Luka 22 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 22:1-71

Yudasi Avomera Kumupereka Yesu

1Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira, 2akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu. 3Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo. 4Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu. 5Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama. 6Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.

Paska Womaliza

7Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe. 8Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”

9Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”

10Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe, 11ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’ 12Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”

13Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.

Za Mgonero wa Ambuye

14Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo. 15Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa. 16Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”

17Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu. 18Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”

19Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”

20Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu. 21Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano. 22Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.” 23Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.

Mkangano Pakati pa Ophunzira

24Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu. 25Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’ 26Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira. 27Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani. 28Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero. 29Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine, 30kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31“Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu. 32Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”

33Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”

34Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”

35Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?”

Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”

36Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula. 37Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”

38Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.”

Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”

Yesu Apemphera ku Phiri la Olivi

39Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye. 40Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.” 41Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti, 42“Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.” 43Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa. 44Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.

45Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni. 46Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”

Amugwira Yesu

47Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone. 48Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”

49Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?” 50Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.

51Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.

52Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga? 53Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”

Petro Akana Yesu

54Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali. 55Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi. 56Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”

57Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”

58Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.”

Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”

59Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”

60Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira. 61Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.” 62Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.

Asilikali Amuchita Chipongwe Yesu

63Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya. 64Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?” 65Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.

Yesu Pamaso pa Pilato ndi Herode

66Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo. 67Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.”

Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire. 68Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe. 69Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”

70Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?”

Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”

71Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”

King James Version

Luke 22:1-71

1Now the feast of unleavened bread drew nigh, which is called the Passover. 2And the chief priests and scribes sought how they might kill him; for they feared the people.

3¶ Then entered Satan into Judas surnamed Iscariot, being of the number of the twelve. 4And he went his way, and communed with the chief priests and captains, how he might betray him unto them. 5And they were glad, and covenanted to give him money. 6And he promised, and sought opportunity to betray him unto them in the absence of the multitude.

7¶ Then came the day of unleavened bread, when the passover must be killed. 8And he sent Peter and John, saying, Go and prepare us the passover, that we may eat. 9And they said unto him, Where wilt thou that we prepare? 10And he said unto them, Behold, when ye are entered into the city, there shall a man meet you, bearing a pitcher of water; follow him into the house where he entereth in. 11And ye shall say unto the goodman of the house, The Master saith unto thee, Where is the guestchamber, where I shall eat the passover with my disciples? 12And he shall shew you a large upper room furnished: there make ready. 13And they went, and found as he had said unto them: and they made ready the passover. 14And when the hour was come, he sat down, and the twelve apostles with him. 15And he said unto them, With desire I have desired to eat this passover with you before I suffer: 16For I say unto you, I will not any more eat thereof, until it be fulfilled in the kingdom of God. 17And he took the cup, and gave thanks, and said, Take this, and divide it among yourselves: 18For I say unto you, I will not drink of the fruit of the vine, until the kingdom of God shall come.

19¶ And he took bread, and gave thanks, and brake it, and gave unto them, saying, This is my body which is given for you: this do in remembrance of me. 20Likewise also the cup after supper, saying, This cup is the new testament in my blood, which is shed for you.

21¶ But, behold, the hand of him that betrayeth me is with me on the table. 22And truly the Son of man goeth, as it was determined: but woe unto that man by whom he is betrayed! 23And they began to enquire among themselves, which of them it was that should do this thing.

24¶ And there was also a strife among them, which of them should be accounted the greatest. 25And he said unto them, The kings of the Gentiles exercise lordship over them; and they that exercise authority upon them are called benefactors. 26But ye shall not be so: but he that is greatest among you, let him be as the younger; and he that is chief, as he that doth serve. 27For whether is greater, he that sitteth at meat, or he that serveth? is not he that sitteth at meat? but I am among you as he that serveth. 28Ye are they which have continued with me in my temptations. 29And I appoint unto you a kingdom, as my Father hath appointed unto me; 30That ye may eat and drink at my table in my kingdom, and sit on thrones judging the twelve tribes of Israel.

31¶ And the Lord said, Simon, Simon, behold, Satan hath desired to have you, that he may sift you as wheat: 32But I have prayed for thee, that thy faith fail not: and when thou art converted, strengthen thy brethren. 33And he said unto him, Lord, I am ready to go with thee, both into prison, and to death. 34And he said, I tell thee, Peter, the cock shall not crow this day, before that thou shalt thrice deny that thou knowest me. 35And he said unto them, When I sent you without purse, and scrip, and shoes, lacked ye any thing? And they said, Nothing. 36Then said he unto them, But now, he that hath a purse, let him take it, and likewise his scrip: and he that hath no sword, let him sell his garment, and buy one. 37For I say unto you, that this that is written must yet be accomplished in me, And he was reckoned among the transgressors: for the things concerning me have an end. 38And they said, Lord, behold, here are two swords. And he said unto them, It is enough.

39¶ And he came out, and went, as he was wont, to the mount of Olives; and his disciples also followed him. 40And when he was at the place, he said unto them, Pray that ye enter not into temptation. 41And he was withdrawn from them about a stone’s cast, and kneeled down, and prayed, 42Saying, Father, if thou be willing, remove this cup from me: nevertheless not my will, but thine, be done. 43And there appeared an angel unto him from heaven, strengthening him. 44And being in an agony he prayed more earnestly: and his sweat was as it were great drops of blood falling down to the ground. 45And when he rose up from prayer, and was come to his disciples, he found them sleeping for sorrow, 46And said unto them, Why sleep ye? rise and pray, lest ye enter into temptation.

47¶ And while he yet spake, behold a multitude, and he that was called Judas, one of the twelve, went before them, and drew near unto Jesus to kiss him. 48But Jesus said unto him, Judas, betrayest thou the Son of man with a kiss? 49When they which were about him saw what would follow, they said unto him, Lord, shall we smite with the sword?

50¶ And one of them smote the servant of the high priest, and cut off his right ear. 51And Jesus answered and said, Suffer ye thus far. And he touched his ear, and healed him. 52Then Jesus said unto the chief priests, and captains of the temple, and the elders, which were come to him, Be ye come out, as against a thief, with swords and staves? 53When I was daily with you in the temple, ye stretched forth no hands against me: but this is your hour, and the power of darkness.

54¶ Then took they him, and led him, and brought him into the high priest’s house. And Peter followed afar off. 55And when they had kindled a fire in the midst of the hall, and were set down together, Peter sat down among them. 56But a certain maid beheld him as he sat by the fire, and earnestly looked upon him, and said, This man was also with him. 57And he denied him, saying, Woman, I know him not. 58And after a little while another saw him, and said, Thou art also of them. And Peter said, Man, I am not. 59And about the space of one hour after another confidently affirmed, saying, Of a truth this fellow also was with him: for he is a Galilæan. 60And Peter said, Man, I know not what thou sayest. And immediately, while he yet spake, the cock crew. 61And the Lord turned, and looked upon Peter. And Peter remembered the word of the Lord, how he had said unto him, Before the cock crow, thou shalt deny me thrice. 62And Peter went out, and wept bitterly.

63¶ And the men that held Jesus mocked him, and smote him. 64And when they had blindfolded him, they struck him on the face, and asked him, saying, Prophesy, who is it that smote thee? 65And many other things blasphemously spake they against him.

66¶ And as soon as it was day, the elders of the people and the chief priests and the scribes came together, and led him into their council, saying, 67Art thou the Christ? tell us. And he said unto them, If I tell you, ye will not believe: 68And if I also ask you, ye will not answer me, nor let me go. 69Hereafter shall the Son of man sit on the right hand of the power of God. 70Then said they all, Art thou then the Son of God? And he said unto them, Ye say that I am. 71And they said, What need we any further witness? for we ourselves have heard of his own mouth.