Luka 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 18:1-43

Fanizo la Mayi Wakhama pa Kupempha

1Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke. 2Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu. 3Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’

4“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu, 5koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’ ”

6Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena. 7Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira? 8Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”

Fanizo la Mfarisi ndi Wolandira Msonkho

9Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse. 10“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho. 11Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu. 12Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’

13“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’

14“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”

Yesu Adalitsa Ana Aangʼono

15Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula. 16Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere. 17Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”

Munthu Wachuma ndi Ufumu wa Mulungu

18Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?”

19Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha. 20Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’ ”

21Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”

22Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”

23Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri. 24Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu! 25Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”

26Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”

27Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”

28Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”

29Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu 30adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.”

Yesu Aneneratu za Imfa Yake Kachitatu

31Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa. 32Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira, 33adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”

34Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.

Yesu Achiritsa Wosaona

35Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha, 36anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika. 37Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”

38Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

39Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”

40Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti, 41“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”

42Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.” 43Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

New Russian Translation

Луки 18:1-43

Притча Иисуса о настойчивой вдове

1Желая показать ученикам, что следует всегда молиться и не унывать, Иисус рассказал им такую притчу.

2– В одном городе был судья, который не боялся Бога и не стыдился людей. 3В том же городе жила вдова, которая постоянно ходила к нему и умоляла: «Защити меня от моего противника». 4Некоторое время судья ей отказывал, но в конце концов решил: «Пусть я Бога не боюсь и с людьми не считаюсь, 5но так как эта вдова постоянно надоедает мне, то я разрешу ее тяжбу, иначе она замучит меня своими просьбами».

6И Господь сказал:

– Слышите, что сказал несправедливый судья? 7Так неужели Бог не защитит Своих избранных, которые взывают к Нему день и ночь? Неужели Он будет медлить с помощью? 8Говорю вам: Он без промедления защитит их. Но когда Сын Человеческий придет, то найдет ли Он веру на земле?

Притча о фарисее и сборщике налогов

9Тем, кто был уверен в собственной праведности и с презрением смотрел на других, Иисус рассказал такую притчу:

10– Два человека пришли во двор храма помолиться. Один из них был фарисей, а другой – сборщик налогов. 11Фарисей, встав, молился о себе так: «Боже, благодарю Тебя, что я не такой, как другие люди: воры, мошенники, неверные супруги или как этот сборщик налогов. 12Я пощусь два раза в неделю и даю десятину со всякого дохода». 13А сборщик налогов, стоя вдали, не смел даже глаз к небу поднять, но бил себя в грудь и говорил: «Боже, будь милостив ко мне, грешнику». 14Говорю вам, что именно этот человек пошел домой оправданным перед Богом, а не первый. Потому что каждый возвышающий себя будет унижен, а каждый, принижающий себя, будет возвышен.

Иисус благословляет детей

(Мат. 19:13-15; Мк. 10:13-16)

15Некоторые люди приносили к Иисусу даже младенцев, чтобы Он прикоснулся к ним и благословил. Ученики же, увидев это, бранили их. 16Но Иисус подозвал их к Себе и сказал:

– Пусть дети приходят ко Мне, не запрещайте им, потому что Царство Божье принадлежит таким, как они. 17Говорю вам истину: кто не примет Божье Царство, как ребенок, тот не войдет в него.

Разговор Иисуса с богатым начальником

(Мат. 19:16-29; Мк. 10:17-30)

18Один начальник спросил Его:

– Благой Учитель, что мне делать, чтобы наследовать вечную жизнь?

19– Почему ты называешь Меня благим? – ответил Иисус. – Никто не благ, кроме одного Бога. 20Ты знаешь заповеди: «не нарушай супружескую верность», «не убивай», «не кради», «не лжесвидетельствуй», «почитай отца и мать»18:20 См. Исх. 20:12-16; Втор. 5:16-20..

21– Все это я соблюдаю еще с дней моей юности, – сказал он. 22Услышав это, Иисус сказал ему:

– Одного тебе еще не хватает. Продай все, что у тебя есть, и раздай деньги бедным, и тогда у тебя будет сокровище на небесах. Потом приходи и следуй за Мной.

23Когда начальник услышал это, он опечалился, потому что был очень богат. 24Иисус посмотрел на него и сказал:

– Как трудно богатым войти в Божье Царство! 25Легче верблюду пройти сквозь игольное ушко, чем богатому войти в Божье Царство.

26Те, кто это слышал, спросили:

– Кто же тогда вообще может быть спасен?

27Иисус ответил:

– Невозможное человеку возможно Богу.

28Тогда Петр сказал:

– Вот, мы оставили все, что у нас было, и пошли за Тобой.

29Иисус сказал им:

– Говорю вам истину: каждый, кто оставил дом, или жену, или братьев, или родителей, или детей ради Божьего Царства, 30получит во много раз больше в этой жизни, а в будущем – жизнь вечную.

Иисус в третий раз говорит о Своей смерти и воскресении

(Мат. 20:17-19; Мк. 10:32-34)

31Иисус отвел двенадцать учеников в сторону и сказал им:

– Вот, мы восходим в Иерусалим, и там исполнится все написанное пророками о Сыне Человеческом. 32Он будет отдан язычникам, те будут глумиться над Ним, унижать Его, плевать в Него, 33бичевать и затем убьют. Но на третий день Он воскреснет.

34Ученики ничего из этого не поняли; все, что Он сказал, было для них закрыто, и они не догадывались, что Он имел в виду.

Иисус исцеляет слепого нищего

(Мат. 20:29-34; Мк. 10:46-52)

35Когда Иисус подходил к Иерихону, у дороги сидел слепой и просил милостыню. 36Услышав, что мимо идет толпа, он спросил, что происходит.

37– Идет Иисус из Назарета, – сказали ему. 38Тогда слепой закричал:

– Иисус, Сын Давида!18:38 Сын Давида – один из титулов Христа. Согласно пророчествам ожидаемый Христос (т. е. праведный Царь и Освободитель) должен был быть потомком царя Давида (см. Ис. 11:1-5; Иер. 23:5-6). Сжалься надо мной!

39Те, что шли впереди, стали говорить, чтобы он замолчал, но слепой кричал еще громче:

– Сын Давида, сжалься надо мной!

40Иисус остановился и велел, чтобы этого человека подвели к Нему. Когда тот подошел, Иисус спросил его:

41– Что ты хочешь, чтобы Я сделал для тебя?

– Господи, я хочу видеть, – ответил слепой.

42Иисус сказал ему:

– Прозри! Твоя вера исцелила тебя.

43Слепой сразу же обрел зрение и пошел за Иисусом, славя Бога. И весь народ, увидев это, восхвалял Бога.