Luka 5 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 5:1-39

Yesu Ayitana Ophunzira Oyamba

1Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu. 2Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo. 3Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.

4Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”

5Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”

6Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika. 7Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.

8Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!” 9Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira, 10chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo.

Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 11Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.

Yesu Achiritsa Munthu Wakhate

12Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

13Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.

14Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”

15Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo. 16Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.

Yesu Achiritsa Wofa Ziwalo

17Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala. 18Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu. 19Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.

20Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”

21Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”

22Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu? 23Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’24Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’ ” 25Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu. 26Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”

Kuyitanidwa kwa Levi

27Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.” 28Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.

29Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi. 30Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”

31Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala. 32Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”

Yesu Afunsidwa za Kusala Kudya

33Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”

34Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo? 35Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”

36Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale. 37Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka. 38Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano. 39Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’ ”

New Serbian Translation

Лука 5:1-39

Исус позива прве ученике

1Једном је Исус стајао крај Генисаретског језера. Народ се око њега гурао да чује реч Божију. 2Тада је Исус спазио две лађице које су стајале уз обалу. Рибари нису били у њима, него су испирали мреже. 3Ушао је у једну од њих која је припадала Симону и замолио га да отисне мало лађицу од обале. Онда је сео у лађицу и поучавао народ.

4Кад је престао да говори, рекао је Симону: „Отисни се на пучину, па тамо баците мреже за лов.“

5Симон му одговори: „Учитељу, целу ноћ смо се трудили и ништа нисмо уловили. Али кад ти кажеш, бацићу мреже.“

6Када су то учинили, извукли су толико риба, да су мреже почеле да се цепају. 7Још су махнули и друговима у другој лађици да дођу и помогну им. Напунили су обе лађице толико да умало не потонуше.

8Кад то виде Симон Петар, паде на колена пред Исусом и рече: „Господе, иди од мене јер сам грешан човек!“ 9Страх је, наиме, обузео и њега и оне који су били са њим, због количине риба које уловише. 10Исто је било и са Заведејевим синовима, Јаковом и Јованом, Симоновим друговима.

Исус рече Симону: „Не плаши се! Од сада ћеш ловити људе.“ 11Кад су извукли чамце на обалу, оставили су све и кренули за њим.

Исус лечи губавца

12Једном, док је Исус био у неком граду, дошао је један човек сав у губи. Кад је видео Исуса, пао је пред њим ничице и замолио га: „Господе, ако хоћеш, можеш да ме очистиш.“

13Исус испружи руку и дотаче га, рекавши: „Хоћу, буди чист!“ Губа са њега нестаде истог тренутка.

14Исус му онда нареди: „Не говори никоме о овоме, него иди и покажи се свештенику, па принеси жртву за очишћење, коју је Мојсије прописао, да се њима пружи доказ.“

15Ипак, глас о Исусу се пронео још више, тако да је много народа долазило к њему да га слуша и да их он излечи од болести. 16Али, Исус се повлачио на усамљена места и молио се.

Исус лечи одузетог човека

17Једнога дана је Исус поучавао. Тамо су седели и неки фарисеји и учитељи Закона који су дошли из свих места у Галилеји, Јудеји и из Јерусалима. А Господња сила је била тамо да би он лечио. 18Уто неки људи на носилима донеше једног одузетог човека. Хтели су да га унесу и положе пред Исуса, 19али то нису могли због мноштва. Међутим, они се попну на кров, уклоне црепове, па га са постељом спусте насред собе, право пред њега.

20Исус, видевши њихову веру, рече: „Пријатељу, опраштају ти се твоји греси!“ 21Зналци Светог писма и фарисеји почеше да умују у себи, говорећи: „Ко је овај богохулник? Ко може да опрашта грехе осим самог Бога?“

22Исус је знао о чему они умују, па им је рекао: „Зашто овако размишљате у срцу? 23Шта је лакше рећи: ’Твоји греси су опроштени’, или: ’Устани и ходај?’ 24Али да знате: Син Човечији има власт да на земљи опрашта грехе.“ Онда рече одузетоме: „Теби кажем: устани, узми своја носила и иди својој кући!“ 25Човек одмах устаде са своје постеље и оде кући славећи Бога. 26Сви су били усхићени, славили су Бога и пуни страха говорили: „Данас смо видели невероватне ствари!“

Исус позива Левија

27Касније, када је изашао, видео је порезника по имену Левије како седи на месту за прикупљање пореза. Исус му рече: „Пођи за мном!“ 28Он остави све, устане и пође за њим.

29Левије је, затим, у својој кући приредио велику гозбу у његову част. Тамо је заједно са њима за трпезом било много порезника и других људи. 30А фарисеји и зналци Светог писма су приговарали његовим ученицима, говорећи: „Зашто једете и пијете с порезницима и другим грешницима?“

31Исус им одговори: „Лекар не треба здравима него болеснима. 32Ја нисам дошао да позовем праведнике на покајање, већ грешнике.“

О посту

33Они му рекоше: „Јованови ученици често посте и моле се, а исто чине и фарисејски; ипак, твоји једу и пију.“

34Исус им рече: „Зар можете силити сватове да посте док је младожења са њима? 35Ипак, доћи ће дани када ће им отети младожењу, па ће тада постити.“

36Исус им још исприча причу: „Нико не прави закрпу од нове одеће да би је ставио на стару, јер тиме цепа нову одећу, а ни старој одећи не пристаје закрпа од нове. 37Такође, нико не улива ново вино у старе мехове, јер ће мехови попуцати од врења новога вина, па ће вино истећи, а мехови пропасти. 38Зато се ново вино мора сипати у нове мехове. 39Али, нико ко је пио старо вино, не жели ново, јер каже: ’Старо је боље.’“