Machitidwe a Atumwi 16 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 16:1-40

Timoteyo Atsagana ndi Paulo ndi Sila

1Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki. 2Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino. 3Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki. 4Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire. 5Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.

Paulo Awona Masomphenya

6Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya. 7Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero. 8Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa. 9Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.” 10Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.

Lidia Atembenuka Mtima ku Filipi

11Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli. 12Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.

13Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo. 14Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo. 15Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.

Paulo ndi Sila Mʼndende

16Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake. 17Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.” 18Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.

19Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu. 20Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu. 21Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”

22Gulu la anthu linatsutsana ndi Paulo ndi Sila, ndipo woweruza milandu analamula kuti avulidwe ndi kumenyedwa. 23Atawakwapula kwambiri anawaponya mʼndende, nalamula woyangʼanira kuti awasunge mosamalitsa. 24Chifukwa cha mawu amenewa woyangʼanira ndende anakawayika mʼchipinda chamʼkati mwa ndende, nawamangirira miyendo yawo mʼzigologolo.

25Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera. 26Mwadzidzidzi kunachitika chivomerezi champhamvu kotero kuti maziko a ndende anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse za ndende zinatsekuka, ndipo maunyolo a aliyense anamasuka. 27Woyangʼanira ndende uja atadzuka ku tulo, anaona kuti zitseko za ndende zinali zotsekula, ndipo anasolola lupanga lake nafuna kudzipha chifukwa ankaganiza kuti amʼndende athawa. 28Koma Paulo anafuwula kuti, “Usadzipweteke! Tonse tilipo!”

29Woyangʼanira ndendeyo anayitanitsa nyale, nathamangira mʼkati ndipo anadzigwetsa pa mapazi a Paulo ndi Sila akunjenjemera. 30Iye anawatulutsa kunja ndipo anawafunsa kuti, “Amuna inu, ndichite chiyani kuti ndipulumuke?”

31Iwo anayankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka, iwe ndi a mʼbanja lako.” 32Kenaka analalikira mawu a Ambuye kwa iyeyo ndi onse amene anali mʼnyumba mwake. 33Usiku womwewo woyangʼanira ndendeyo anawatenga nakawatsuka mabala awo; ndipo pomwepo iye ndi a mʼbanja lake anabatizidwa. 34Woyangʼanira ndendeyo anapita nawo ku nyumba yake, nakawapatsa chakudya, ndipo banja lonse linadzazidwa ndi chimwemwe chifukwa anakhulupirira Mulungu.

35Kutacha, woweruza milandu uja anatuma asilikali kwa woyangʼanira ndendeyo kukanena kuti, “Amasuleni anthu aja.” 36Woyangʼanira ndendeyo anawuza Paulo kuti, “Woweruza milandu walamula kuti iwe ndi Sila mumasulidwe. Tsopano muzipita. Pitani mumtendere.”

37Koma Paulo anati kwa asilikaliwo: “Iwo anatikwapula pa gulu la anthu asanatiweruze, ngakhale kuti ndife nzika za Chiroma natiponya mʼndende. Kodi tsopano akufuna kutitulutsa mwamseri? Ayi! Asiyeni abwere okha kuti adzatitulutse.”

38Asilikali aja anakafotokozera woweruza milandu ndipo pamene anamva kuti Paulo ndi Sila anali nzika za Chiroma, anachita mantha. 39Iye anabwera kudzawapepesa ndipo anawatulutsa mʼndende, nawapempha kuti achoke mu mzindawo. 40Paulo ndi Sila atatuluka mʼndende, anapita ku nyumba ya Lidiya, kumene anakumana ndi abale nawalimbikitsa. Kenaka anachoka.

New Russian Translation

Деяния 16:1-40

Тимофей присоединяется к Павлу и Силе

1Павел пришел в Дервию и Листру. Там жил ученик по имени Тимофей.

Мать Тимофея была верующей иудеянкой, а отец его был грек. 2О Тимофее хорошо отзывались братья в Листре и Иконии. 3Павел захотел взять его с собой в путешествие. И ради иудеев, которые жили в той местности, обрезал его, поскольку все знали, что отец Тимофея грек. 4Путешествуя из города в город, Павел и его спутники призывали верующих соблюдать решение, принятое апостолами и старейшинами в Иерусалиме. 5Церкви укреплялись в вере, и число уверовавших с каждым днем увеличивалось.

Павлу является в видении человек из Македонии

6Они проходили через Фригию и Галатийскую область, но Святой Дух не позволил им возвещать слово в провинции Азия. 7Подойдя к границе с Мисией, они собрались идти в Вифинию, но Дух Иисуса не позволил им, 8и они, пройдя Мисию, пришли в Троаду. 9Ночью Павлу было видение: ему явился человек из Македонии. Он стоял и просил его:

– Приди в Македонию и помоги нам!

10После этого видения мы16:10 Мы – здесь можно увидеть, что с этого момента Лука сам стал участником этого путешествия. Участие Луки в описываемых событиях заметно в следующих отрывках: 16:10-17; 20:5–21:18; 27:1–28:16. решили, что Бог призывает нас возвещать им Радостную Весть, и сразу же приготовились отправиться в Македонию.

Обращение Лидии в Филиппах

11Из Троады мы отплыли прямо в Самофракию и оттуда на следующий день в Неаполь. 12Из Неаполя мы продолжили путешествие в Филиппы, римскую колонию и главный город той части Македонии. Там мы пробыли несколько дней. 13В субботу мы вышли за ворота города к реке, где, как мы предполагали, было место для молитвы. Мы сели и начали разговаривать с женщинами, которые там собрались. 14Среди них была одна по имени Лидия, из города Фиатиры, которая торговала дорогими пурпурными тканями. Лидия чтила Бога, и Господь открыл ее сердце к тому, что говорил Павел. 15После того как она и ее домашние были крещены, она пригласила нас к себе.

– Если вы считаете меня верной Господу, то придите и погостите у меня в доме, – упрашивала она и уговорила нас.

Арест Павла и Силы в Филиппах

16Однажды, когда мы шли к месту молитвы, по дороге нам повстречалась некая рабыня, одержимая духом-змеем16:16 Духом-змеем – букв.: «духом Пифоном». Согласно одной из версий древнегреческого мифа, Пифоном называлась огромная змея, опустошавшая окрестности Дельф. Она сторожила дельфийский оракул и давала там прорицания до того, как ее убил Аполлон. Позже Пифоном стали называть духа прорицания, который овладевал людьми.. Предсказаниями она приносила большой доход своим хозяевам. 17Рабыня шла за Павлом и за нами и кричала:

– Эти люди – слуги Всевышнего Бога! Они возвещают вам путь спасения!

18Она делала это изо дня в день, и когда Павлу все это надоело, он обернулся и сказал духу:

– Во имя Иисуса Христа я повелеваю тебе: выйди из нее!

В тот же момент дух ее покинул. 19Когда ее хозяева поняли, что у них пропал источник дохода, они схватили Павла и Силу и поволокли их на площадь к городским властям. 20Они привели их к начальникам города и сказали:

– Эти люди – иудеи, и они служат причиной беспорядков в нашем городе. 21Они вводят обычаи, которые нам, римлянам, не следует ни принимать, ни исполнять.

22Толпа тоже присоединилась к обвинениям против Павла и Силы, и начальники велели раздеть их и бить палками. 23Их сильно избили и бросили в темницу, а темничному стражу приказали бдительно их охранять. 24Получив такой приказ, он закрыл их во внутреннюю камеру и забил их ноги в колоду.

25Около полуночи Павел и Сила молились и пели хвалебные песни Богу, а другие заключенные слушали их. 26Внезапно произошло такое сильное землетрясение, что поколебались основания темницы. Все двери раскрылись, и у всех заключенных цепи упали с ног. 27Когда темничный страж проснулся и увидел, что все двери темницы раскрыты, он схватил меч и хотел покончить с собой, думая, что все заключенные убежали. 28Но Павел успел крикнуть:

– Не губи себя! Мы все здесь!

29Страж потребовал света, вбежал внутрь и, дрожа, пал перед Павлом и Силой. 30Он вывел их наружу и спросил:

– Господа мои, что мне делать, чтобы быть спасенным?

31– Веруй в Господа Иисуса, – ответили они, – и ты будешь спасен, и твои домашние.

32И они возвестили слово Господа ему и его домашним. 33В тот же ночной час темничный страж промыл им раны и сразу же был крещен, он сам и все домашние его. 34Он привел Павла и Силу к себе домой и накрыл для них стол. Вместе со всеми своими домашними он радовался тому, что поверил в Бога.

35Наступил день, и городские начальники послали своих служителей в темницу с приказом:

– Освободите этих людей.

36Темничный страж сказал Павлу:

– Начальники приказали освободить вас! Вы можете идти с миром!

37Но Павел сказал:

– Они без суда избили нас перед народом, несмотря на то что мы римские граждане, и бросили нас в темницу. Сейчас же они хотят от нас избавиться так, чтобы никто не знал? Нет! Пусть они сами придут и выведут нас.

38Служители доложили об этом городским начальникам, и когда те услышали, что Павел и Сила римские граждане, то испугались. 39Они пришли, принесли им свои извинения, вывели из темницы и попросили, чтобы те покинули город. 40Выйдя из темницы, Павел и Сила пошли в дом Лидии. Там они встретились с братьями и ободрили их. После этого они отправились дальше.