Luka 17 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 17:1-37

Za Uchimo, Chikhulupiriro ndi Ntchito

1Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo. 2Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa. 3Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha.

“Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni. 4Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”

5Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”

6Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.

7“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’ 8Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’ 9Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita? 10Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’ ”

Yesu Achiritsa Akhate Khumi

11Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu. 12Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali 13ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”

14Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.

15Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza. 16Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.

17Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti? 18Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?” 19Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”

Za Ufumu wa Mulungu

20Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso, 21kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”

22Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona. 23Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo. 24Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake. 25Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.

26“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu. 27Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.

28“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga. 29Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.

30“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera. 31Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse. 32Kumbukirani mkazi wa Loti! 33Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga. 34Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa. 35Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa. 36Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”

37Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?”

Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Луко 17:1-37

Об искушении, прощении, вере и долге

(Мат. 18:6-7, 15, 21-22; Мк. 9:42)

1Исо сказал Своим ученикам:

– Всегда будет повод для греха, но горе тому, кто толкает людей на грех. 2Для того, кто хотя бы одному из этих малых даст повод ко греху, было бы лучше, если бы ему надели на шею мельничный жёрнов и бросили в море. 3Поэтому следите за собой! Если твой брат согрешает, упрекни его, и если он раскается, прости его. 4Если даже он согрешит против тебя семь раз в день и семь раз придёт к тебе и скажет: «Я каюсь», прости его.

5Посланники Масеха как-то попросили Его:

– Прибавь нам веры!

6Повелитель ответил:

– Если у вас есть вера величиной хоть с горчичное зерно, то вы можете сказать этому тутовому дереву: «Вырвись с корнем и пересади себя в море», и оно вам подчинится.

7– Допустим, у кого-то из вас есть раб, который пашет или пасёт овец. Скажете ли вы ему, когда он возвратится с поля: «Заходи, возляг и ешь»? 8Нет, вы скорее скажете: «Приготовь для меня ужин, затем подпояшься и прислуживай мне, пока я буду есть и пить, а потом будешь есть и пить сам». 9Благодарит ли хозяин раба за то, что тот делает, что ему приказано? 10Так и вы, когда сделаете всё, что вам было приказано, говорите: «Мы недостойные рабы, мы сделали лишь то, что обязаны были сделать».

Исцеление десяти прокажённых

11По пути в Иерусалим Исо проходил вдоль границы между Сомарией и Галилеей. 12Когда Он входил в одно селение, Его встретили десять прокажённых. Остановившись неподалёку, 13они громко закричали:

– Исо, Наставник, сжалься над нами!

14Когда Исо их увидел, Он сказал:

– Пойдите и покажитесь священнослужителям.

Те пошли и по дороге были исцелены. 15Один из них, как только увидел, что исцелён, возвратился, громко прославляя Всевышнего. 16Он пал к ногам Исо и благодарил Его. И этот человек был сомарянином17:16 См. сноску на 10:33..

17– Разве не десять человек были очищены? – спросил Исо. – Где же остальные девять? 18Почему никто из них, кроме этого чужеземца, не возвратился, чтобы прославить Всевышнего?

19И сказал сомарянину:

– Встань и иди, твоя вера спасла тебя.

О возвращении Ниспосланного как Человек

(Мат. 24:28, 37-39)

20Однажды блюстители Закона спросили Исо, когда придёт Царство Всевышнего. Он ответил:

– Царство Всевышнего не придёт зримым образом17:20 Или: «Нельзя по приметам предсказать пришествие Царства Всевышнего».. 21Никто не сможет сказать: «Вот оно здесь» или «Оно там», потому что Царство Всевышнего уже среди вас.

22Потом Он сказал ученикам:

– Придёт такое время, когда вы захотите увидеть хотя бы один из дней правления Ниспосланного как Человек, но не увидите. 23Вам будут говорить: «Вон Он там!» или «Вот Он здесь!» – но вы не бегите смотреть. 24Потому что, когда Ниспосланный как Человек придёт вновь, это будет подобно блеску молнии, освещающему небо от края и до края. 25Но прежде Ему предстоит вытерпеть много страданий и быть отвергнутым этим поколением.

26Но как было во времена Нуха17:26 Нух – также известен как Ной., так будет и в дни перед возвращением Ниспосланного как Человек. 27Люди ели, пили, женились и выходили замуж до того дня, когда Нух вошёл в ковчег. Потом пришёл потоп и всех их уничтожил.

28То же самое было и в дни Лута. Люди ели и пили, покупали и продавали, сажали и строили. 29Но в день, когда Лут покинул Содом, с неба пролились дождём огонь и сера и всех их уничтожили.

30Так же будет и в день, когда явится Ниспосланный как Человек. 31В тот день, если кто-то окажется на крыше, а его вещи – в доме, пусть он не спускается вниз за вещами. И кто в поле – пусть уже не возвращается. 32Помните жену Лута!17:32 Жена Лута, хотя и была выведена из Содома, но сердце её было привязано к тому, что она там оставляла. Это и погубило её (см. Нач. 19:23-26). 33Кто пытается сохранить свою жизнь, тот потеряет её, и кто потеряет свою жизнь за Меня, тот сохранит её. 34Говорю вам, что в ту ночь двое будут на одной постели, и один будет взят, а другой оставлен17:34 Взят… оставлен – существуют два основных толкования этих слов: 1) Повелитель Исо заберёт Своих последователей, а другие останутся для наказания; 2) грешники будут взяты на Суд, а Его последователи останутся. В любом случае, видно, что будет разделение, критерием которого станет вера и жизнь людей.. 35-36Две женщины будут вместе молоть зерно, и одна будет взята, а другая оставлена17:35-36 Некоторые рукописи включают стих 36: «И будут два человека в поле, и один будет взят, а другой оставлен»..

37– Где, Повелитель? – спросили они. Исо ответил:

– Где труп, туда соберутся и стервятники17:37 Существует множество толкований этого стиха. Вот два наиболее вероятных: 1) где моральное разложение достигнет своего апогея, там неизбежно будут и суды Всевышнего; 2) как по кружащим в небе стервятникам можно безошибочно определить, что там лежит труп, так и пришествие Масеха будет явным для всех..