Machitidwe a Atumwi 11 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 11:1-30

Petro Afotokozera Mpingo

1Atumwi ndi abale a ku Yudeya konse anamva kuti anthu a mitundu ina analandiranso Mawu a Mulungu. 2Tsono Petro atafika ku Yerusalemu, abale amene anali a mdulidwe anamutsutsa iye, 3ndipo anati, “Iwe unalowa mʼnyumba ya anthu osachita mdulidwe ndi kudya nawo.”

4Koma Petro anayamba kuwafotokozera zonse mwatsatanetsatane momwe zinachitikira kuti, 5“Ine ndimapemphera mu mzinda wa Yopa ndipo ndili ngati wokomoka ndinaona masomphenya. Ndinaona chinthu chokhala ngati chinsalu chachikulu chikutsika kuchokera kumwamba chogwiridwa msonga zake zinayi, ndipo chinatsikira pa ine. 6Ine ndinayangʼana mʼkati mwake ndipo ndinaona nyama za miyendo inayi za mʼdziko lapansi, zirombo, zokwawa, ndi mbalame zamlengalenga. 7Kenaka ine ndinamva mawu akuti, ‘Petro, Imirira. Ipha, nudye.’

8“Ine ndinayankha kuti, ‘Ayi, Ambuye! Pakuti chinthu chodetsedwa ndi chonyansa sindinadyepo pakamwa pangapa.’

9“Mawu ochokera kumwamba ananenanso kachiwiri kuti, ‘Chimene Mulungu wachiyeretsa usanene kuti ndi chodetsedwa.’ 10Zimenezi zinachitika katatu ndipo kenaka zonse zinatengedwa kupita kumwamba.

11“Nthawi yomweyo anthu atatu amene anatumidwa kuchokera ku Kaisareya anayima pa nyumba yomwe ndimakhalayo. 12Mzimu anandiwuza kuti ndisakayike, koma ndipite nawo. Abale asanu ndi mmodzi awa anapitanso nane ndipo tinalowa mʼnyumba ya munthuyo. 13Iye anatiwuza mmene anaonera mngelo atayimirira mʼnyumba mwake ndi kumuwuza kuti, ‘Tumiza anthu ku Yopa kuti akayitane Simoni wotchedwa Petro. 14Iye adzakuwuza uthenga umene udzapulumutsa iwe ndi a pa banja ako.’

15“Nditangoyamba kuyankhula, Mzimu Woyera anafika pa iwo monga momwe anafikira pa ife poyamba paja. 16Kenaka ndinakumbukira zimene Ambuye ananena kuti, ‘Yohane anabatiza ndi madzi, koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.’ 17Tsono ngati Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyo imene anatipatsa ife, amene tinakhulupirira Ambuye Yesu Khristu, ndine yani kuti nditsutsane ndi Mulungu?”

18Iwo atamva zimenezi analibenso chonena ndipo anayamika Mulungu nati, “Potero Mulungu wapatsa anthu a mitundu ina mwayi wotembenuka mtima ndi kulandira moyo.”

Mpingo wa ku Antiokeya

19Tsopano amene anabalalika chifukwa cha mazunzo amene anayamba ataphedwa Stefano, anapita mpaka ku Foinike, ku Kupro ndi ku Antiokeya, ndipo ankalalikira kwa Ayuda okha. 20Komabe, ena pakati pawo ochokera ku Kupro ndi ku Kurene anapita ku Antiokeya ndipo iwo anayamba kuyankhulanso kwa Agriki, nawawuza za Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu. 21Mphamvu ya Ambuye inali nawo ndipo anthu ambiri anakhulupirira natembenukira kwa Ambuye.

22Mbiri imeneyi inamveka ku mpingo wa ku Yerusalemu ndipo iwo anatumiza Barnaba ku Antiokeya. 23Atafika ndi kuona chisomo cha Mulungu pa iwo, anakondwa ndi kuwalimbikitsa anthu onsewo kuti apitirire kukhala woona mu mtima mwa Ambuye. 24Barnabayo anali munthu wabwino, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi chikhulupiriro ndipo gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Ambuye.

25Kenaka Barnaba anapita ku Tarisisi kukafuna Saulo, 26ndipo pamene anamupeza anabwera naye ku Antiokeya. Barnaba ndi Saulo anasonkhana ndi mpingo kwa chaka chimodzi naphunzitsa anthu ambirimbiri. Okhulupirirawo anayamba kutchedwa Akhristu ku Antiokeya.

27Masiku amenewo ku Antiokeya kunafika aneneri ena ochokera ku Yerusalemu. 28Mmodzi wa iwo dzina lake Agabu, anayimirira ndipo Mzimu anamutsogolera kunenera zamʼtsogolo kuti padzakhala njala yayikulu pa dziko lonse lapansi. (Izi zinachitikadi nthawi ya ulamuliro wa Klaudiyo). 29Ophunzirawo, aliyense monga mwakupata kwake, anatsimikiza kuthandiza abale okhala ku Yudeya. 30Izi anazichitadi ndipo anatuma Barnaba ndi Saulo kukapereka mphatsozo kwa akulu a mpingo.

La Bible du Semeur

Actes 11:1-30

Le rapport de Pierre aux croyants de Jérusalem

1Les apôtres et les frères qui habitaient la Judée apprirent que les non-Juifs venaient d’accepter la Parole de Dieu. 2Et dès que Pierre fut de retour à Jérusalem, les croyants d’origine juive lui firent des reproches : 3Comment ! lui dirent-ils, tu es entré chez des incirconcis et tu as mangé avec eux !

4Mais Pierre se mit à leur exposer, point par point, ce qui s’était passé.

5– Pendant mon séjour à Jaffa, dit-il, j’étais en train de prier, quand je suis tombé en extase et j’ai eu une vision : une sorte de grande toile, tenue aux quatre coins, est descendue du ciel et elle est venue tout près de moi. 6J’ai regardé attentivement ce qu’il y avait dedans et j’ai vu des quadrupèdes, des bêtes sauvages, des reptiles et des oiseaux. 7J’ai entendu alors une voix qui me disait : « Lève-toi, Pierre, tue ces bêtes et mange-les. » 8Mais j’ai répondu : « Oh ! non, Seigneur, car jamais de ma vie je n’ai rien mangé de souillé ou d’impur. » 9La voix céleste s’est fait entendre une deuxième fois : « Ce que Dieu a déclaré pur, ce n’est pas à toi de le considérer comme impur. »

10Cela est arrivé trois fois, puis tout a disparu dans le ciel.

11Et voilà qu’au même moment trois hommes sont arrivés à la maison où nous nous trouvions11.11 Certains manuscrits ont : je me trouvais.. Ils venaient de Césarée et avaient été envoyés vers moi. 12Alors l’Esprit me dit d’aller avec eux sans hésiter. Je pris donc avec moi les six frères que voici et nous nous sommes rendus chez cet homme.

13Celui-ci nous a raconté qu’un ange lui était apparu dans sa maison et lui avait dit : « Envoie quelqu’un à Jaffa pour faire venir chez toi Simon, surnommé Pierre. 14Il te dira comment toi et tous les tiens vous serez sauvés. »

15J’ai donc commencé à leur parler, quand l’Esprit Saint est descendu sur eux, de la même manière qu’il était descendu sur nous au commencement. 16Aussitôt, je me suis souvenu de cette parole du Seigneur :

Jean a baptisé dans de l’eau, mais vous,

vous serez baptisés dans le Saint-Esprit.

17Puisque Dieu leur a accordé le même don qu’à nous quand nous avons cru, qui étais-je, moi, pour pouvoir m’opposer à Dieu ?

18Ce récit les apaisa et ils louèrent Dieu et dirent : Dieu a aussi donné aux non-Juifs de changer pour recevoir la vie.

La Parole annoncée aux non-Juifs à Antioche

19Les disciples s’étaient dispersés lors de la persécution survenue après la mort d’Etienne. Ils allèrent jusqu’en Phénicie, dans l’île de Chypre et à Antioche11.19 Antioche: capitale de la province romaine de Syrie. Troisième ville de l’Empire romain (après Rome et Alexandrie). Appelée souvent Antioche de Syrie pour la distinguer d’Antioche de Pisidie (voir 13.14)., mais ils n’annonçaient la Parole qu’aux Juifs. 20Toutefois, quelques-uns d’entre eux, qui étaient originaires de Chypre et de Cyrène, se rendirent à Antioche et s’adressèrent aussi aux non-Juifs11.20 Certains manuscrits ont : des Juifs de culture grecque. en leur annonçant le Seigneur Jésus. 21Or le Seigneur était avec eux ; un grand nombre de personnes crurent et se convertirent au Seigneur.

22Bientôt l’Eglise qui était à Jérusalem apprit la nouvelle. Elle envoya Barnabas à Antioche. 23A son arrivée, il constata ce que la grâce de Dieu avait accompli et il en fut rempli de joie. Il encouragea donc tous les croyants à rester fidèles au Seigneur avec une ferme assurance. 24Barnabas était en effet un homme bienveillant, rempli d’Esprit Saint et de foi. Et un grand nombre de personnes s’attachèrent au Seigneur. 25Barnabas se rendit alors à Tarse pour y chercher Saul. Quand il l’eut trouvé, il l’amena avec lui à Antioche. 26Ils passèrent toute une année à travailler ensemble dans l’Eglise et enseignèrent beaucoup de gens. C’est à Antioche que, pour la première fois, les disciples de Jésus furent appelés « chrétiens ».

27A cette même époque, des prophètes se rendirent de Jérusalem à Antioche. 28L’un d’eux, nommé Agabus, se leva et prédit sous l’inspiration de l’Esprit qu’une grande famine sévirait bientôt dans le monde entier11.28 Le monde entier: expression qui désigne souvent l’Empire romain (voir Lc 2.1-2).. Elle eut lieu, en effet, sous le règne de l’empereur Claude11.28 Claude: empereur romain qui a régné de 41 à 54 apr. J.-C. La famine a sévi dans diverses provinces romaines entre 46 et 48.. 29Les disciples d’Antioche décidèrent alors de donner, chacun selon ses moyens, et d’envoyer des secours aux frères qui habitaient la Judée. 30C’est ce qu’ils firent : ils envoyèrent leurs dons aux responsables de l’Eglise par l’intermédiaire de Barnabas et de Saul11.30 Deuxième visite de Paul à Jérusalem, qui coïncide selon certains avec celle qu’il mentionne en Ga 2.1-10..