Luka 9 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 9:1-62

Yesu Atuma Ophunzira ake Khumi ndi Awiri

1Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda. 2Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala. 3Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera. 4Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo. 5Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.” 6Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.

7Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa, 8ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso. 9Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

10Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida. 11Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.

12Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”

13Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.”

Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.” 14(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000).

Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.” 15Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi. 16Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu. 17Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.

Petro Avomereza Khristu

18Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”

19Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”

20Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?”

Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”

Yesu Aneneratu za Imfa yake

21Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi. 22Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”

23Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine. 24Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa. 25Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini? 26Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera. 27Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

28Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera. 29Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri. 30Anthu awiri, Mose ndi Eliya, 31anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu. 32Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye. 33Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).

34Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta. 35Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.” 36Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.

Kuchiritsidwa kwa Mwana Wogwidwa ndi Chiwanda

37Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye. 38Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu. 39Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga. 40Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”

41Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”

42Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake. 43Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu.

Yesu Abwereza Kunena za Imfa yake

Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake, 44“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.” 45Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.

Wamkulu Ndani?

46Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo. 47Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake. 48Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”

49Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”

50Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”

A Samariya Akana Yesu

51Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu, 52ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira, 53koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu. 54Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?” 55Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula, 56ndipo iwo anapita ku mudzi wina.

Kutsatira Yesu

57Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”

58Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”

59Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.”

Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”

60Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”

61Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”

62Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”

New International Version – UK

Luke 9:1-62

Jesus sends out the Twelve

1When Jesus had called the Twelve together, he gave them power and authority to drive out all demons and to cure diseases, 2and he sent them out to proclaim the kingdom of God and to heal those who were ill. 3He told them: ‘Take nothing for the journey – no staff, no bag, no bread, no money, no extra shirt. 4Whatever house you enter, stay there until you leave that town. 5If people do not welcome you, leave their town and shake the dust off your feet as a testimony against them.’ 6So they set out and went from village to village, proclaiming the good news and healing people everywhere.

7Now Herod the tetrarch heard about all that was going on. And he was perplexed because some were saying that John had been raised from the dead, 8others that Elijah had appeared, and still others that one of the prophets of long ago had come back to life. 9But Herod said, ‘I beheaded John. Who, then, is this I hear such things about?’ And he tried to see him.

Jesus feeds the five thousand

10When the apostles returned, they reported to Jesus what they had done. Then he took them with him and they withdrew by themselves to a town called Bethsaida, 11but the crowds learned about it and followed him. He welcomed them and spoke to them about the kingdom of God, and healed those who needed healing.

12Late in the afternoon the Twelve came to him and said, ‘Send the crowd away so they can go to the surrounding villages and countryside and find food and lodging, because we are in a remote place here.’

13He replied, ‘You give them something to eat.’

They answered, ‘We have only five loaves of bread and two fish – unless we go and buy food for all this crowd.’ 14(About five thousand men were there.)

But he said to his disciples, ‘Make them sit down in groups of about fifty each.’ 15The disciples did so, and everyone sat down. 16Taking the five loaves and the two fish and looking up to heaven, he gave thanks and broke them. Then he gave them to the disciples to distribute to the people. 17They all ate and were satisfied, and the disciples picked up twelve basketfuls of broken pieces that were left over.

Peter declares that Jesus is the Messiah

18Once when Jesus was praying in private and his disciples were with him, he asked them, ‘Who do the crowds say I am?’

19They replied, ‘Some say John the Baptist; others say Elijah; and still others, that one of the prophets of long ago has come back to life.’

20‘But what about you?’ he asked. ‘Who do you say I am?’

Peter answered, ‘God’s Messiah.’

Jesus predicts his death

21Jesus strictly warned them not to tell this to anyone. 22And he said, ‘The Son of Man must suffer many things and be rejected by the elders, the chief priests and the teachers of the law, and he must be killed and on the third day be raised to life.’

23Then he said to them all: ‘Whoever wants to be my disciple must deny themselves and take up their cross daily and follow me. 24For whoever wants to save their life will lose it, but whoever loses their life for me will save it. 25What good is it for someone to gain the whole world, and yet lose or forfeit their very self? 26Whoever is ashamed of me and my words, the Son of Man will be ashamed of them when he comes in his glory and in the glory of the Father and of the holy angels.

27‘Truly I tell you, some who are standing here will not taste death before they see the kingdom of God.’

The transfiguration

28About eight days after Jesus said this, he took Peter, John and James with him and went up onto a mountain to pray. 29As he was praying, the appearance of his face changed, and his clothes became as bright as a flash of lightning. 30Two men, Moses and Elijah, appeared in glorious splendour, talking with Jesus. 31They spoke about his departure,9:31 Greek exodos which he was about to bring to fulfilment at Jerusalem. 32Peter and his companions were very sleepy, but when they became fully awake, they saw his glory and the two men standing with him. 33As the men were leaving Jesus, Peter said to him, ‘Master, it is good for us to be here. Let us put up three shelters – one for you, one for Moses and one for Elijah.’ (He did not know what he was saying.)

34While he was speaking, a cloud appeared and covered them, and they were afraid as they entered the cloud. 35A voice came from the cloud, saying, ‘This is my Son, whom I have chosen; listen to him.’ 36When the voice had spoken, they found that Jesus was alone. The disciples kept this to themselves and did not tell anyone at that time what they had seen.

Jesus heals a demon-possessed boy

37The next day, when they came down from the mountain, a large crowd met him. 38A man in the crowd called out, ‘Teacher, I beg you to look at my son, for he is my only child. 39A spirit seizes him and he suddenly screams; it throws him into convulsions so that he foams at the mouth. It scarcely ever leaves him and is destroying him. 40I begged your disciples to drive it out, but they could not.’

41‘You unbelieving and perverse generation,’ Jesus replied, ‘how long shall I stay with you and put up with you? Bring your son here.’

42Even while the boy was coming, the demon threw him to the ground in a convulsion. But Jesus rebuked the impure spirit, healed the boy and gave him back to his father. 43And they were all amazed at the greatness of God.

Jesus predicts his death a second time

While everyone was marvelling at all that Jesus did, he said to his disciples, 44‘Listen carefully to what I am about to tell you: the Son of Man is going to be delivered into the hands of men.’ 45But they did not understand what this meant. It was hidden from them, so that they did not grasp it, and they were afraid to ask him about it.

46An argument started among the disciples as to which of them would be the greatest. 47Jesus, knowing their thoughts, took a little child and made him stand beside him. 48Then he said to them, ‘Whoever welcomes this little child in my name welcomes me; and whoever welcomes me welcomes the one who sent me. For it is the one who is least among you all who is the greatest.’

49‘Master,’ said John, ‘we saw someone driving out demons in your name and we tried to stop him, because he is not one of us.’

50‘Do not stop him,’ Jesus said, ‘for whoever is not against you is for you.’

Samaritan opposition

51As the time approached for him to be taken up to heaven, Jesus resolutely set out for Jerusalem. 52And he sent messengers on ahead, who went into a Samaritan village to get things ready for him; 53but the people there did not welcome him, because he was heading for Jerusalem. 54When the disciples James and John saw this, they asked, ‘Lord, do you want us to call fire down from heaven to destroy them9:54 Some manuscripts them, just as Elijah did?’ 55But Jesus turned and rebuked them. 56Then he and his disciples went to another village.

The cost of following Jesus

57As they were walking along the road, a man said to him, ‘I will follow you wherever you go.’

58Jesus replied, ‘Foxes have dens and birds have nests, but the Son of Man has nowhere to lay his head.’

59He said to another man, ‘Follow me.’

But he replied, ‘Lord, first let me go and bury my father.’

60Jesus said to him, ‘Let the dead bury their own dead, but you go and proclaim the kingdom of God.’

61Still another said, ‘I will follow you, Lord; but first let me go back and say goodbye to my family.’

62Jesus replied, ‘No-one who puts a hand to the plough and looks back is fit for service in the kingdom of God.’