Machitidwe a Atumwi 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 1:1-26

Lonjezo la Mzimu Woyera

1Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa, 2mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha. 3Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi. 4Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani. 5Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”

Yesu Akwera Kumwamba

6Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”

7Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo. 8Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”

9Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.

10Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo. 11Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”

Matiyasi Alowa Mʼmalo mwa Yudasi Isikarioti

12Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo. 13Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo. 14Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.

15Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120). 16Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu. 17Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”

18(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka. 19Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).

20Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti,

“Nyumba yake isanduke bwinja,

ndipo pasakhale wogonamo.

Ndiponso,

“Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.

21Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe, 22kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”

23Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi. 24Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa 25kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.” 26Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

מעשי השליחים 1:1‏-26

1‏-2תאופילוס היקר,

במכתבי הראשון1‏.1‏-2 א 1‏-2 ראה הבשורה על פי לוקס א 1 סיפרתי לך על חייו, מעשיו ותורתו של ישוע המשיח, וכיצד עלה לשמים, לאחר שנתן לשליחיו הנבחרים הוראות נוספות בגבורת רוח הקודש. 3במשך ארבעים יום לאחר צליבתו נגלה ישוע אל השליחים פעמים אחדות, והוכיח להם בדרכים שונות שהוא אכן חי. בהזדמנויות אלה הוא גם שוחח איתם על מלכות האלוהים.

4באחת הפגישות האלה הורה ישוע לתלמידיו שלא יעזבו את ירושלים עד שיבוא עליהם רוח הקודש, כפי שהבטיח להם האב. ישוע שוחח איתם על כך פעמים רבות בעבר.

5”יוחנן הטביל אתכם במים,“ הזכיר להם ישוע, ”אולם בעוד ימים אחדים תיטבלו ברוח הקודש!“

6כשנגלה אליהם ישוע בפעם אחרת, שאלו אותו: ”אדון, האם אתה עומד להשיב את המלכות לישראל?“

7”האב הוא הקובע תאריכים אלה,“ ענה ישוע, ”ואינכם צריכים לדעת אותם. 8אולם כשרוח הקודש יצלח עליכם, תקבלו כוח וסמכות להיות עדים לי בירושלים, ביהודה ושומרון ועד קצה העולם.“

9זמן קצר לאחר מכן עלה ישוע לשמים לעיני תלמידיו, ונעלם בתוך ענן. 10בעוד התלמידים מאמצים את עיניהם כדי לזכות במבט נוסף, עמדו ביניהם לפתע שני אנשים לבושים גלימות לבנות, 11ואמרו: ”אנשי הגליל, מדוע אתם עומדים ומביטים לשמים? ישוע אמנם עלה לשמים, אך יום אחד הוא יחזור בדיוק כפי שהלך מכם!“

12כשקרה הדבר הזה הם היו בהר־הזיתים, ועתה חזרו ברגל לירושלים (מרחק של פחות מקילומטר).

13‏-14כשהגיעו העירה, הם התאספו לתפילה בחדר העלייה שבו גרו. באסיפה זאת נכחו האנשים הבאים:

פטרוס,

יוחנן ויעקב,

‎אַנְדְּרֵי,

פיליפוס,

תומא,

בר־תלמי,

מתתיהו,

יעקב בן־חלפי,

שמעון מהקנאים,

יהודה בן־יעקב

ואחיו של ישוע.

היו שם גם נשים אחדות, וביניהן אמו של ישוע.

15אסיפת התפילה נמשכה ימים אחדים, ויום אחד, כשנכחו שם מאה ועשרים איש, קם שמעון פטרוס ואמר:

16”אחים, נבואות התנ״ך צריכות היו להתקיים בנוגע ליהודה, אשר בגד בישוע והוביל אליו את ההמון, שהרי רוח הקודש דיבר על כך לפני זמן רב בפי דוד המלך. 17יהודה היה אחד מאיתנו; הוא נבחר בדיוק כמונו להיות שליח. 18בכסף שקיבל תמורת הבגידה הוא קנה לעצמו שדה, ושם מצא את מותו – הוא נפל ארצה על פניו, בטנו נבקעה ומעיו נשפכו החוצה. 19הידיעה על מותו התפשטה במהירות בין כל תושבי ירושלים, והם מכנים את המקום ההוא בשפתם1‏.19 א 19 בארמית. ’חקל דמא‘, שפירושו ’שדה־הדם‘. 20דוד המלך ניבא על כך בתהלים, ואמר שביתו יהיה שומם ושאיש לא יישב בו. ובמקום אחר אמר דוד שתפקידו (של יהודה) יינתן למישהו אחר.1‏.20 א 20 תהלים סט 26; קט 8

21‏-22”משום כך עלינו לבחור במישהו אחר, אשר ימלא את מקומו של יהודה, ויצטרף אלינו בעדותנו על תחייתו של ישוע אדוננו. הבה נבחר באדם שהיה איתנו מאז הימים הראשונים – מאז שישוע נטבל על־ידי יוחנן ועד שנלקח מאיתנו לשמים.“

23הנאספים נקבו בשני שמות: יוסף יוסטוס (שנקרא גם ”בר־שבא“) ומתתיהו. 24‏-25לאחר מכן התפללו כולם וביקשו שייבחר האדם הנכון. ”אלוהים,“ התפללו, ”אתה המכיר כל לב, הראה נא לנו במי מהשניים בחרת למלא את מקומו של יהודה הבוגד, שהלך למקום הראוי לו!“

26הם הפילו גורל כדי לבחור בין שני המועמדים, ושמו של מתתיהו עלה בגורל. באותו יום הצטרף מתתיהו אל אחד־עשר השליחים.