Machitidwe a Atumwi 17 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 17:1-34

Paulo ku Tesalonika

1Atadutsa ku Amfipoli ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge ya Ayuda. 2Paulo, monga mwachizolowezi chake, analowa mʼsunagoge, ndipo anakambirana nawo Mawu a Mulungu kwa masabata atatu, 3kuwafotokozera ndi kuwatsimikizira kuti Khristu anayenera kufa ndi kuuka. Iye anati, “Yesu amene ndikukulalikirani ndiye Khristu.” 4Ena mwa Ayuda anakopeka mtima ndipo anatsatira Paulo ndi Sila, monganso linachitira gulu lalikulu la Agriki woopa Mulungu, pamodzi ndi amayi odziwika ambiri.

5Koma Ayuda ena anachita nsanje; kotero anasonkhanitsa anthu akhalidwe loyipa ochokera pa msika ndipo napanga gulu nayambitsa chipolowe mu mzindawo. Anathamangira ku nyumba ya Yasoni kukafuna Paulo ndi Sila kuti awabweretse pa gulu la anthu. 6Koma atalephera kuwapeza, anakokera Yasoniyo ndi abale ena ku bwalo la akulu a mzindawo akufuwula kuti, “Anthu awa, Paulo ndi Sila, amene akhala akusokoneza dziko lonse lapansi, tsopano afikanso kuno. 7Yasoni ndiye anawalandira mʼnyumba mwake. Onsewa akuchita zotsutsana ndi malamulo a Kaisara pomanena kuti palinso mfumu ina, yotchedwa Yesu.” 8Atamva zimenezi, gulu la anthu ndi akulu a mzinda anavutika mu mtima. 9Iwo analipiritsa Yasoni ndi anzakewo ndipo anawamasula.

Ku Bereya

10Mdima utagwa, abale anatumiza Paulo ndi Sila ku Bereya. Atafika kumeneko anapita ku sunagoge ya Ayuda. 11Tsopano anthu a ku Bereya anali akhalidwe labwino kusiyana ndi Atesalonika, pakuti iwo analandira mawu ndi chidwi chachikulu ndipo ankasanthula Malemba tsiku ndi tsiku kuti aone ngati zimene ankanena Paulozo zinali zoona. 12Ayuda ambiri anakhulupirira, monga anachitiranso amayi ndi amuna ambiri odziwika a Chigriki.

13Ayuda a ku Tesalonika atadziwa kuti Paulo akulalikira Mawu a Mulungu ku Bereya, anapitanso kumeneko, ndi kuwutsa mitima ya anthu nayambitsa chisokonezo. 14Nthawi yomweyo abale anatumiza Paulo ku nyanja koma Sila ndi Timoteyo anatsalira ku Bereya. 15Anthu amene anamuperekeza Paulo nafika naye ku Atene, ndipo anabwerera ku Bereya atawuzidwa kuti Sila ndi Timoteyo amutsatire msanga.

Ku Atene

16Paulo akudikira Timoteyo ndi Sila ku Atene, anavutika mu mtima kwambiri poona kuti mzindawo unali odzaza ndi mafano. 17Tsono anakambirana ndi Ayuda ndi Agriki amene amaopa Mulungu mʼsunagoge, komanso anthu amene amapezeka pa msika tsiku ndi tsiku ndi ena amene amakumana nawo. 18Gulu la Aepikureya ndi Astoiki, anthu anzeru, anayamba kutsutsana naye. Ena a iwo anafunsa kuti, “Kodi wolongololayu akufuna kunena chiyani?” Enanso anati, “Akuoneka ngati akulalikira milungu yachilendo.” Iwo ananena zimenezi chifukwa Paulo amalalikira Uthenga Wabwino wa Yesu ndi kuuka kwa akufa. 19Kenaka iwo anamutenga nafika naye ku bwalo la Areopagi kumene anamufunsa kuti, “Kodi tingadziweko chiphunzitso chatsopano chimene ukuchifotokozachi? 20Iwe ukubweretsa zinthu zina zachilendo mʼmakutu mwathu, ndipo ife tikufuna tidziwe tanthauzo lake.” 21Atene onse ndi alendo amene amakhala kumeneko samachita kanthu kena koma kufotokoza ndi kumvera fundo zatsopano.

22Paulo anayimirira mʼbwalo la Areopagi nati: “Inu anthu a ku Atene! Ine ndikuona kuti mʼnjira zonse ndinu opembedza kwambiri. 23Pakuti pamene ndimayenda ndi kuona zinthu zimene mumazipembedza, ndapezanso guwa lansembe lolembedwapo kuti, kwa mulungu wosadziwika. Tsopano chimene mumachipembedza osachidziwa ndi chimene ndikuchilalikira.

24“Mulungu amene analenga dziko lapansi ndiponso zonse zili mʼmenemo ndiye Ambuye wakumwamba ndi dziko lapansi ndipo sakhala mʼnyumba zachipembedzo zomangidwa ndi manja. 25Ndipo satumikiridwa ndi manja a anthu ngati kuti Iye amasowa kanthu, chifukwa Iye ndiye amapereka moyo ndi mpweya kwa anthu onse ndi zina zonse. 26Kuchoka kwa munthu mmodzi Iye analenga mtundu uliwonse wa anthu, kuti akakhale pa dziko lonse lapansi; ndipo Iye anakonzeratu nthawi yawo ndiponso malo enieni kumene adzakhale. 27Mulungu anachita izi kuti anthu amufunefune, ndikuti pomufunafunapo amupeze ngakhale kuti Iye sali kutali ndi aliyense wa ife. 28‘Pakuti timakhala mwa Iye, kuyenda mwa Iye ndi kukhala moyo mwa Iye.’ Monga olemba ndakatulo anu ena akuti, ‘Ife ndi zidzukulu zake.’

29“Tsono popeza ndife ana a Mulungu, tisaganize kuti umulungu wake ndi wofanana ndi ndalama zagolide, zasiliva, mwala, kapenanso fanizo lopangidwa mwaluso la nzeru za anthu. 30Nthawi imene anthu sankadziwa, Mulungu anawalekerera koma tsopano akulamulira kuti anthu onse, kulikonse atembenuke mtima. 31Pakuti Iye wayika tsiku limene adzaweruze dziko lapansi mwa chilungamo kudzera mwa Munthu amene anamusankha. Iye watsimikizira anthu onse zimenezi pomuukitsa.”

32Atamva za kuuka kwa akufa, ena a iwo anaseka, koma enanso anati, “Ife tikufuna tidzamvenso zimenezi tsiku lina.” 33Ndipo Paulo anatuluka mʼBwalolo. 34Anthu ena ochepa anamutsatira Paulo ndipo anakhulupirira. Pakati pawo panali Dionisiyo mmodzi wa bwalo la Areopagi ndi mayi wina wotchedwa Damalisi ndi enanso.

New Russian Translation

Деяния 17:1-34

Служение в Фессалонике

1Пройдя Амфиполь и Аполлонию, они пришли в Фессалонику, где была иудейская синагога. 2Павел, по своему обычаю, пошел в синагогу и там три субботы подряд рассуждал с иудеями о Писании, 3объясняя и доказывая, что Христос должен был пострадать и воскреснуть из мертвых.

– Иисус, о Котором я вам возвещаю, и есть Христос, – говорил Павел.

4Им удалось убедить как нескольких иудеев, так и многих благочестивых греков и немало знатных женщин. И все они присоединились к Павлу и Силе. 5Это возбудило зависть остальных иудеев, и они, взяв с собой негодных людей, которых нашли на базаре, собрали толпу и устроили в городе беспорядки. Они ринулись к дому Иасона, ища Павла и Силу, чтобы вывести их к толпе. 6Не найдя их там, они потащили Иасона и других братьев к городским властям.

– Эти люди устраивают беспорядки по всему миру, а сейчас пришли и сюда, – кричала толпа, 7– и Иасон принял их в свой дом. Они нарушают повеления кесаря и говорят, что есть другой царь, Которого зовут Иисус.

8Толпа и городские власти, слыша это, встревожились. 9Они взяли с Иасона и остальных залог и отпустили их.

Служение в Верии

10Как только наступила ночь, братья отправили Павла и Силу в Верию. Прибыв туда, они пошли в иудейскую синагогу. 11Верийцы были людьми более открытыми, чем фессалоникийцы. Они с большим интересом восприняли сказанное Павлом и каждый день исследовали Писания, чтобы проверить, соответствует ли услышанное ими истине. 12Многие из них поверили, поверило также много знатных гречанок и немало греков. 13Но когда иудеи в Фессалонике узнали о том, что Павел возвещает слово Божье в Верии, они пришли и туда и стали подстрекать и возмущать народ. 14Братья сразу же отправили Павла к морю, а Сила и Тимофей остались в городе. 15Провожатые Павла пришли с ним в Афины, а затем отправились обратно с повелением от Павла, чтобы Сила и Тимофей как можно скорее пришли к нему.

Служение Павла в Афинах

16Павел в ожидании своих спутников ходил по Афинам, и его возмущало огромное количество идолов в этом городе. 17Он беседовал в синагоге с иудеями и чтущими Бога греками. Каждый день он говорил со случайными встречными на площади. 18В беседу с ним вступали и некоторые философы, принадлежавшие к школам эпикурейцев и стоиков17:18 Эпикурейцы – философская школа, основанная Эпикуром (341–270 гг. до н. э.) в Афинах. Согласно их учению, смысл жизни заключается в спокойном наслаждении жизненными благами, не отуманенными болью и суеверным страхом перед богами. Стоики – философская школа, основанная Зеноном из Китиона (340–265 гг. до н. э.) и получившая свое название от портика (Стоа) в Афинах, в котором и учил основатель этой школы. Стоики учили, что главной целью человеческого существования является счастье, которое могли обеспечить только праведные поступки.. Одни спрашивали:

– И что этот пустомеля хочет сказать?

Другие говорили:

– Он, кажется, возвещает о чужеземных богах, –

потому что Павел возвещал Радостную Весть об Иисусе и воскресении17:18 Иисус и воскресение – слово «воскресение» («Анастасис» – греч.) могло восприниматься греками как имя некой богини, которую зовут Анастасия.. 19Павла привели на городской совет, Ареопаг17:19 Ареопаг – (греч. «холм Ареса») так называлось и место где собирался совет, и сам совет. Арес («Марс» – лат.) в греческой и римской мифологии был богом войны., и попросили:

– Расскажи нам, что это за новое учение, которое ты проповедуешь? 20Ты говоришь о чем-то странном, и нам хотелось бы знать, что все это значит.

21Наилучшим времяпрепровождением для афинян и живущих там иностранцев было говорить или слушать что-нибудь новое.

22И Павел, встав посреди Ареопага, сказал:

– Афиняне! Я по всему вижу, что вы очень религиозны. 23Я ходил вокруг и внимательно осматривал ваши святыни. На одном из жертвенников было написано: «НЕИЗВЕСТНОМУ БОГУ». Этого неизвестного Бога, Которого вы почитаете, даже не зная, Кто Он такой, я и возвещаю вам. 24Бог, сотворивший мир и все, что в нем, является Господом неба и земли. Он не живет в храмах, построенных руками людей, 25и не нуждается в том, чтобы люди служили Ему своими руками, как будто Ему чего-то не хватает, ведь Он Сам дает всем людям жизнь, дыхание и все остальное. 26От одного человека Он произвел все человечество, чтобы люди заселили всю землю, на которой Он определил для всех время и границы обитания. 27И все это Бог сделал для того, чтобы люди искали Его, могли ощутить Его и найти Его, хотя Он и не далек от каждого из нас. 28Ведь «в Нем мы живем, движемся и существуем»17:28 Здесь приводится цитата Эпименида Критского, жившего в VI – V вв. до н. э., как об этом говорили и некоторые из ваших поэтов: «Ведь мы и есть Его род»17:28 Здесь приводится цитата Арата Киликийца (IV – III вв. до н. э.). Похожие строки есть и у Клеанфа (IV – III вв. до н. э.).. 29И раз мы род Бога, то мы не должны представлять Божество в виде золотого, серебряного или каменного истукана или в виде какого-либо образа, сделанного по замыслу человека и умением его. 30Итак, оставляя в стороне времена невежества, Бог сейчас повелевает всем людям повсюду покаяться. 31Он назначил день, когда Он будет судить мир по справедливости, и уже избрал Человека, Который и будет судьей. Он подтвердил это перед всеми, воскресив Его из мертвых!

32Когда они услышали о воскресении из мертвых, то некоторые из них начали посмеиваться, другие же сказали:

– Об этом мы послушаем тебя в другой раз.

33С этим Павел и покинул собрание. 34Несколько человек, однако, присоединились к Павлу и уверовали. Среди них были Дионисий, член Ареопага, женщина по имени Дамарь и другие.