Luka 9 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 9:1-62

Yesu Atuma Ophunzira ake Khumi ndi Awiri

1Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda. 2Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala. 3Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera. 4Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo. 5Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.” 6Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.

7Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa, 8ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso. 9Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

10Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida. 11Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.

12Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”

13Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.”

Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.” 14(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000).

Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.” 15Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi. 16Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu. 17Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.

Petro Avomereza Khristu

18Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”

19Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”

20Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?”

Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”

Yesu Aneneratu za Imfa yake

21Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi. 22Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”

23Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine. 24Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa. 25Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini? 26Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera. 27Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

28Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera. 29Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri. 30Anthu awiri, Mose ndi Eliya, 31anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu. 32Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye. 33Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).

34Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta. 35Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.” 36Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.

Kuchiritsidwa kwa Mwana Wogwidwa ndi Chiwanda

37Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye. 38Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu. 39Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga. 40Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”

41Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”

42Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake. 43Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu.

Yesu Abwereza Kunena za Imfa yake

Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake, 44“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.” 45Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.

Wamkulu Ndani?

46Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo. 47Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake. 48Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”

49Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”

50Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”

A Samariya Akana Yesu

51Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu, 52ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira, 53koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu. 54Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?” 55Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula, 56ndipo iwo anapita ku mudzi wina.

Kutsatira Yesu

57Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”

58Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”

59Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.”

Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”

60Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”

61Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”

62Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 9:1-62

مأموريت دوازده شاگرد عيسی

1روزی عيسی دوازده شاگرد خود را فرا خواند و به ايشان قدرت و اقتدار داد تا ارواح پليد را از وجود ديوانگان بيرون كنند و بيماران را شفا بخشند. 2آنگاه ايشان را فرستاد تا فرا رسيدن ملكوت خدا را به مردم اعلام نمايند و بيماران را شفا دهند.

3پيش از آنكه به راه افتند، عيسی به آنان فرمود: «در اين سفر، هيچ چيز با خود نبريد، نه چوبدستی، نه كوله‌بار، نه خوراک، نه پول و نه لباس اضافی. 4به هر شهری كه رفتيد، فقط در يک خانه میهمان باشيد. 5اگر اهالی شهری به پيغام شما توجهی نكردند، به هنگام ترک آن شهر، حتی گرد و خاک آنجا را از پايهايتان بتكانيد تا بدانند كه خدا نسبت به آنان غضبناک است!»

6پس شاگردان، شهر به شهر و آبادی به آبادی می‌گشتند و پيغام انجيل را به مردم می‌رساندند و بيماران را شفا می‌بخشيدند.

مرگ يحيی

7وقتی كه هيروديس حكمران جليل خبر معجزات عيسی را شنيد، نگران و پريشان شد، زيرا بعضی درباره عيسی می‌گفتند كه او همان يحيای تعميددهنده است كه زنده شده است. 8عده‌ای ديگر نيز می‌گفتند كه او همان الياس است كه ظهور كرده و يا يكی از پيغمبران قديمی است كه زنده شده است. اين گونه شايعات همه جا به گوش می‌رسيد.

9اما هيروديس می‌گفت: «من خود سر يحيی را از تنش جدا كردم! پس اين ديگر كيست كه اين داستانهای عجيب و غريب را درباره‌اش می‌شنوم؟» از این رو مشتاق بود كه عيسی را ملاقات كند.

غذا دادن به پنج هزار مرد

10پس از مدتی، رسولان برگشتند و عيسی را از آنچه كرده بودند، آگاه ساختند. آنگاه عيسی همراه ايشان، به دور از چشم مردم، به سوی شهر بيت‌صيدا به راه افتاد. 11اما عده بسياری از مقصد او باخبر شدند و به دنبالش شتافتند. عيسی نيز با خوشرويی ايشان را پذيرفت و باز درباره ملكوت خدا ايشان را تعليم داد و بيماران را شفا بخشيد.

12نزديک غروب، دوازده شاگرد عيسی آمده، به او گفتند: «مردم را مرخص فرما تا به آبادی‌های اطراف بروند و برای گذراندن شب، جا و خوراک بيابند، چون در اين بيابان، چيزی برای خوردن پيدا نمی‌شود.»

13عيسی جواب داد: «شما خودتان به ايشان خوراک بدهيد!»

شاگردان با تعجب گفتند: «چگونه؟ ما حتی برای خودمان، چيزی جز پنج نان و دو ماهی نداريم! شايد می‌خواهی كه برويم و برای تمام اين جمعيت غذا بخريم؟» 14فقط تعداد مردها در آن جمعيت، حدود پنج هزار نفر بود.

آنگاه عيسی فرمود: «به مردم بگوييد كه در دسته‌های پنجاه نفری، بر روی زمين بنشينند.» 15شاگردان همه را نشاندند.

16عيسی آن پنج نان و دو ماهی را در دست گرفت و به سوی آسمان نگاه كرد و شكر نمود. سپس نانها را تكه‌تكه كرد و به شاگردانش داد تا در ميان مردم تقسيم كنند. 17همه خوردند و سير شدند و دوازده سبد نيز از تكه‌های باقيمانده، اضافه آمد.

اعتقاد پطرس درباره عيسی

18يک روز كه عيسی به تنهايی دعا می‌كرد، شاگردانش نزد او آمدند و او از ايشان پرسيد: «به نظر مردم، من كه هستم؟»

19جواب دادند: «يحيای تعميددهنده، يا الياس نبی، و يا يكی از پيغمبران قديم كه زنده شده است.»

20آنگاه از ايشان پرسيد: «شما چه؟ شما مرا كه می‌دانيد؟»

پطرس در جواب گفت: «تو مسيح موعود هستی!»

عيسی مرگ خود را پيشگويی می‌كند

21اما عيسی ايشان را اكيداً منع كرد كه اين موضوع را با كسی در میان نگذارند. 22سپس به ايشان فرمود: «لازم است كه من رنج و عذاب بسيار بكشم. بزرگان قوم، كاهنان اعظم و علمای دين مرا محكوم كرده، خواهند كشت. اما من روز سوم زنده خواهم شد!»

23سپس به همه فرمود: «هر كه می‌خواهد مرا پيروی كند، بايد از خواسته‌ها و آسايش خود چشم بپوشد و هر روز، زحمات و سختیها را همچون صليب بر دوش بكشد و به دنبال من بيايد. 24هر كه در راه من جانش را از دست بدهد، حيات جاودان را خواهد يافت، اما هر كه بكوشد جانش را حفظ كند، حيات جاودان را از دست خواهد داد. 25پس چه فايده‌ای دارد كه شخص تمام دنيا را به چنگ بياورد، اما حيات جاويد را از دست بدهد؟

26«هر كه در اين جهان از من و سخنان من عار داشته باشد، من نيز وقتی در جلال خود و جلال پدر، با فرشتگان مقدس به جهان بازگردم، از او عار خواهم داشت. 27اما يقين بدانيد كه در اينجا كسانی ايستاده‌اند كه تا ملكوت خدا را نبينند، نخواهند مرد.»

شاگردان جلال مسيح را می‌بينند

28هشت روز پس از اين سخنان، عيسی به همراه پطرس، يعقوب و يوحنا، بر فراز تپه‌ای برآمد تا دعا كند. 29به هنگام دعا، ناگهان چهره عيسی نورانی شد و لباس او از سفيدی، چشم را خيره می‌كرد. 30‏-31در همان حال، دو مرد، يعنی موسی و الياس، با ظاهری پرشكوه و نورانی ظاهر شدند و با عيسی درباره مرگ او كه می‌بايست طبق خواست خدا، بزودی در اورشليم واقع گردد، به گفتگو پرداختند.

32اما در اين هنگام، پطرس و دوستانش را خواب در ربوده بود. وقتی بيدار شدند، عيسی و آن دو مرد را غرق در نور و جلال ديدند. 33هنگامی كه موسی و الياس آن محل را ترک می‌كردند پطرس كه دستپاچه بود و نمی‌دانست چه می‌گويد، به عيسی گفت: «استاد، چه عالی است! همین‌جا بمانيم و سه سايبان بسازيم، يكی برای تو، يكی برای موسی و يكی هم برای الياس.»

34سخن پطرس هنوز تمام نشده بود كه ابری درخشان پديدار گشت و وقتی بر ايشان سايه انداخت، شاگردان را ترس فرا گرفت. 35آنگاه از ابر ندايی در رسيد كه «اينست پسر محبوب من. سخنان او را بشنويد!»

36وقتی كه ندا خاتمه يافت، متوجه شدند كه عيسی تنهاست. آنان تا مدتها، به كسی درباره اين واقعه چيزی نگفتند.

شفای يک پسر غشی

37روز بعد، وقتی از تپه پايين می‌آمدند، با جمعيت بزرگی روبرو شدند. 38ناگهان مردی از ميان جمعيت فرياد زد: «استاد، التماس می‌كنم بر پسرم، كه تنها فرزندم است، نظر لطف بيندازی، 39چون يک روح پليد مرتب داخل وجود او می‌شود و او را به فرياد كشيدن وا می‌دارد. روح پليد او را متشنج می‌كند، به طوری كه از دهانش كف بيرون می‌آيد. او هميشه به پسرم حمله می‌كند و به سختی او را رها می‌سازد. 40از شاگردانت درخواست كردم كه اين روح را از وجود پسرم بيرون كنند، اما نتوانستند.»

41عيسی فرمود: «شما مردم اين زمانه، چقدر سرسخت و بی‌ايمان هستيد! تا كی اين وضع را تحمل كنم؟ پسر را نزد من بياوريد!»

42در همان هنگام كه پسر را می‌آوردند، روح پليد او را تكان سختی داد و بر زمين زد. پسر می‌غلتيد و دهانش كف می‌كرد. اما عيسی به روح پليد دستور داد كه بيرون بيايد. به اين ترتيب آن پسر را شفا بخشيد و به پدرش سپرد. 43مردم همه از قدرت خدا شگفت‌زده شده بودند.

عيسی بار دیگر درباره مرگش پيشگويی می‌کند

در همان حال كه همه با حيرت از كارهای عجيب عيسی تعريف می‌كردند، او به شاگردان خود فرمود: 44«به آنچه می‌گويم، خوب توجه كنيد: مرا كه مسيح هستم بزودی به دست مردم تسليم خواهند كرد.» 45اما شاگردان منظور او را نفهميدند، چون ذهنشان كور شده بود و می‌ترسيدند در اين باره از او سؤال كنند.

چه كسی بزرگتر است؟

46سپس بين شاگردان عيسی اين بحث درگرفت كه چه كسی از همه بزرگتر است! 47عيسی كه متوجه افكار ايشان شده بود، كودكی را نزد خود خواند، 48و به ايشان فرمود: «هر كه افرادی اينچنين كوچک را بپذيرد، مرا پذيرفته است؛ و هر كه مرا پذيرد، در حقيقت خدايی را كه مرا فرستاده پذيرفته است. بزرگی شما به اين بستگی دارد كه تا چه اندازه ديگران را می‌پذيريد.»

بر زبان راندن نام عيسی

49شاگرد او، يوحنا گفت: «استاد، ما شخصی را ديديم كه با بر زبان آوردن نام تو، ارواح پليد را از وجود ديوانه‌ها بيرون می‌كرد. ما نيز سعی كرديم مانع كار او شويم، چون از گروه ما نبود!»

50عيسی فرمود: «مانع او نشويد، چون كسی كه بر ضد شما نباشد، از شماست.»

حركت عيسی به سوی اورشليم

51هنگامی كه زمان بازگشت عيسی به آسمان نزديک شد، با عزمی راسخ به سوی اورشليم به راه افتاد. 52او چند نفر را جلوتر فرستاد تا در يكی از دهكده‌های سامری‌نشين، محلی برای اقامت ايشان آماده سازند. 53اما اهالی آن دهكده، ايشان را نپذيرفتند چون می‌دانستند كه عازم اورشليم هستند. (سامريان و يهوديان، دشمنی ديرينه‌ای با يكديگر داشتند.)

54وقتی فرستادگان برگشتند و اين خبر را آوردند، يعقوب و يوحنا به عيسی گفتند: «استاد، آيا می‌خواهی از خدا درخواست كنيم كه از آسمان آتش بفرستد و ايشان را از بين ببرد، همانگونه كه الياس نيز كرد؟» 55اما عيسی ايشان را سرزنش نمود. 56بنابراين از آنجا به آبادی ديگری رفتند.

بهای پيروی از عيسی

57در بين راه، شخصی به عيسی گفت: «می‌خواهم هر جا كه می‌روی، تو را پيروی كنم!»

58عيسی در جواب فرمود: «روباه‌ها، لانه دارند و پرندگان، آشيانه! اما من حتی جايی برای خوابيدن ندارم!»

59يكبار نيز او كسی را دعوت كرد تا پيروی‌اش نمايد. آن شخص پذيرفت اما خواست كه اين كار را به پس از مرگ پدرش موكول كند. 60عيسی به او گفت: «بگذار كسانی در فكر اين چيزها باشند كه حيات جاودانی ندارند. وظيفه تو اينست كه بيايی و مژده ملكوت خدا را در همه جا اعلام نمايی.»

61شخصی نيز به عيسی گفت: «خداوندا، من حاضرم تو را پيروی كنم. اما بگذار اول بروم و از خانواده‌ام اجازه بگيرم!»

62عيسی به او فرمود: «كسی كه تمام هوش و حواسش متوجه خدمت به من نباشد، لايق اين خدمت نيست!»