Machitidwe a Atumwi 10 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 10:1-48

Kenturiyo Korneliyo Ayitana Petro

1Ku Kaisareya kunali munthu wina dzina lake Korneliyo, mkulu wa asilikali 100 wa gulu la Italiya. 2Iye ndi banja lake lonse amapembedza ndi kuopa Mulungu. Iye amathandiza osowa mowolowamanja ndipo amapemphera kwa Mulungu nthawi zonse. 3Tsiku lina, nthawi ili ngati 3 koloko masana, anaona masomphenya. Anaona bwino ndithu mngelo wa Mulungu, amene anabwera kwa iye ndi kuti, “Korneliyo.”

4Korneliyo anamuyangʼanitsitsa mngeloyo mwa mantha. Iye anafunsa kuti, “Nʼchiyani kodi Ambuye?”

Mngelo anayankha kuti, “Mapemphero ako ndi zachifundo zako zafika pamaso pa Mulungu ngati chikumbutso. 5Tsopano tuma anthu apite ku Yopa kuti akayitane munthu dzina lake Simoni Petro. 6Iye akukhala ndi Simoni mmisiri wa zikopa, amene nyumba yake ili mʼmbali mwa nyanja.”

7Mngeloyo anayankhula naye anachoka, Korneliyo anayitana antchito ake awiri ndiponso msilikali mmodzi wa iwo amene ankamutumikira yemwe ankapembedza Mulungu. 8Iye anawafotokozera zonse zimene zinachitika ndipo anawatuma kuti apite ku Yopa.

Masomphenya a Petro

9Mmawa mwake, nthawi ili ngati 12 koloko anthuwo atayandikira mzindawo, Petro anakwera pa denga kukapemphera. 10Iye anamva njala ndipo anafuna chakudya, ndipo akukonza chakudyacho, iye anachita ngati wakomoka. 11Iye anaona kuthambo kutatsekuka, ndi chinthu china chikutsitsidwa pansi chooneka ngati chinsalu chachikulu chomangidwa pa msonga zake zinayi. 12Mʼmenemo munali nyama zonse zamiyendo inayi pamodzinso ndi zokwawa za dziko lapansi ndiponso mbalame zamlengalenga. 13Petro anamva mawu akuti, “Petro, dzuka, ipha nudye.”

14Petro anayankha kuti, “Ayi, Ambuye! Ine sindinadyepo kanthu kosayeretsedwa kapena konyansa.”

15Petro anamvanso kachiwiri mawu akuti, “Usachiyese chonyansa chimene Mulungu wachiyeretsa.”

16Zimenezi zinachitika katatu ndipo nthawi yomweyo chinsalu chija chinatengedwanso kupita kumwamba.

17Petro akuganizira za tanthauzo la masomphenyawo, anthu amene Korneliyo anawatuma anapeza kumene kunali nyumba ya Simoni ndipo anayima pa chipata. 18Iwo anayitana nafunsa ngati Simoni amene amadziwika ndi dzina loti Petro amakhala kumeneko.

19Petro akuganizirabe za masomphenyawo, Mzimu Woyera anati kwa iye, “Simoni, anthu atatu akukufunafuna. 20Dzuka, tsika. Usakayike upite nawo pakuti ndawatuma ndine.”

21Petro anatsika ndipo anati kwa anthuwo, “Amene mukufunayo ndine. Mwabwera kuno chifukwa chiyani?”

22Anthuwo anayankha kuti, “Ife tachokera kwa Korneliyo, mkulu woyangʼanira asilikali 100. Iye ndi munthu wolungama ndiponso woopa Mulungu, amene amalemekezedwa ndi Ayuda onse. Mngelo woyera anamuwuza kuti mupite ku nyumba yake kuti akamve mawu amene inu mukanene.” 23Pamenepo Petro anawalowetsa mʼnyumba ndipo anawasamala ngati alendo ake. Mmawa mwake Petro ananyamuka napita nawo ndipo abale ena a ku Yopa anapita naye pamodzi.

Petro ku Nyumba ya Korneliyo

24Tsiku linalo Petro anafika ku Kaisareya. Korneliyo anawadikirira ndipo anali atawasonkhanitsa pamodzi abale ake ndi abwenzi ake a pamtima. 25Petro akulowa mʼnyumba, Korneliyo anakumana naye ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake namulambira. 26Koma Petro anamuyimiritsa nati, “Imirira, inenso ndine munthu ngati iwe.”

27Akuyankhula naye, Petro analowa mʼnyumba ndipo anapeza gulu lalikulu la anthu litasonkhana. 28Iye anawawuza kuti, “Inu mukudziwa bwino kuti ndi kutsutsana ndi lamulo ngati Myuda ayanjana ndi Mkunja kapena kuyendera wina aliyense wa mtundu wina. Koma Mulungu wandionetsa ine kuti ndisatchule munthu aliyense kuti ndi wosayenera kapena wonyansa. 29Nʼchifukwa chake ndabwera mosawiringula pamene munandiyitana. Tsopano ndikufunseni,” Mwandiyitanira chiyani?

30Komeliyo anayankha kuti, “Masiku anayi apitawo, nthawi yonga yomwe ino, 3 koloko masana ndimapemphera mʼnyumba mwanga. Mwadzidzidzi patsogolo panga panayimirira munthu wovala zovala zonyezimira. 31Ndipo anati, ‘Korneliyo, Mulungu wamva mapemphero ako ndipo wakumbukira mphatso zako kwa osauka. 32Tuma anthu ku Yopa akayitane Simoni wotchedwa Petro. Iye akukhala mʼnyumba ya Simoni mmisiri wazikopa amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.’ 33Nʼchifukwa chake ndinatumiza anthu nthawi yomweyo ndipo mwachita bwino kuti mwabwera. Tsopano ife tonse tili pano pamaso pa Mulungu kuti timve zonse zimene Ambuye akukulamulani kuti mutiwuze ife.”

34Ndipo Petro anayamba kuyankhula nati, “Zoonadi, tsopano ndazindikira kuti Mulungu sakondera. 35Koma amalandira anthu a mtundu uli wonse amene amaopa Iye ndiponso kuchita chilungamo. 36Uwu ndi uthenga umene Mulungu anatumiza kwa Aisraeli, kulalikira Uthenga Wabwino wamtendere mwa Yesu Khristu amene ndi Ambuye wa onse. 37Inu mukudziwa zimene zinachitika ku Yudeya konse, kuyambira ku Galileya pambuyo pa ubatizo umene Yohane analalikira, 38kuti Mulungu, anamudzoza Yesu, wa ku Nazareti ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu ndiponso mmene Iye anapita nachita zabwino ndi kuchiritsa onse amene anali pansi pa mphamvu ya mdierekezi, popeza kuti Mulungu anali naye.

39“Ife ndife mboni za zonse zimene anachita mʼdziko la Ayuda ndiponso ku Yerusalemu. Anamupha Iye pakumupachika pa mtengo, 40koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa pa tsiku lachitatu, ndipo analola kuti aonekere poyera. 41Iye sanaonekere kwa anthu onse koma kwa mboni zimene Mulungu anazisankhiratu, kwa ife amene timadya ndi kumwa naye atauka kwa akufa. 42Iye anatilamulira ife kuti tilalikire kwa anthu ndi kuchitira umboni kuti Iye ndiye amene Mulungu anamusankha kukhala woweruza wa amoyo ndi akufa. 43Aneneri onse achitira Iye umboni kuti aliyense amene akhulupirira Iye amakhululukidwa machimo chifukwa cha dzina lake.”

44Petro akuyankhulabe mawu amenewa, Mzimu Woyera unatsikira pa onse amene amamva uthengawo. 45Abale a mdulidwe omwe anabwera ndi Petro anadabwa kuona kuti mphatso ya Mzimu Woyera yapatsidwanso kwa anthu a mitundu ina. 46Pakuti anamva iwo akuyankhula mʼmalilime ndi kuyamika Mulungu. Ndipo Petro anati, 47“Kodi alipo amene angawaletse anthu awa kubatizidwa mʼmadzi? Iwotu alandira Mzimu Woyera monga ifenso.” 48Tsono iye analamula kuti abatizidwe mʼdzina la Yesu Khristu. Ndipo anthu aja anamupempha Petro kuti akhale nawo masiku angapo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Деяния 10:1-48

Видение Корнилия

1В Кесарии был человек по имени Корнилий, римский офицер из полка, носившего название Италийский. 2Корнилий, как и вся его семья, был человеком благочестивым и боящимся Аллаха10:2 Боящиеся Аллаха – так назывались представители разных народов, которые поверили в единого Бога, но ещё полностью не перешли в религию иудеев, т. е. не прошли надлежащий обряд водного погружения и не были обрезаны, как того требовал Таурат., он щедро раздавал милостыню и постоянно молился Аллаху10:2 Несмотря на то что Корнилий был человеком благочестивым, он тем не менее нуждался в спасении (см. 11:14).. 3Однажды около трёх часов дня10:3 То есть когда Корнилий совершал иудейскую молитву «минха», подобную арабской послеполуденной молитве «салату-ль-акр» (см. 10:30 и сноску на 3:1). Корнилию было видение. Он ясно видел ангела от Аллаха, который явился ему и сказал:

– Корнилий!

4Корнилий взглянул на него в ужасе и сказал:

– Что, владыка?

Ангел ответил:

– Аллах вспомнил о тебе, потому что твои молитвы и милостыни вознеслись к Нему, как приятный запах жертвоприношения. 5Пошли людей в Иоппию, чтобы они позвали Шимона, которого называют Петиром, 6он остановился у кожевника Шимона, в доме у моря.

7Когда ангел, говоривший с ним, ушёл, Корнилий позвал двух своих слуг и благочестивого солдата, исполнявшего его личные поручения. 8Пересказав им всё, что произошло, он послал их в Иоппию.

Видение Петира

9В полдень следующего дня, когда посланные уже подходили к городу, Петир поднялся на крышу дома помолиться10:9 На Ближнем Востоке дома имели плоскую крышу, на которую вела наружная лестница.. 10Он был голоден и хотел есть. Пока готовили пищу, Петиру было видение. 11Он видел раскрытые небеса и нечто похожее на широкое полотно, которое опускалось на землю, придерживаемое за четыре конца. 12В этом полотне были всякие виды четвероногих животных, пресмыкающиеся и птицы. 13Затем голос сказал ему:

– Встань, Петир, заколи и съешь.

14– Ни в коем случае, Владыка! – ответил Петир. – Я сроду не ел ничего осквернённого или ритуально нечистого10:14 Таурат подразделяет животных на ритуально чистых, разрешённых для употребления человеком в пищу, и на нечистых, употребление мяса которых запрещается и влечёт за собой ритуальное осквернение (см. Лев. 11). Отсюда и происходит отказ от употребления свинины в странах Центральной Азии..

15Тогда голос сказал ему во второй раз:

– Не называй нечистым то, что Аллах очистил.

16Так было три раза, и тотчас полотно было поднято на небо.

Петир идёт в дом Корнилия

17Петир всё недоумевал, что бы значило это видение, когда люди, посланные Корнилием, расспросив про дом Шимона, подошли и остановились у ворот. 18Они стали спрашивать, здесь ли остановился Шимон, называемый Петиром. 19Петир всё ещё обдумывал видение, когда Дух сказал ему:

– Тебя ищут три человека. 20Вставай и спускайся вниз. Иди с ними без колебаний, потому что это Я их послал.

21Петир спустился вниз и сказал этим людям:

– Я тот, кого вы ищете. По какому делу вы пришли?

22Они ответили:

– Римский офицер Корнилий, человек праведный и боящийся Аллаха, уважаемый всем иудейским народом, получил от святого ангела повеление пригласить тебя в свой дом и выслушать, что ты ему скажешь.

23Тогда Петир пригласил их войти в дом и оказал им гостеприимство.

Петир в доме Корнилия

На следующий день Петир отправился с ними в сопровождении нескольких братьев из Иоппии. 24На другой день они прибыли в Кесарию. Корнилий уже ждал их, созвав своих родственников и близких друзей. 25Когда Петир пришёл, Корнилий встретил его и, павши к его ногам, поклонился ему. 26Но Петир поднял его, сказав:

– Встань, я тоже человек.

27Разговаривая с Корнилием, Петир вошёл в дом, где уже собралось много народу. 28Он сказал им:

– Вы сами знаете, что иудею возбраняется общаться с иноплеменником и заходить к нему в дом10:28 Закон нигде напрямую не запрещает иудеям входить в дома иноплеменников. Но все же этот запрет логически вытекал из Закона. Евреям было запрещено есть нечистую для них пищу, приготовленную в языческих домах, чтобы не оскверниться. Кроме того, Закон и ритуальные постановления о пище говорили о святости и особой роли Исраила, об их принадлежности Самому Всевышнему (см. Исх. 19:5-6; Лев. 20:25-26), и это значило, что им не следует соприкасаться с морально и духовно «нечистыми» язычниками.. Но Аллах показал мне, что я ни одного человека не должен называть осквернённым или нечистым, 29и поэтому, когда за мной пришли, я пошёл без возражений. Позвольте же мне спросить теперь, зачем вы послали за мной?

30Корнилий ответил:

– Три дня назад в это самое время, в три часа дня я молился в своём доме, как вдруг передо мной предстал человек в сверкающей одежде. 31«Корнилий, – сказал он, – твоя молитва услышана, и твои милостыни вспомянуты Аллахом. 32Пошли людей в Иоппию за Шимоном, которого ещё называют Петиром, он гостит в доме кожевника Шимона, что у моря». 33Я сразу послал за тобой, и хорошо, что ты пришёл. Сейчас все мы здесь, перед Аллахом, и хотим выслушать то, что Вечный повелел тебе сказать.

34Петир начал говорить:

– Теперь я понимаю, что Аллах действительно беспристрастен, 35и в каждом народе Ему угоден тот, кто боится Его и поступает по правде! 36Он послал народу Исраила Радостную Весть о том, что мы можем иметь мир с Ним через Ису аль-Масиха, Который является Повелителем всех людей. 37Вы знаете о тех событиях, которые происходили по всей Иудее, начиная от Галилеи, после того как Яхия начал призывать народ пройти обряд погружения в воду10:37 Или: «обряд омовения»; также в ст. 47 и 48.: 38о том, как Аллах помазал Святым Духом и наделил силой Ису из Назарета, и Он ходил, совершая добрые дела и исцеляя всех, кто был во власти Иблиса, потому что с Ним был Аллах. 39Мы свидетели всему тому, что Иса делал в Иерусалиме и по всей стране иудеев. Его убили, повесив на дереве10:39 См. сноску на 5:30., 40но Аллах на третий день воскресил Его и дал Ему являться людям – 41не всему народу, а заранее избранным Аллахом свидетелям, то есть нам, и мы ели и пили с Ним после того, как Он воскрес из мёртвых. 42Он повелел нам возвещать людям Радостную Весть и свидетельствовать о том, что именно Ему Аллах определил судить живых и мёртвых. 43О Нём свидетельствуют все пророки, утверждая, что каждый верующий в Него получает прощение грехов благодаря Его имени.

44Петир ещё говорил это, когда на всех слушавших его сошёл Святой Дух. 45Верующие из обрезанных10:45 То есть из иудеев., которые пришли с Петиром, были удивлены, что дар Святого Духа был излит и на уверовавших язычников, 46потому что они слышали, как те говорили на других языках и славили Аллаха. Тогда Петир сказал:

47– Может ли кто-нибудь помешать этим людям, которые получили Святого Духа так же, как и мы, пройти обряд погружения в воду?

48И он велел им пройти обряд погружения в воду в знак единения с Исой аль-Масихом. Потом хозяева попросили Петира остаться с ними ещё на несколько дней.