Luka 18 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 18:1-43

Fanizo la Mayi Wakhama pa Kupempha

1Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke. 2Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu. 3Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’

4“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu, 5koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’ ”

6Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena. 7Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira? 8Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”

Fanizo la Mfarisi ndi Wolandira Msonkho

9Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse. 10“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho. 11Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu. 12Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’

13“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’

14“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”

Yesu Adalitsa Ana Aangʼono

15Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula. 16Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere. 17Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”

Munthu Wachuma ndi Ufumu wa Mulungu

18Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?”

19Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha. 20Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’ ”

21Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”

22Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”

23Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri. 24Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu! 25Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”

26Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”

27Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”

28Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”

29Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu 30adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.”

Yesu Aneneratu za Imfa Yake Kachitatu

31Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa. 32Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira, 33adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”

34Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.

Yesu Achiritsa Wosaona

35Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha, 36anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika. 37Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”

38Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

39Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”

40Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti, 41“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”

42Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.” 43Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

Slovo na cestu

Lukáš 18:1-43

Ježíš vypráví podobenství o neodbytné vdově

1Ježíš ještě připojil podobenství o tom, jak je zapotřebí vytrvale se modlit: 2„V jednom městě žil soudce, který na Boha nedal a na lidi se neohlížel. 3Byla tam také jedna vdova a ta za ním neustále chodila, aby jí dopomohl v právu proti člověku, který jí ublížil. 4Soudce ji dlouho odbýval, ale nakonec si řekl: ‚Je mi sice jedno, co si Bůh nebo lidé o té věci myslí, 5ale když je tak neodbytná, vyhovím jí. Jinak bude stále za mnou chodit, až mne umoří.‘ 6Vidíte, neodbytné prosebnici nakonec vyhoví i tak špatný soudce. 7Jak by Bůh nepřišel na pomoc těm, kteří k němu volají dnem i nocí. 8I když jim okamžitě nevyhoví, přesto jim trpělivě naslouchá a nakonec pomůže v pravý čas. Ale až znovu přijdu, naleznu lidi s tak vytrvalou vírou?“

Ježíš vypráví podobenství o dvou modlících se mužích

9Těm, kteří si myslí, že jsou bez chyby, a dívají se na druhé spatra, vyprávěl Ježíš toto podobenství: 10„Dva muži přišli do chrámu, aby se pomodlili; jeden farizej a druhý publikán. 11Farizej si stoupl dopředu a modlil se: ‚Bože, děkuji ti, že nejsem tak chamtivý, nečestný nebo rozbíječ rodiny jako ostatní lidé, třeba jako tady ten výběrčí daní. 12Dvakrát týdně se postím a dávám ti desetinu ze všech svých příjmů.‘ 13Ten výběrčí stál úplně vzadu, hlavu měl skloněnou, ani se neodvážil pohlédnout vzhůru. Na znamení lítosti se bil do prsou a modlil se: ‚Bože, slituj se nade mnou, jsem velký hříšník.‘ “ 14Ježíš uzavřel: „Publikán nebyl v chrámu nadarmo; Bůh ho vzal na milost, ale toho farizeje si ani nevšiml. Každý, kdo vynáší sám sebe, bude pokořen, a kdo se před Bohem koří, bude povýšen.“

Ježíš žehná malým dětem

15Lidé přinášeli k Ježíšovi i malé děti, aby jim žehnal. Když to učedníci viděli, odháněli je. 16Ježíš však zavolal rodiče s dětmi k sobě a řekl: „Nebraňte dětem v přístupu ke mně, neodhánějte je. Boží království je právě pro takové, jako jsou ony; 17kdo neuvěří tak prostě jako dítě, nevejde do něho.“

Ježíš mluví k bohatému muži

18Jeden vznešený muž se Ježíše zeptal: „Svatý učiteli, co musím dělat, abych získal věčný život?“ 19Ježíš mu řekl: „Co tě vede k tomu, že mě nazýváš svatým? Vždyť svatý je pouze Bůh! 20Znáš jeho přikázání: Nezcizoložíš, nezabiješ, nikoho neokradeš, nepomluvíš a nenařkneš nikoho křivě, budeš si vážit svých rodičů.“ 21Muž odpověděl: „Tato přikázání se snažím dodržovat už od svého mládí.“ 22Ježíš mu řekl: „A přece ti ještě něco chybí. Prodej všechno, co máš, rozdej to chudým, a budeš mít poklad v nebi. Pak přijď a následuj mne.“ 23Jak to muž uslyšel, zesmutněl a odešel, protože byl velice bohatý.

24Když to Ježíš uviděl, řekl: „Jak nesnadno přicházejí lidé k Bohu. 25To spíš projde velbloud uchem jehly než boháč do Božího království.“ 26Lidé, kteří to slyšeli, se ptali: „Kdo tedy vůbec může být spasen?“ 27On odpověděl: „Na co člověk nestačí, to může učinit Bůh.“ 28Na to řekl Petr: „Ty víš, že jsme pro tebe opustili všechno a šli za tebou.“ 29Ježíš odpověděl: „Žádný, kdo se musel pro Boží království něčeho vzdát – domova, manželky, sourozenců, rodičů nebo dětí, nezůstane bez odměny. 30Již v tomto světě získá mnohem více a v budoucím obdrží život věčný.“

Ježíš potřetí předpovídá svou smrt

31Ježíš si vzal stranou svých dvanáct učedníků a řekl jim: „Jdeme teď do Jeruzaléma a tam se vyplní všechno, co napsali starodávní proroci o Synu člověka. 32Budu vydán do rukou pohanů, budou se mi vysmívat, budou mne týrat a plivat na mě. 33Pak mne zbičují a zabijí, ale třetího dne vstanu z mrtvých.“ 34Učedníci to vůbec nechápali a jeho slova jim byla záhadou.

Ježíš uzdravuje slepého žebráka

35Když se blížili k Jerichu, seděl u cesty slepec a žebral. 36Slyšel, že kolem proudí davy lidí a ptal se, co to má znamenat. 37Řekli mu, že tudy jde Ježíš z Nazaretu. 38Začal volat: „Ježíši, Davidův potomku, slituj se nade mnou.“ 39Lidé, kteří Ježíše provázeli, slepce okřikovali, ale on volal tím víc: „Králi z Davidova rodu, slituj se nade mnou.“ 40Ježíš se zastavil a zavolal slepce k sobě. 41Když ho k němu přivedli, zeptal se Ježíš: „Co pro tebe mám udělat?“ Slepec odpověděl: „Pane, ať vidím!“ 42Ježíš řekl: „Prohlédni! Tvá víra tě zachránila.“ 43V tom okamžiku slepec nabyl zrak, děkoval Bohu a šel za Ježíšem. A všichni, kteří toho byli svědky, chválili Boha.