Machitidwe a Atumwi 13 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 13:1-52

Barnaba ndi Saulo Atumidwa ndi Mpingo

1Mu mpingo wa ku Antiokeya munali aneneri ndi aphunzitsi awa: Barnaba, Simeoni, Lukia wa ku Kurene, Manayeni (amene analeredwa pamodzi ndi mfumu Herode), ndiponso Saulo. 2Iwo pamene ankapembedza Ambuye ndi kusala kudya, Mzimu Woyera anati, “Mundipatulire Barnaba ndi Saulo kuti akagwire ntchito imene ndinawayitanira.” 3Ndipo atasala kudya ndi kupemphera anasanjika manja awo pa iwo nawatumiza.

Ku Kupro

4Barnaba ndi Saulo motumidwa ndi Mzimu Woyera, anapita ku Selukeya ndipo kuchokera kumeneko anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro. 5Pamene anafika ku Salamisi, analalikira Mawu a Mulungu mʼMasunagoge a Ayuda. Iwo anali ndi Yohane monga wowatumikira.

6Iwo anayenda pa chilumba chonse mpaka anafika ku Pafo, kumeneko anapezanako ndi Myuda, wamatsenga amene analinso mneneri wonama dzina lake Barayesu. 7Iyeyu, amathandiza mkulu wa boma, Sergio Paulo. Mkulu wa bomayu, munthu wanzeru, anayitana Barnaba ndi Saulo chifukwa anafuna kumva Mawu a Mulungu. 8Koma Elima wamatsengayo, (Elima tanthauzo lake ndi wamatsenga), anatsutsana nawo ndipo anafuna kumuletsa mkulu wa bomayo kuti asakhulupirire. 9Koma Saulo, amenenso amatchedwa Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera anamuyangʼanitsitsa Elima ndipo anati, 10“Iwe ndiwe mwana wa mdierekezi ndiponso mdani wa chilungamo! Ndiwe wodzaza ndi chinyengo cha mtundu uliwonse ndi kuchenjera konse. Kodi sudzaleka kupotoza njira zolungama za Ambuye? 11Tsopano dzanja la Ambuye likukutsutsa iwe. Udzakhala wosaona ndipo kwa kanthawi sudzatha kuona kuwala kwa dzuwa.”

Nthawi yomweyo khungu ndi mdima zinamugwera ndipo anafunafuna munthu woti amugwire dzanja kuti amutsogolere. 12Pamene mkulu wa bomayo anaona zimene zinachitika anakhulupirira pakuti anadabwa ndi chiphunzitso cha Ambuye.

Antiokeya wa ku Pisidiya

13Kuchokera ku Pafo, Paulo ndi anzake anayenda pa sitima ya pamadzi kupita ku Perga wa ku Pamfiliya, kumeneko Yohane anawasiya nabwerera ku Yerusalemu. 14Kuchokera ku Perga anapita ku Pisidiya wa ku Antiokeya. Pa tsiku la Sabata analowa mʼsunagoge, nakhala pansi. 15Atawerenga mawu a mʼMalamulo ndi Aneneri, akulu a sunagoge anawatumizira mawu ndi kuti, “Abale ngati muli ndi mawu olimbikitsa nawo anthuwa, nenani.”

16Atayimirira, Paulo anakweza dzanja lake ndi kuti, “Inu Aisraeli ndiponso inu a mitundu ina amene mumapembedza Mulungu, tandimverani! 17Mulungu wa Aisraeli anasankha makolo athu ndipo anawapatsa chuma chambiri pamene amakhala ku Igupto. Anawatulutsa mʼdzikomo ndi dzanja lake lamphamvu. 18Ndipo Iye anapirira khalidwe lawo mʼchipululu kwa zaka makumi anayi. 19Mulungu anawagonjetsera mitundu isanu ndi iwiri ya ku Kanaani ndipo anapereka dzikolo kwa Israeli kuti likhale lawo. 20Izi zonse zinatenga zaka 450.

“Zitatha izi, Mulungu anawapatsa oweruza mpaka nthawi ya mneneri Samueli. 21Kenaka anthu anapempha kuti awapatse mfumu, ndipo anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, wa fuko la Benjamini amene analamulira zaka makumi anayi. 22Mulungu atamuchotsa Sauli, anayika Davide kukhala mfumu yawo. Mulungu anamuchitira umboni kuti, ‘Ndapeza Davide mwana wa Yese munthu wa pamtima panga; iye adzachita zonse zimene ine ndikufuna kuti iye achite.’

23“Kuchokera mwa zidzukulu za munthu ameneyu, Mulungu anawutsa Yesu kukhala Mpulumutsi wa Aisraeli, monga analonjezera. 24Yesu asanabwere, Yohane analalikira kwa anthu onse Aisraeli za kutembenuka mtima ndi ubatizo. 25Pamene Yohane amatsiriza ntchito yake anati: ‘Mukuganiza kuti ine ndine yani? Ine sindine ameneyo ayi, koma Iye akubwera pambuyo panga, amene ine sindine woyenera kumasula zingwe za nsapato zake.’

26“Abale, ana a Abrahamu, ndiponso inu a mitundu ina amene mumaopa Mulungu, Iye watumiza uthenga wachipulumutsowo kwa ife. 27Anthu a ku Yerusalemu ndi atsogoleri awo sanazindikire Yesu, komabe pomuweruza Yesu anakwaniritsa mawu a Aneneri amene amawerengedwa Sabata lililonse. 28Ngakhale sanapeze chifukwa choti afe, anapempha Pilato kuti amuphe. 29Atachita zonse zimene zinalembedwa za Iye, iwo anamuchotsa pa mtengo ndipo anamuyika mʼmanda. 30Koma Mulungu anamuukitsa, 31ndipo kwa masiku ambiri anaonekera kwa amene anayenda naye kuchokera ku Galileya mpaka ku Yerusalemu. Iwowa tsopano ndi mboni zake kwa anthu a Israeli.

32“Ife tikukuwuzani Uthenga Wabwino; umene Mulungu analonjeza makolo athu. 33Iye wakwaniritsa zimenezi kwa ife ana awo, poukitsa Yesu kuchokera kwa akufa. Monga zinalembedwa mu Salimo lachiwiri kuti,

“Iwe ndiwe mwana wanga;

lero ine ndakhala Atate ako.”

34Zakuti Mulungu anamuukitsa kuti asawole konse, zinanenedwa mʼmawu awa:

“ ‘Ine, ndidzakupatsa madalitso opatulika ndi odalirika amene ndinalonjeza Davide.’

35Nʼchifukwa chakenso zinalembedwa mu Salimo lina kuti,

“ ‘Simudzalekerera woyera wanu kuti awole.’

36“Pakuti pamene Davide anatsiriza kutumikira Mulungu mu mʼbado wake, anamwalira, iye anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ndipo thupi lake linawola. 37Koma amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa sanawole ayi.

38“Nʼchifukwa chake, abale anga, dziwani kuti mwa Yesu chikhululukiro cha machimo chikulalikidwa. 39Kudzera mwa Iye aliyense amene akhulupirira, alungamitsidwa kuchoka ku tchimo lililonse limene silingachoke ndi Malamulo a Mose. 40Samalani kuti zimene aneneri akunena zisakuchitikireni inu:

41“ ‘Onani, inu anthu onyoza,

dabwani ndipo wonongekani,

chifukwa ine ndidzachita china chake mʼmasiku anu,

inu simudzazikhulupirira

ngakhale wina atakufotokozerani!’ ”

42Pamene Paulo ndi Barnaba amatuluka mʼSunagoge, anthu anawapempha kuti adzapitirize kuyankhula zinthu zimenezi Sabata linalo. 43Atatha mapemphero, Ayuda ambiri ndi anthu odzipereka otembenukira ku Chiyuda anatsatira Paulo ndi Barnaba, iwo anayankhula ndi anthuwo ndipo anawapempha kuti apitirire mʼchisomo cha Mulungu.

44Pa Sabata linalo pafupifupi anthu onse a mu mzindawo anasonkhana kudzamva Mawu a Ambuye. 45Pamene Ayuda anaona gulu la anthu, anachita nsanje ndipo anayankhula zamwano kutsutsana ndi zimene Paulo amanena.

46Ndipo Paulo ndi Barnaba anawayankha molimba mtima kuti, “Ife tinayenera kuyankhula Mawu a Mulungu kwa inu poyamba. Popeza inu mwawakana ndi kudziyesa nokha osayenera moyo wosatha, ife tsopano tikupita kwa anthu a mitundu ina. 47Pakuti izi ndi zimene Ambuye anatilamula ife:

“ ‘Ine ndakuyika iwe ukhale kuwunika kwa anthu a mitundu ina,

kuti ukafikitse chipulumutso ku malekezero a dziko lapansi!’ ”

48Anthu a mitundu ina atamva izi, anakondwa ndipo analemekeza Mawu Ambuye; ndipo onse amene anawasankha kuti alandire moyo osatha anakhulupirira.

49Mawu a Ambuye anafalikira mʼchigawo chonse. 50Koma Ayuda anawutsa mitima ya akazi otchuka opembedza Mulungu ndi akulu a mu mzindamo. Iwo anabweretsa mazunzo kwa Paulo ndi Barnaba ndipo anawathamangitsa mʼchigawo chawo. 51Tsono iwo anasasa fumbi la ku mapazi awo powatsutsa, ndipo anapita ku Ikoniya. 52Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chimwemwe ndiponso ndi Mzimu Woyera.

New Russian Translation

Деяния 13:1-52

Варнава и Савл посланы на служение

1В церкви Антиохии были пророки и учители: Варнава, Симеон, называемый Нигер13:1 Нигер – «черный» (лат.)., киренец Луций, Манаин, получивший воспитание вместе с правителем Иродом, и Савл. 2Однажды, когда они служили Господу и постились, Святой Дух сказал:

– Отделите мне Варнаву и Савла для дела, к которому Я их призвал.

3И они после поста и молитвы возложили на них руки и отпустили их.

Апостолы проповедуют на Кипре

4Эти два апостола, посланные Святым Духом, пошли в Селевкию, а оттуда отплыли на Кипр. 5Они прибыли в Саламин и там возвещали слово Божье в иудейских синагогах. Иоанн тоже был с ними и помогал им. 6Они прошли весь остров и пришли в Пафос. Там они встретили одного иудея по имени Вар-Иисус, который был колдуном и лжепророком. 7Он был с римским проконсулом Сергием Павлом, человеком большого ума. Проконсул пригласил Варнаву и Савла, желая услышать слово Божье. 8Но колдун, которого также звали Елима (что значит «чародей»), действовал против них и пытался отвратить проконсула от веры. 9Тогда Савл, он же Павел, исполнившись Святого Духа, посмотрел прямо на Елиму 10и сказал:

– Сын дьявола, враг всякой праведности, полный лжи и нечестия! Неужели ты никогда не перестанешь искривлять прямые пути Господни? 11Рука Господа обращена против тебя, ты будешь поражен слепотой и некоторое время не будешь видеть солнечного света.

И сразу же его окутали мрак и тьма, и он стал метаться из стороны в сторону, ища кого-либо, кто бы повел его за руку. 12Когда проконсул увидел, что произошло, он уверовал, изумленный учением о Господе.

Служение в писидийской Антиохии

13Отплыв из Пафоса, Павел и его спутники прибыли в Пергию в Памфилии13:13 Далее (до 14:26) это путешествие проходило по территории Малой Азии (часть современной Турции).. Там Иоанн оставил их и возвратился в Иерусалим. 14Из Пергии они пошли дальше, в Писидийскую Антиохию. В субботу они пришли в синагогу и сели. 15После чтения из Закона и Пророков начальники синагоги передали им:

– Братья, если у вас есть что-либо сказать в назидание людям, то говорите.

16Павел встал и, сделав жест рукой, сказал:

– Израильтяне и все боящиеся Бога, выслушайте меня! 17Бог израильского народа избрал наших отцов. Он возвысил народ во время пребывания его в Египте и могучей рукой вывел их оттуда13:17 См. Исх. 6:6; 12:51.. 18Сорок лет Он терпел их13:18 Или: «заботился о них». в пустыне. 19Он истребил в Ханаане семь народов13:19 Семь народов – см. Втор. 7:1. и отдал их землю в наследие нашим предкам.

20На это ушло около четырехсот пятидесяти лет. Затем, до времени пророка Самуила, Бог давал им судей. 21Потом народ попросил себе царя, и Бог дал им из рода Вениамина Саула, сына Киша. Саул правил лет сорок. 22Потом, отстранив Саула, Бог сделал царем Давида. Он свидетельствовал о нем: «Я нашел Давида, сына Иессея, человек этот Мне по сердцу, он исполнит все Мои желания»13:22 См. 1 Цар. 13:14; Пс. 88:21.. 23Из потомков Давида Бог, согласно Своему обещанию, призвал Спасителя Израилю – Иисуса. 24Перед пришествием Иисуса Иоанн призывал к крещению в знак покаяния весь народ Израиля. 25Заканчивая свое служение, Иоанн говорил: «За кого вы меня принимаете? Я не Он. Но за мной идет Тот, у Кого я не достоин даже развязать ремни сандалий на ногах».

26Братья, дети рода Авраама, и те, кто боится Бога! Эта весть спасения была послана к нам! 27Жители Иерусалима и их начальники не узнали Христа, они осудили Его и тем самым исполнили слова пророков, которые читаются каждую субботу. 28Они не нашли в Нем никакой вины, за которую Он был бы достоин смерти, и все-таки выпросили у Пилата разрешение казнить Его. 29Когда они исполнили все, что было о Нем написано, они сняли Его с дерева и положили в гробницу. 30Но Бог воскресил Его из мертвых, 31и еще много дней те, кто пришел вместе с Ним из Галилеи в Иерусалим, видели Его. Они сейчас – Его свидетели перед народом.

32Мы провозглашаем вам сейчас эту Радостную Весть: то, что Бог обещал нашим отцам, 33Он исполнил для нас, их детей, воскресив Иисуса. Во втором псалме написано:

«Ты Сын Мой,

сегодня Я родил Тебя»13:33 Пс. 2:7.

34А о том, что Бог воскресил Его из мертвых, так что тело Его уже никогда не увидит тления, Он сказал так:

«Я дам вам святые и неизменные благословения, обещанные Давиду»13:34 См. Ис. 55:3..

35И в другом месте Он говорит:

«Ты не дашь Твоему Святому увидеть тление»13:35 См. Пс. 15:10..

36Давид в своем поколении исполнял Божий замысел. Давид умер, его похоронили с его отцами, и тело его истлело. 37Но Тот, Кого Бог воскресил, избежал тления.

38Поэтому, братья, я хочу, чтобы вы знали, что благодаря Ему вам сегодня возвещается прощение грехов, 39и во всем, в чем Закон Моисея не мог вас оправдать, каждый верующий получает оправдание в Нем. 40Смотрите, чтобы не случилось с вами того, о чем сказано у пророков:

41«Посмотрите, насмешники,

изумитесь и погибните,

потому что Я совершу в ваши дни такое,

чему бы вы никогда не поверили,

если бы вам рассказали об этом»13:40-41 См. Авв. 1:5..

42Когда Павел и Варнава покидали синагогу, их попросили говорить о том же в следующую субботу. 43Собрание разошлось, но многие иудеи и благочестивые люди из обращенных в иудаизм пошли за Павлом и Варнавой. Те говорили с ними и убеждали их и дальше жить, доверяясь благодати Божьей.

44В следующую субботу почти весь город собрался, чтобы послушать слово Господа. 45Когда иудеи13:45 То есть иудеи, отвергающие Иисуса. увидели столько народа, они исполнились завистью и стали с оскорблениями возражать тому, что говорил Павел. 46Тогда Павел и Варнава решительно сказали им:

– Слово Божье следовало в первую очередь возвещать вам. Но так как вы отрицаете его и не считаете себя достойными вечной жизни, мы обращаемся теперь к язычникам, 47как и повелел нам Господь. Он сказал:

«Я сделал тебя светом для язычников,

чтобы через тебя спасение достигло концов земли»13:47 См. Ис. 49:6..

48Когда язычники слышали это, они радовались и славили Господа за Его слово, и все предназначенные к вечной жизни уверовали.

49Слово Господне распространилось по всей той области.

50Иудеи13:50 То есть предводители иудеев; также в ст. 14:4. подговорили благочестивых женщин из знатных семей и начальников города, и те возбудили преследование против Павла и Варнавы и выгнали их из своих пределов. 51Тогда они отряхнули пыль со своих ног во свидетельство против них и пошли в Иконию. 52Ученики же исполнялись радости и Святого Духа.