Luka 5 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 5:1-39

Yesu Ayitana Ophunzira Oyamba

1Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu. 2Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo. 3Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.

4Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”

5Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”

6Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika. 7Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.

8Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!” 9Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira, 10chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo.

Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 11Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.

Yesu Achiritsa Munthu Wakhate

12Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

13Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.

14Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”

15Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo. 16Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.

Yesu Achiritsa Wofa Ziwalo

17Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala. 18Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu. 19Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.

20Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”

21Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”

22Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu? 23Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’24Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’ ” 25Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu. 26Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”

Kuyitanidwa kwa Levi

27Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.” 28Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.

29Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi. 30Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”

31Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala. 32Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”

Yesu Afunsidwa za Kusala Kudya

33Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”

34Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo? 35Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”

36Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale. 37Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka. 38Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano. 39Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’ ”

New Russian Translation

Луки 5:1-39

Чудесный улов рыбы

(Мат. 4:18-22; Мк. 1:16-20; Ин. 1:40-42)

1Однажды Иисус стоял у Геннисаретского озера5:1 Геннисаретское озеро – также называлось Галилейским и Тибериадским., и народ, столпившись вокруг Него, слушал слово Божье. 2Иисус увидел у воды две лодки, которые принадлежали рыбакам, промывавшим невдалеке сети. 3Он вошел в одну из лодок, которая принадлежала Симону, и попросил того отплыть немного от берега. Затем Он сел и стал учить народ из лодки. 4Когда Иисус закончил говорить, Он сказал Симону:

– Отплыви на глубокое место и закинь сети для лова.

5Симон ответил:

– Наставник, мы трудились всю ночь и ничего не поймали, но если Ты так говоришь, то я закину сети.

6И когда они сделали это, то поймали столько рыбы, что сети начали рваться. 7Они знаками стали звать на помощь товарищей из другой лодки. Те подплыли, и вместе они наполнили две лодки так, что лодки стали тонуть. 8Когда Симон Петр это увидел, он пал к ногам Иисуса и сказал:

– Уйди от меня, Господи, ведь я человек грешный!

9Он сказал так потому, что его и всех, кто вместе с ним ловил рыбу, объял ужас при виде столь обильного улова. 10Были поражены и товарищи Симона: Иаков и Иоанн, сыновья Зеведея. Иисус же сказал Симону:

– Не бойся, отныне ты будешь ловить людей.

11И вытащив лодки на берег, они оставили все и пошли за Ним.

Иисус исцеляет прокаженного

(Мат. 8:2-4; Мк. 1:40-44)

12Однажды, когда Иисус находился в одном из городов, Ему встретился человек, покрытый проказой. Когда он увидел Иисуса, то пал на лицо свое и стал умолять Его:

– Господи, если Ты захочешь, Ты можешь меня очистить.

13Иисус протянул руку и прикоснулся к нему, сказав:

– Хочу, очистись!

Проказа сразу же сошла с него, 14и Иисус предупредил его никому об этом не рассказывать, но повелел:

– Пойди, покажись священнику и принеси жертву за очищение, как это повелел Моисей5:14 См. Лев. 14:1-32.. Так твое исцеление будет удостоверено перед людьми.

15Однако слух об Иисусе распространялся все шире, и люди толпами шли к Нему, чтобы послушать Его и исцелиться от болезней. 16Иисус же часто уходил в безлюдные места и молился.

Иисус исцеляет парализованного

(Мат. 9:2-8; Мк. 2:3-12)

17Однажды, когда Иисус учил, рядом сидели фарисеи и учители Закона, которые собрались из всех селений Галилеи, Иудеи и из Иерусалима. С Иисусом была сила Господа, чтобы исцелять больных. 18И тут пришли несколько человек, неся на циновке парализованного, и пытались внести его в дом, чтобы положить перед Иисусом. 19Но из-за толпы они не смогли этого сделать, и тогда они поднялись на крышу и, разобрав черепицу, опустили парализованного на циновке в середину толпы, прямо перед Иисусом. 20Когда Иисус увидел их веру, Он сказал больному:

– Друг, прощаются тебе твои грехи!

21Фарисеи и учители Закона подумали про себя: «Кто Этот Человек, Который так кощунствует? Кто, кроме одного лишь Бога, может прощать грехи?» 22Узнав, о чем они думают, Иисус ответил им:

– Что у вас за мысли в сердце? 23Что легче – сказать: «Прощаются тебе твои грехи» – или сказать: «Встань и ходи»? 24Но чтобы вы знали, что Сын Человеческий имеет власть на земле прощать грехи …

И тут Иисус обратился к парализованному человеку:

– Говорю тебе, встань, возьми свою циновку и иди домой.

25Тот сразу же у всех на глазах встал, взял то, на чем лежал, и пошел домой, прославляя Бога. 26Всех охватило изумление, и они прославляли Бога. Объятые страхом, они говорили:

– Невероятные вещи видели мы сегодня.

Иисус обедает с грешниками в доме Левия

(Мат. 9:9-13; Мк. 2:14-17)

27Выйдя из этого дома, Иисус увидел сборщика налогов по имени Левий, сидевшего на месте сбора таможенных пошлин.

– Следуй за Мной, – сказал ему Иисус.

28Левий встал, оставил все и пошел за Ним. 29Потом он устроил у себя дома большой пир для Иисуса. На пир собралось много сборщиков налогов и другого народа. Они возлежали вместе с Иисусом. 30Фарисеи же и учители Закона возмущенно спрашивали учеников Иисуса:

– Почему вы едите и пьете со сборщиками налогов и с грешниками?

31Иисус ответил им:

– Не здоровым нужен врач, а больным. 32Я пришел призвать к покаянию не праведников, а грешников.

Религиозные вожди спрашивают Иисуса о посте

(Мат. 9:14-17; Мк. 2:18-22)

33Тогда они сказали Иисусу:

– Ученики Иоанна и фарисеев часто постятся и молятся, а Твои ученики – едят и пьют.

34Иисус им ответил:

– Разве можно заставить гостей на свадьбе поститься, пока с ними жених? 35Но наступит время, когда жених будет взят от них, вот тогда, в те дни, они и будут поститься.

36Он также рассказал им притчу:

– Никто не пришивает заплату к старому плащу, оторвав для этого кусок от нового. Если он это сделает, то он и новый плащ испортит, и к старому заплата не подойдет. 37И никто не наливает молодое вино в старые бурдюки, иначе молодое вино прорвет их – оно вытечет, а бурдюки пропадут. 38Нет, молодое вино льют в новые бурдюки. 39И никто, пьющий старое вино, не захочет молодого, потому что скажет: «Старое лучше».