Luka 24 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 24:1-53

Yesu Auka kwa Akufa

1Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda. 2Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika 3ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu. 4Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo. 5Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa? 6Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya: 7‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’ ” 8Ndipo anakumbukira mawu ake.

9Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse. 10Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi. 11Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru. 12Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.

Zochitika pa Njira ya ku Emau

13Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu. 14Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo. 15Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi; 16koma iwo sanamuzindikire.

17Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?”

Iwo anayima ndi nkhope zakugwa. 18Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”

19Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?”

Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse. 20Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye; 21koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi. 22Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa 23koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo. 24Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”

25Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena! 26Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?” 27Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.

28Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira. 29Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.

30Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira. 31Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo. 32Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”

33Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi 34ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.” 35Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira

36Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”

37Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa. 38Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu? 39Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”

40Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake. 41Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?” 42Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika. 43Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.

44Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”

45Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba. 46Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu. 47Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu. 48Inu ndinu mboni za zimenezi. 49Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”

Kupita Kumwamba

50Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa. 51Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba. 52Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu. 53Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.

Knijga O Kristu

Luka 24:1-53

Isusovo uskrsnuće

(Mt 28:1-10; Mk 16:1-8; Iv 20:1-9)

1U osvit dana u nedjelju24:1 U grčkome: prvoga dana tjedna. dođu na grob s miomirisima što su ih pripravile 2i nađu kamen s ulaza u grob odmaknut. 3Ušle su unutra, ali nisu našle tijelo Gospodina Isusa. 4Dok su tako zbunjene stajale, uz njih se pojave dva čovjeka u blistavoj odjeći. 5Žene se prestraše i poniknu licem prema zemlji. “Zašto tražite živoga među mrtvima?” upitaju ih dvojica. 6“Nije ovdje, uskrsnuo je! Sjetite se što vam je govorio još u Galileji: 7‘Sina Čovječjega predat će u ruke grešnicima i raspet će ga, ali on će treći dan uskrsnuti.’”

8One se sjete da je Isus to rekao. 9Požure zato s groba to javiti jedanaestorici učenika i ostalima. 10Bile su to Marija Magdalena, Ivana i Marija, majka Jakovljeva, i još neke žene. Sve su one to ispričale apostolima, 11ali njima se činilo da je sve to izmišljotina. I nisu im vjerovali. 12Ipak, Petar potrči do groba. Kad je stigao, proviri unutra i spazi samo povoje od lanena platna. Vrati se zatim čudeći se onomu što se dogodilo.

Isus se ukazuje učenicima na putu u Emaus

13Toga su dana dvojica Isusovih sljedbenika putovala u selo Emaus, udaljeno od Jeruzalema jedanaest kilometara.24:13 U grčkome: šezdeset stadija. 14Putem su razgovarali o svemu što se dogodilo. 15Dok su tako razgovarali i raspravljali, pristupi im Isus i pođe s njima. 16Ali njihovim je očima bilo uskraćeno da ga prepoznaju.

17“O čemu to raspravljate putujući?” upita ih.

Oni zastanu, shrvani tugom. 18Jedan od njih, imenom Kleofa, odgovori mu: “Ti si, čini se, jedini tuđinac u Jeruzalemu koji ne zna što se ondje dogodilo ovih dana.”

19“Što se dogodilo?” upita Isus.

“Pa to s Isusom Nazarećaninom”, rekli su. “On je bio prorok silan i na riječi i na djelima pred Bogom i pred svim narodom. 20Ali naši svećenički poglavari i članovi Velikog vijeća predali su ga da bude osuđen na smrt te su ga raspeli. 21A mi smo se nadali da je on Otkupitelj koji će spasiti Izrael. Osim toga, već je treći dan otkako se to dogodilo. 22Još su nas i neke žene, koju su ga s nama slijedile, zbunile: čim je svanulo otišle su na grob, 23ali ondje nisu našle njegovo tijelo. Došle su i rekle da su im se ukazali anđeli i kazali im da je živ. 24Neki od nas pojurili su na grob i našli su sve kao što su žene ispričale, ali njega nisu vidjeli.”

25“Neumnici!” reče im nato Isus. “Nikako da povjerujete sve što su proroci navijestili. 26Nisu li oni prorekli da će Krist morati sve to pretrpjeti prije nego što uđe u svoju slavu?” 27Zatim im, započevši od Mojsija, protumači što su svi proroci o njemu zapisali u Svetome pismu.

28Približili su se već selu kamo su išli, a Isus se pričini da će nastaviti put. 29Ali oni su ga nagovarali: “Ostani s nama! Već je večer; dan je na izmaku!” On ostane i uđe s njima u kuću. 30Dok je sjedio s njima za stolom, Isus uzme kruh, blagoslovi ga i razlomi te im ga dade. 31Uto se njima otvore oči pa ga prepoznaju, a on nestane.

32“Nije li nam srce usplamtjelo kad nam je putem pričao i tumačio Pisma?” upitaju oni jedan drugoga. 33Smjesta se spreme i vrate u Jeruzalem. Ondje nađu na okupu Jedanaestoricu i ostale Isusove sljedbenike. 34“Gospodin je zaista uskrsnuo!” kazaše im. “Zaista se ukazao Šimunu!”

Isus se pojavljuje pred učenicima

(Iv 20:19-23)

35Ispripovijedaju im zatim susret s Gospodinom na putu u Emaus te kako su ga prepoznali kad je razlomio kruh. 36Dok su oni o tome razgovarali, Isus odjednom stane među njih. “Mir vama!” reče im. 37Zbunjeni i prestrašeni, mislili su da vide duha. 38Ali Isus im reče: “Zašto se bojite? Zašto vam se sumnja rađa u srcu? 39Pogledajte mi ruke i noge! Ja sam to! Opipajte me pa ćete vidjeti! Duhovi nemaju kostiju i mesa kao ja!” 40Pokaže im svoje ruke i noge.

41Od čuđenja i veselja nisu mogli vjerovati. On upita: “Imate li što za jelo?” 42Pruže mu komad pečene ribe, 43a on ga uzme i pojede pred njima.

44Reče zatim: “O ovome sam vam govorio dok sam prije bio s vama: Trebalo se ispuniti sve što u Mojsijevu zakonu, proročkim knjigama i psalmima piše o meni.” 45Otvori im zatim um da razumiju Sveto pismo 46pa reče: “Piše da će Krist trpjeti i treći dan ustati od mrtvih. 47U njegovo ime propovijedajte obraćenje i oproštenje grijeha svim narodima počevši od Jeruzalema. 48Vi ste svjedoci toga.

49A ja ću vam poslati Svetoga Duha, baš kao što je Otac obećao. Ostanite u gradu dok vas Sveti Duh ne ispuni silom odozgora!”

Uzašašće

(Mk 16:19-20; Djela 1:9-11)

50Isus ih zatim povede u blizinu Betanije. Ondje podigne ruke i blagoslovi ih. 51Tako se, blagoslivljajući ih, i rastane od njih: uznesen je na nebo. 52Oni mu se ničice poklone, a zatim se silno radosni vrate u Jeruzalem. 53Ondje su u Hramu neprestano slavili Boga.