Luka 2 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 2:1-52

Kubadwa kwa Yesu

1Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma. 2(Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya). 3Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.

4Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide. 5Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera. 6Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe, 7ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.

Abusa ndi Angelo

8Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku. 9Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha. 10Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse. 11Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye. 12Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”

13Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,

14“Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba,

ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”

15Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”

16Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe. 17Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo, 18ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa. 19Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira. 20Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.

Yesu Aperekedwa mʼNyumba ya Mulungu

21Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.

22Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye. 23(Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”), 24ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”

25Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye. 26Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye. 27Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo, 28Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:

29“Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza,

tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.

30Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,

31chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,

32kuwala kowunikira anthu a mitundu ina

ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”

33Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye. 34Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho, 35kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”

36Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa, 37ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera. 38Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.

39Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti. 40Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.

Yesu mʼNyumba ya Mulungu

41Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska. 42Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo. 43Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi. 44Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo. 45Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna. 46Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso. 47Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake. 48Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”

49Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?” 50Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.

51Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.

52Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.

Священное Писание

Лука 2:1-52

Рождение Исы Масиха

1В те дни император Август2:1 Август был римским императором с 27 г. до н. э. до 14 г. н. э. издал указ о проведении переписи по всей Римской империи. 2Это была первая перепись, она проводилась в то время, когда Сирией управлял Квириний2:2 Квириний, вероятно, был римским чиновником или полководцем, который проводил эту первую перепись в Сирии, длившуюся с 11 по 4 гг. до н. э., а во время второй переписи с 6 по 9 гг. н. э. он был римским наместником.. 3Поэтому каждый отправился в свой город для регистрации. 4Юсуф тоже пошёл из галилейского города Назарета в Иудею, в город Давуда, называемый Вифлеем, потому что он был потомком царя Давуда. 5Он отправился на перепись вместе с Марьям, которая была с ним обручена и ожидала ребёнка. 6В Вифлееме у Марьям подошло время родов, 7и она родила своего первенца, запеленала Его и положила в кормушку для скота, потому что для них не нашлось места в гостинице2:7 Или: «в комнате для гостей»..

Ангелы возвещают пастухам радостную весть

8Неподалёку были пастухи, которые жили в поле и стерегли ночью своё стадо. 9Вдруг перед ними предстал ангел от Вечного, окружённый сиянием славы Вечного. Пастухи очень испугались, 10но ангел сказал им:

– Не бойтесь. Я пришёл сообщить вам весть, что принесёт великую радость всему народу! 11Сегодня в городе Давуда родился ваш Спаситель2:11 Спаситель – ср. Ис. 43:11; Ос. 13:4. – Масих2:11 Масих (переводится как «Помазанник») – праведный Царь и Освободитель, Спаситель, обещанный Всевышним ещё в Таурате, Забуре и Книге Пророков., Повелитель! 12Вот вам знак: вы найдёте младенца, запелёнатого и лежащего в кормушке.

13И вдруг к ангелу присоединилось многочисленное небесное воинство, славившее Всевышнего и восклицавшее:

14– Хвала Всевышнему в вышине небес!

А на земле мир тем людям, к которым Он благоволит!

15Когда ангелы вернулись на небеса, пастухи сказали друг другу:

– Пойдём в Вифлеем и посмотрим, что там произошло, о чём это нам объявил Вечный?

16Они поспешили туда и нашли Марьям, Юсуфа и младенца, лежащего в кормушке для скота. 17Когда они Его увидели, то рассказали всё, что им было сказано об этом младенце. 18Все, кто слушал, удивлялись рассказу пастухов, 19а Марьям всё запоминала и размышляла об этом. 20Пастухи возвратились, прославляя и восхваляя Всевышнего за всё, что они видели и слышали: всё оказалось точно так, как им и было сказано.

Обрезание, наречение имени и посвящение Исы Масиха Всевышнему

21На восьмой день, когда пришло время совершить над Ним обряд обрезания, Его назвали Иса – имя, которое ангел дал Ему ещё до того, как Он был зачат. 22Когда закончилось время очищения, предписанное Законом Мусы2:22 По Закону очищение женщины завершалось на сороковой день после рождения сына (см. Лев. 12:2-8)., Марьям и Юсуф понесли младенца в Иерусалим, чтобы посвятить Его Вечному, 23потому что в Законе Вечного написано: «Каждый первенец мужского пола должен быть посвящён Вечному»2:23 См. Исх. 13:2, 12, 15.. 24Они должны были также по Закону Вечного принести в жертву пару горлиц или двух молодых голубей2:24 См. Лев. 12:6-8..

Благословение и пророчество Шимона

25В Иерусалиме в это время был человек, которого звали Шимон. Он был праведен и благочестив и с надеждой ожидал Того, Кто принесёт утешение для Исраила, и на нём был Святой Дух. 26Святой Дух открыл ему, что он не умрёт, пока не увидит Масиха, посланного Вечным. 27Ведомый Святым Духом, Шимон пришёл в храм, и когда родители принесли младенца Ису, чтобы совершить над Ним то, что было установлено Законом, 28Шимон взял Его на руки и прославил Всевышнего, сказав:

29– Владыка! Теперь, как Ты и обещал,

Ты отпускаешь Своего раба с миром,

30потому что мои глаза увидели спасение Твоё,

31которое Ты приготовил перед лицом всех народов,

32свет откровения язычникам

и славу народа Твоего, Исраила!2:32 См. Ис. 42:6; 49:6.

33Отец и мать удивлялись тому, что было сказано об Исе. 34Потом Шимон благословил их и сказал Марьям, матери ребёнка:

– Это дитя будет причиной падения и возвышения для многих в Исраиле и станет знамением от Всевышнего, которое будет многими отвергаемо, – 35да и тебе самой меч пронзит душу. Через всё это откроются тайные мысли многих людей.

36Там находилась также пророчица Ханна, дочь Пануила, из рода Ашира. Она была в глубокой старости. Ханна прожила семь лет со своим мужем, 37а всю остальную жизнь она жила вдовой. Ей было восемьдесят четыре года2:37 Или: «Она была вдовой восемьдесят четыре года».. Она никогда не покидала храма, день и ночь служа Всевышнему постами и молитвами. 38Подойдя в этот момент к тем, кто принёс младенца, она возблагодарила Всевышнего и говорила о ребёнке всем ожидавшим избавления для Иерусалима.

39Когда родители Исы сделали всё, что предписывал Закон Вечного, они возвратились в Галилею, в свой родной город Назарет. 40Ребёнок рос и набирался сил и мудрости, и Всевышний был благосклонен к Нему.

Двенадцатилетний Иса в храме

41Каждый год на праздник Освобождения2:41 Праздник Освобождения – этот праздник отмечался исключительно в Иерусалиме в память об избавлении иудейского народа под руководством пророка Мусы из Египетского рабства (см. Исх. 12; 13:17-22; 14; Втор. 16:1-8). родители Исы ходили в Иерусалим. 42Когда Ему было двенадцать лет, они, как обычно, пошли на праздник. 43После окончания праздника, когда все возвращались домой, мальчик Иса остался в Иерусалиме, но Его родители об этом не знали. 44Полагая, что Он идёт среди других путников, они после целого дня пути стали искать Его среди родственников и знакомых. 45Не найдя, они возвратились в Иерусалим, чтобы искать там. 46Через три дня они нашли мальчика в храме. Он сидел среди учителей, слушал их и задавал вопросы. 47Все, кто Его слышал, поражались Его пониманию и Его ответам. 48Родители были изумлены, увидев Его там.

– Сынок, почему Ты так с нами поступил? – спросила Его мать. – Твой отец и я беспокоились и искали Тебя.

49– Зачем же вы Меня искали? – спросил Он. – Разве вы не знали, что Я должен быть в доме Отца Моего?

50Но они не поняли, о чём Он им говорил. 51Он возвратился с ними в Назарет и был послушен им. Но всё происшедшее Его мать хранила в своей памяти.

52Иса взрослел и становился мудрее. Его любили и люди, и Всевышний2:52 Ср. 1 Цар. 2:26..