Luka 9 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 9:1-62

Yesu Atuma Ophunzira ake Khumi ndi Awiri

1Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda. 2Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala. 3Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera. 4Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo. 5Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.” 6Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.

7Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa, 8ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso. 9Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

10Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida. 11Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.

12Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”

13Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.”

Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.” 14(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000).

Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.” 15Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi. 16Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu. 17Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.

Petro Avomereza Khristu

18Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”

19Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”

20Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?”

Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”

Yesu Aneneratu za Imfa yake

21Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi. 22Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”

23Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine. 24Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa. 25Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini? 26Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera. 27Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

28Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera. 29Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri. 30Anthu awiri, Mose ndi Eliya, 31anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu. 32Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye. 33Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).

34Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta. 35Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.” 36Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.

Kuchiritsidwa kwa Mwana Wogwidwa ndi Chiwanda

37Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye. 38Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu. 39Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga. 40Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”

41Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”

42Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake. 43Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu.

Yesu Abwereza Kunena za Imfa yake

Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake, 44“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.” 45Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.

Wamkulu Ndani?

46Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo. 47Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake. 48Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”

49Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”

50Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”

A Samariya Akana Yesu

51Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu, 52ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira, 53koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu. 54Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?” 55Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula, 56ndipo iwo anapita ku mudzi wina.

Kutsatira Yesu

57Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”

58Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”

59Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.”

Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”

60Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”

61Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”

62Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”

New International Reader’s Version

Luke 9:1-62

Jesus Sends Out the Twelve Disciples

1Jesus called together the 12 disciples. He gave them power and authority to drive out all demons and to heal sicknesses. 2Then he sent them out to announce God’s kingdom and to heal those who were sick. 3He told them, “Don’t take anything for the journey. Do not take a walking stick or a bag. Do not take any bread, money or extra clothes. 4When you are invited into a house, stay there until you leave town. 5Some people may not welcome you. If they don’t, leave their town and shake the dust off your feet. This will be a witness against the people living there.” 6So the 12 disciples left. They went from village to village. They announced the good news and healed people everywhere.

7Now Herod, the ruler of Galilee, heard about everything that was going on. He was bewildered, because some were saying that John the Baptist had been raised from the dead. 8Others were saying that Elijah had appeared. Still others were saying that a prophet of long ago had come back to life. 9But Herod said, “I had John’s head cut off. So who is it that I hear such things about?” And he tried to see Jesus.

Jesus Feeds the Five Thousand

10The disciples returned. They told Jesus what they had done. Then he took them with him. They went off by themselves to a town called Bethsaida. 11But the crowds learned about it and followed Jesus. He welcomed them and spoke to them about God’s kingdom. He also healed those who needed to be healed.

12Late in the afternoon the 12 disciples came to him. They said, “Send the crowd away. They can go to the nearby villages and countryside. There they can find food and a place to stay. There is nothing here.”

13Jesus replied, “You give them something to eat.”

The disciples answered, “We have only five loaves of bread and two fish. We would have to go and buy food for all this crowd.” 14About 5,000 men were there.

But Jesus said to his disciples, “Have them sit down in groups of about 50 each.” 15The disciples did so, and everyone sat down. 16Jesus took the five loaves and the two fish. He looked up to heaven and gave thanks. He broke them into pieces. Then he gave them to the disciples to give to the people. 17All of them ate and were satisfied. The disciples picked up 12 baskets of leftover pieces.

Peter Says That Jesus Is the Messiah

18One day Jesus was praying alone. Only his disciples were with him. He asked them, “Who do the crowds say I am?”

19They replied, “Some say John the Baptist. Others say Elijah. Still others say that one of the prophets of long ago has come back to life.”

20“But what about you?” he asked. “Who do you say I am?”

Peter answered, “God’s Messiah.”

Jesus Speaks About His Coming Death

21Jesus strongly warned them not to tell this to anyone. 22He said, “The Son of Man must suffer many things. The elders will not accept him. The chief priests and the teachers of the law will not accept him either. He must be killed and on the third day rise from the dead.”

23Then he said to all of them, “Whoever wants to follow me must say no to themselves. They must pick up their cross every day and follow me. 24Whoever wants to save their life will lose it. But whoever loses their life for me will save it. 25What good is it if someone gains the whole world but loses or gives up their very self? 26Suppose someone is ashamed of me and my words. The Son of Man will come in his glory and in the glory of the Father and the holy angels. Then he will be ashamed of that person.

27“What I’m about to tell you is true. Some who are standing here will not die before they see God’s kingdom.”

Jesus’ Appearance Is Changed

28About eight days after Jesus said this, he went up on a mountain to pray. He took Peter, John and James with him. 29As he was praying, the appearance of his face changed. His clothes became as bright as a flash of lightning. 30Two men, Moses and Elijah, appeared in shining glory. Jesus and the two of them talked together. 31They talked about how he would be leaving them soon. This was going to happen in Jerusalem. 32Peter and his companions had been very sleepy. But then they became completely awake. They saw Jesus’ glory and the two men standing with him. 33As the men were leaving Jesus, Peter spoke up. “Master,” he said to him, “it is good for us to be here. Let us put up three shelters. One will be for you, one for Moses, and one for Elijah.” Peter didn’t really know what he was saying.

34While he was speaking, a cloud appeared and covered them. The disciples were afraid as they entered the cloud. 35A voice came from the cloud. It said, “This is my Son, and I have chosen him. Listen to him.” 36When the voice had spoken, they found that Jesus was alone. The disciples kept quiet about this. They didn’t tell anyone at that time what they had seen.

Jesus Heals a Boy Who Is Controlled by an Evil Spirit

37The next day Jesus and those who were with him came down from the mountain. A large crowd met Jesus. 38A man in the crowd called out. “Teacher,” he said, “I beg you to look at my son. He is my only child. 39A spirit takes hold of him, and he suddenly screams. It throws him into fits so that he foams at the mouth. It hardly ever leaves him. It is destroying him. 40I begged your disciples to drive it out. But they couldn’t do it.”

41“You unbelieving and evil people!” Jesus replied. “How long do I have to stay with you? How long do I have to put up with you?” Then he said to the man, “Bring your son here.”

42Even while the boy was coming, the demon threw him into a fit. The boy fell to the ground. But Jesus ordered the evil spirit to leave the boy. Then Jesus healed him and gave him back to his father. 43They were all amazed at God’s greatness.

Jesus Speaks a Second Time About His Coming Death

Everyone was wondering about all that Jesus did. Then Jesus said to his disciples, 44“Listen carefully to what I am about to tell you. The Son of Man is going to be handed over to men.” 45But they didn’t understand what this meant. That was because it was hidden from them. And they were afraid to ask Jesus about it.

Who Is the Most Important Person?

46The disciples began to argue about which one of them would be the most important person. 47Jesus knew what they were thinking. So he took a little child and had the child stand beside him. 48Then he spoke to them. “Anyone who welcomes this little child in my name welcomes me,” he said. “And anyone who welcomes me welcomes the one who sent me. The one considered least important among all of you is really the most important.”

49“Master,” said John, “we saw someone driving out demons in your name. We tried to stop him, because he is not one of us.”

50“Do not stop him,” Jesus said. “Anyone who is not against you is for you.”

The Samaritans Do Not Welcome Jesus

51The time grew near for Jesus to be taken up to heaven. So he made up his mind to go to Jerusalem. 52He sent messengers on ahead. They went into a Samaritan village to get things ready for him. 53But the people there did not welcome Jesus. That was because he was heading for Jerusalem. 54The disciples James and John saw this. They asked, “Lord, do you want us to call down fire from heaven to destroy them?” 55But Jesus turned and commanded them not to do it. 56Then Jesus and his disciples went on to another village.

The Cost of Following Jesus

57Once Jesus and those who were with him were walking along the road. A man said to Jesus, “I will follow you no matter where you go.”

58Jesus replied, “Foxes have dens. Birds have nests. But the Son of Man has no place to lay his head.”

59He said to another man, “Follow me.”

But the man replied, “Lord, first let me go and bury my father.”

60Jesus said to him, “Let dead people bury their own dead. You go and tell others about God’s kingdom.”

61Still another person said, “I will follow you, Lord. But first let me go back and say goodbye to my family.”

62Jesus replied, “Suppose someone starts to plow and then looks back. That person is not fit for service in God’s kingdom.”