進去,但門徒不許他去。 31他的好友——亞細亞的幾位官員也派人勸他別冒險進入戲院。

32這時,戲院裡面的人都在大喊大叫,混亂不堪。其實大部分人根本不知道自己為什麼聚在那裡。 33這時,人群中的猶太人把亞歷山大推到前面,請他解釋。亞歷山大舉手示意大家安靜,聽他發言。 34但眾人認出他是個猶太人,便又開始一起高呼:「以弗所人的亞底米女神真偉大!」這樣喊了兩個小時。

35最後,城裡的書記官出面調停,說:「各位以弗所市民,誰不知道以弗所城守護著亞底米女神廟和從宙斯那裡掉下來的神像呢? 36既然這是無可否認的事實,你們就該安靜,不可魯莽行事。 37你們帶來的這些人既沒有偷廟裡的東西,也沒有褻瀆我們的女神。 38如果底米丟和他的同行要控告誰,大可到法庭或總督那裡提出訴訟。 39倘若你們還有其他的要求,也可以通過合法的會議解決。 40今天的騷亂實在沒有道理,難免會被查問,到時候我們很難交代。」 41說完,便叫眾人散去。