Machitidwe a Atumwi 15 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 15:1-41

Msonkhano wa ku Yerusalemu

1Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.” 2Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi. 3Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse. 4Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.

5Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”

6Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi. 7Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira. 8Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife. 9Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro. 10Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza? 11Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”

12Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo. 13Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani. 14Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake. 15Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,

16“ ‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera

ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa.

Ndidzakonzanso malo amene anagumuka,

ndi kuyimanganso,

17kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye,

ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa,

akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi

18zinaululidwa kuyambira kalekale.’

19“Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu. 20Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi. 21Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”

Kalata Yopita kwa Anthu a Mitundu ina

22Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale, 23kuti akapereke kalata yonena kuti,

Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu,

Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya:

Tikupereka moni.

24Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani. 25Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba, 26anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu. 27Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba. 28Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi: 29Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi.

Tsalani bwino.

30Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo. 31Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso. 32Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo. 33Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma. 34Koma Sila anasankha kuti akhale komweko. 35Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.

Paulo Asiyana ndi Barnaba

36Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.” 37Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo. 38Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito. 39Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 40Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka. 41Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.

Священное Писание

Деяния 15:1-41

Совет в Иерусалиме

1Из Иудеи в Антиохию пришли люди, которые стали учить братьев:

– Если вы не будете обрезаны по обряду, предписанному Мусой15:1 См. Нач. 17:10-14; Лев. 12:3., вы не можете быть спасены.

2Это привело к разногласиям и горячему спору между ними с одной стороны и Паулом и Варнавой – с другой. Тогда Паулу и Варнаве поручили пойти вместе с несколькими другими верующими в Иерусалим и обсудить этот вопрос с посланниками Масиха и старейшинами. 3Получив помощь от общины верующих, они пошли через Финикию и Самарию, рассказывая там об обращении язычников. Эта весть вызывала у всех верующих большую радость.

4В Иерусалиме они были приняты членами общины верующих, посланниками Масиха и старейшинами и рассказали им обо всём, что Всевышний совершил через них. 5Но верующие, принадлежавшие к религиозной партии блюстителей Закона, говорили, что язычников следует обрезывать и требовать от них соблюдения Закона Мусы.

6Посланники Масиха и старейшины собрались, чтобы рассмотреть этот вопрос. 7После долгих обсуждений Петир поднялся и сказал:

– Братья, как вы знаете, прошло уже много времени с того дня, как Всевышний выбрал из всех нас меня возвещать слово Радостной Вести другим народам, чтобы и они уверовали. 8Всевышний знает сердца людей, и Он дал свидетельство того, что принимает и уверовавших из других народов, даровав им Святого Духа так же, как и нам. 9Он не делает никакой разницы между нами и ими, потому что Он через веру очистил и их сердца! 10Так зачем же вы испытываете Всевышнего, возлагая на шеи учеников бремя, которое не в состоянии были нести ни наши отцы, ни мы? 11Ведь мы верим в то, что получаем спасение по благодати Повелителя Исы так же, как и они.

12Тогда все затихли и стали слушать рассказ Варнавы и Паула о знамениях и чудесах, которые Всевышний совершил через них среди язычников. 13Когда они закончили, Якуб15:13 Якуб – единоутробный брат Исы Масиха (см. Мат. 13:55). сказал:

– Братья, послушайте меня. 14Шимон15:14 То есть Петир (см. 15:7; 10:5). рассказал нам о том, как Всевышний впервые решил составить из язычников народ для Себя. 15Это полностью согласуется с Книгой Пророков, где сказано:

16«Затем Я возвращусь.

Трон Давуда – как разрушенный шатёр,

но Я восстановлю разрушенное

и воссоздам его,

17чтобы остальные люди,

все народы, которые призваны быть Моими,

стали искать Вечного.

Так говорит Вечный,

18Который объявил об этом издревле»15:16-18 Ам. 9:11-12..

19Поэтому я считаю, что мы не должны создавать трудностей для людей из других народов, обращающихся к Всевышнему. 20Напротив, мы должны написать им письмо, предупредив лишь, чтобы они воздерживались от пищи, осквернённой принесением в жертву идолам, от разврата, от мяса удушенных животных и от крови15:20 См. Нач. 9:4; Исх. 34:15-16; Лев. 17:10-16; 18:6-23. Удушенных животных запрещалось употреблять в пищу потому, что в них оставалась кровь.. 21Ведь Закон Мусы, издавна возвещается в каждом городе и читается в молитвенных домах иудеев каждую субботу.

Письмо Совета к братьям из других народов

22Посланники Масиха и старейшины вместе со всем собранием верующих решили выбрать несколько человек из своей среды и послать их с Паулом и Варнавой в Антиохию. Они выбрали двух руководящих братьев: Иуду, которого ещё называли Бар-Сабба, и Силу. 23С ними передали такое письмо:

«Ваши братья, посланники Масиха и старейшины, – братьям из других народов, находящимся в Антиохии, Сирии и Киликии.

Приветствуем вас!

24До нас дошли слухи о том, что некоторые люди, пришедшие от нас, привели вас в замешательство своими словами и взволновали ваши умы, но мы ничего им не поручали. 25Поэтому мы с общего согласия решили выбрать из нашей среды несколько человек и послать их к вам вместе с нашими дорогими братьями Варнавой и Паулом, 26которые рисковали своей жизнью ради имени нашего Повелителя Исы Масиха. 27Мы посылаем к вам также Иуду и Силу, чтобы они на словах подтвердили то, что мы пишем. 28Святой Дух и мы решили не обременять вас ничем, кроме следующих требований: 29воздерживайтесь от пищи, принесённой в жертву идолам, от крови, от мяса удушенных животных и от всякого разврата. Если вы будете соблюдать это, то поступите правильно.

Всех вам благ».

30Посланные отправились и пришли в Антиохию. Там они собрали общину верующих и вручили письмо. 31Люди читали его и радовались ободряющей вести. 32Иуда и Сила, которые сами были пророками, своими словами ободряли и воодушевляли братьев. 33-34Они провели там некоторое время, и братья отпустили их с пожеланием мира тем, кто их послал15:33-34 Некоторые рукописи включают стих 34: «Сила, однако же, решил остаться».. 35Паул и Варнава остались в Антиохии, где они со многими другими братьями учили и возвещали слово о Повелителе Исе.

Разногласия между Паулом и Варнавой

36Несколько дней спустя Паул предложил Варнаве:

– Давай посетим братьев во всех городах, где мы возвещали слово о Повелителе, и посмотрим, как у них идут дела.

37Варнава хотел взять с собой Иохана, которого ещё называли Марком, 38но Паул не хотел брать с собой того, кто оставил их в Памфилии и не помог исполнить порученную им работу15:38 См. 12:12; 13:13..

39Разногласие по этому вопросу было столь острым, что они расстались15:39 Позже Паул примирился с Варнавой (см. 1 Кор. 9:6) и Марком (см. Кол. 4:10; 2 Тим. 4:11; Флм. 1:24).. Варнава взял Марка и отплыл на Кипр, 40а Паул выбрал Силу и, будучи вверен братьями попечению Вечного Повелителя, отправился в путь. 41Паул проходил через Сирию и Киликию, утверждая общины верующих.