Luka 4 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 4:1-44

Kuyesedwa kwa Yesu

1Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu, 2kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.

3Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”

4Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’ ”

5Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi. 6Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna. 7Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”

8Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ ”

9Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano. 10Pakuti kwalembedwa,

“Adzalamulira angelo ake za iwe

kuti akutchinjirize mosamala;

11ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”

12Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ ”

13Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.

Yesu Akanidwa ku Nazareti

14Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi. 15Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.

16Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba. 17Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,

18“Mzimu wa Ambuye ali pa Ine;

chifukwa wandidzoza

kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka.

Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe

ndi kwa osaona kuti apenyenso,

kumasulidwa kwa osautsidwa,

19ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”

20Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye, 21ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”

22Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”

23Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”

24Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo. 25Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo. 26Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni. 27Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”

28Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi. 29Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho. 30Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.

Yesu Atulutsa Mzimu Woyipa

31Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu. 32Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.

33Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti 34“Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”

35Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.

36Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!” 37Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

38Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize. 39Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.

40Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa. 41Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.

42Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere. 43Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.” 44Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.

La Bible du Semeur

Luc 4:1-44

La tentation de Jésus

(Mt 4.1-11 ; Mc 1.12-13)

1Jésus, rempli de l’Esprit Saint, revint du Jourdain et l’Esprit le conduisit dans le désert 2où il fut tenté par le diable durant quarante jours. Il ne mangea rien durant ces jours-là, et, quand ils furent passés, il eut faim.

3Alors le diable lui dit : Si tu es le Fils de Dieu, ordonne donc à cette pierre de se changer en pain.

4Jésus lui répondit : Il est écrit :

L’homme ne vivra pas seulement de pain4.4 Dt 8.3..

5Le diable l’entraîna sur une hauteur, 6lui montra en un instant tous les royaumes de la terre et lui dit : Je te donnerai la domination universelle ainsi que les richesses et la gloire de ces royaumes. Car tout cela a été remis entre mes mains et je le donne à qui je veux. 7Si donc tu te prosternes devant moi, tout cela sera à toi.

8Jésus lui répondit : Il est écrit :

Tu adoreras le Seigneur, ton Dieu,

et c’est à lui seul que tu rendras un culte4.8 Dt 6.13..

9Le diable le conduisit ensuite à Jérusalem, le plaça tout en haut du Temple et lui dit : Si tu es le Fils de Dieu, jette-toi d’ici en bas, car il est écrit :

10Il donnera des ordresà ses anges à ton sujet,

pour qu’ils veillent sur toi,

11et encore :

Ils te porteront sur leurs mains

pour que ton pied ne heurte pas de pierre4.11 Ps 91.11-12..

12Jésus répondit : Il est aussi écrit :

Tu ne forceras pas la main au Seigneur, ton Dieu4.12 Dt 6.16..

13Lorsque le diable eut achevé de le soumettre à toutes sortes de tentations, il s’éloigna de lui jusqu’au temps fixé4.13 Autre traduction : jusqu’au moment propice..

Ministère de Jésus en Galilée

Jésus, le Serviteur choisi par Dieu

(Mt 4.12-17 ; Mc 1.14-15)

14Jésus, rempli de la puissance de l’Esprit, retourna en Galilée. Sa réputation se répandit dans toute la région. 15Il enseignait dans les synagogues et tous faisaient son éloge.

(Mt 13.53-58 ; Mc 6.1-6)

16Il se rendit aussi à Nazareth, où il avait été élevé, et il entra dans la synagogue le jour du sabbat, comme il en avait l’habitude. Il se leva pour faire la lecture biblique4.16 N’importe quel membre juif de l’assistance pouvait être appelé à faire la lecture des livres de l’Ancien Testament durant le culte de la synagogue., 17et on lui présenta le rouleau du prophète Esaïe. En déroulant le parchemin, il trouva le passage où il est écrit :

18L’Esprit du Seigneur est sur moi

car il m’a oint

pour annoncer une bonne nouvelle aux pauvres.

Il m’a envoyépour annoncer aux captifs la délivrance,

aux aveugles le recouvrement de la vue,

pour apporter la liberté aux opprimés

19et proclamer une année de faveur accordée par le Seigneur4.19 Es 61.1-2 cité selon l’ancienne version grecque..

20Il roula le livre, le rendit au servant et s’assit. Dans la synagogue, tous les yeux étaient braqués sur lui.

21– Aujourd’hui même, commença-t-il, pour vous qui l’entendez, cette prophétie de l’Ecriture est devenue réalité.

22Aucun de ses auditeurs ne restait indifférent : les paroles de grâce qu’il prononçait les étonnaient beaucoup. Aussi disaient-ils : N’est-il pas le fils de Joseph ?

23Alors il leur dit : Vous ne manquerez pas de m’appliquer ce dicton : « Médecin, guéris-toi toi-même » et vous me direz : « On nous a parlé de ce que tu as accompli à Capernaüm. Fais-en donc autant ici, dans ta propre ville ! » 24Et il ajouta : Vraiment, je vous l’assure : aucun prophète n’est bien accueilli dans sa patrie. 25Voici la vérité, je vous le déclare : il y avait beaucoup de veuves en Israël à l’époque d’Elie, quand, pendant trois ans et demi, il n’y a pas eu de pluie et qu’une grande famine a sévi dans tout le pays. 26Or, Elie n’a été envoyé vers aucune d’entre elles, mais vers une veuve qui vivait à Sarepta, dans le pays de Sidon4.26 1 R 17.9.. 27Il y avait aussi beaucoup de lépreux en Israël au temps du prophète Elisée. Et pourtant, aucun d’eux n’a été guéri. C’est le Syrien Naaman qui l’a été4.27 2 R 5.1-14..

28En entendant ces paroles, tous ceux qui étaient dans la synagogue se mirent en colère. 29Ils se levèrent, firent sortir Jésus de la ville, et le menèrent jusqu’au sommet de la montagne sur laquelle elle était bâtie, afin de le précipiter dans le vide. 30Mais il passa au milieu d’eux et s’en alla.

Exorcisme et guérisons à Capernaüm

(Mc 1.21-28)

31Il se rendit à Capernaüm, une autre ville de la Galilée. Il y enseignait les jours de sabbat. 32Ses auditeurs étaient profondément impressionnés par son enseignement, car il parlait avec autorité.

33Dans la synagogue se trouvait un homme sous l’emprise d’un esprit démoniaque et impur. Il se mit à crier d’une voix puissante : 34Ah ! Que nous veux-tu, Jésus de Nazareth ? Es-tu venu pour nous détruire4.34 Autre traduction : tu es venu pour nous détruire. ? Je sais qui tu es ! Tu es le Saint envoyé par Dieu !

35Mais, d’un ton sévère, Jésus lui ordonna : Tais-toi, et sors de cet homme !

Le démon jeta l’homme par terre, au milieu des assistants, et sortit de lui, sans lui faire aucun mal. 36Tous furent saisis de stupeur ; ils se disaient tous, les uns aux autres : Quelle est cette parole ? Il donne des ordres aux esprits mauvais, avec autorité et puissance, et ils sortent !

37Et la renommée de Jésus se répandait dans toutes les localités environnantes.

(Mt 8.14-17 ; Mc 1.29-34)

38En sortant de la synagogue, il se rendit à la maison de Simon. Or, la belle-mère de Simon souffrait d’une forte fièvre, et l’on demanda à Jésus de faire quelque chose pour elle. 39Il se pencha sur elle, donna un ordre à la fièvre, et la fièvre la quitta. Alors elle se leva immédiatement et se mit à les servir.

40Au coucher du soleil, tous ceux qui avaient chez eux des malades atteints des maux les plus divers les amenèrent à Jésus4.40 On attendait le coucher du soleil qui marquait la fin du sabbat pour transporter les malades, car il était interdit de le faire durant le jour du repos.. Il posa ses mains sur chacun d’eux et les guérit. 41Des démons sortaient aussi de beaucoup d’entre eux en criant : Tu es le Fils de Dieu !

Mais Jésus les reprenait sévèrement pour les faire taire, car ils savaient qu’il était le Messie4.41 Jésus ne voulait pas être « accrédité » par les démons..

(Mc 1.35-39)

42Dès qu’il fit jour, Jésus sortit de la maison et se rendit dans un lieu désert. Les foules se mirent à sa recherche et, après l’avoir rejoint, voulurent le retenir pour qu’il ne les quitte pas.

43Mais il leur dit : Je dois aussi annoncer la Bonne Nouvelle du royaume de Dieu aux autres villes, car c’est pour cela que Dieu m’a envoyé.

44Et il prêchait dans les synagogues de la Judée4.44 Certains manuscrits ont : Galilée..