Luka 16 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 16:1-31

Fanizo la Kapitawo Wosakhulupirika

1Yesu anawuza ophunzira ake kuti, “Panali munthu wina wachuma amene kapitawo wake anzake anamuneneza kuti amawononga chuma chakecho. 2Choncho anamuyitana ndi kumufunsa kuti, ‘Kodi nʼchiyani chimene ndikumva za iwe? Pereka tsatanetsatane wa ntchito yako, pakuti supitirizanso kukhala kapitawo wanga.’

3“Kapitawoyo analingalira kuti, ‘Kodi tsopano ndidzachita chiyani? Bwana wanga andichotsa ntchito. Ine ndilibe mphamvu zokwanira zolimira, komanso ine ndimachita manyazi kupempha. 4Ine ndikudziwa chimene ndidzachita kotero kuti, pamene ntchito yanga yatha pano, anthu adzandilandire mʼnyumba zawo.’

5“Choncho iye anayitana aliyense amene anali ndi ngongole kwa bwana wake. Iye anafunsa woyamba, ‘Kodi uli ndi ngongole yotani kwa bwana wanga?’

6“Iye anayankha kuti, ‘Migolo yamafuta a olivi 800.’

“Kapitawo uja anamuwuza iye, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo, khala pansi msanga ndipo lemba kuti ndi migolo 400.’

7“Kenaka iye anafunsa wachiwiri kuti, ‘Nanga iwe uli ndi ngongole yotani?’

“Iye ayankha kuti madengu a tirigu 1,000.

“Iye anati, ‘Tenga pamene unalemba ngongole yakoyo ndipo ulembepo 800.’

8“Bwana anayamikira kapitawo wosakhulupirikayo popeza anachita mochenjera. Pakuti anthu a dziko lino lapansi ndi ochenjera kwambiri akamachita zinthu ndi anthu ofanana nawo kuposa anthu a kuwunika. 9Ine ndikukuwuzani inu, gwiritsani ntchito chuma cha dziko lapansi kuti mudzipezere nokha abwenzi, kuti pamene chatha mudzalandiridwe mʼmalo okhala amuyaya.

10“Amene akhulupirika pa zinthu zochepa akhoza kukhulupirikanso pa zinthu zambiri, ndipo amene sakhulupirika pa zinthu zochepa adzakhala wosakhulupirika pa zinthu zambiri. 11Ndipo ngati simunakhale okhulupirika pogwiritsa ntchito chuma cha dziko lapansi, ndani amene adzakusungitsani chuma chenicheni? 12Ndipo ngati simunakhale okhulupirika ndi chuma cha mwini wake, ndani amene adzakupatsani katundu wanuwanu?

13“Palibe wantchito amene angatumikire mabwana awiri. Mwina iye adzadana ndi wina ndi kukonda winayo, kapena adzakhala wodzipereka kwa wina ndi kumunyoza winayo. Inu simungathe kutumikira Mulungu komanso ndalama nthawi imodzi.”

14Afarisi amene ankakonda ndalama atamva zimenezi anamuseka Yesu. 15Yesu anawawuza kuti, “Inu ndi amene mumadzilungamitsa nokha pamaso pa anthu, koma Mulungu amadziwa mitima yanu. Zinthu zimene anthu amaziyesa zopambana, ndi zonyansa pamaso pa Mulungu.

Ziphunzitso Zina

16“Malamulo ndi Aneneri zinagwira ntchito mpaka nthawi ya Yohane. Kuyambira nthawi imeneyo, Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ukulalikidwa, ndipo aliyense akuyesetsa mwamphamvu kuti alowemo. 17Nʼkwapafupi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zichoke kulekana ndi kuti kalemba kakangʼono kachoke mʼMalamulo.

18“Aliyense amene asiya mkazi wake ndi kukakwatira mkazi wina akuchita chigololo, ndipo mwamuna amene akwatira mkazi wosiyidwayo akuchitanso chigololo.”

Za Munthu Wachuma ndi Lazaro

19“Panali munthu wachuma amene ankavala zovala zofiirira za mtengowapatali ndipo ankakhala moyo wachisangalalo tsiku lililonse. 20Pa khomo la mpanda wake ankagonekapo munthu wopempha wotchedwa Lazaro, wazilonda thupi lonse 21ndipo ankafunitsitsa atadya zomwe zinkagwa pansi kuchokera pamene munthu wolemerayo amadyerapo. Agalu ankabweranso ndi kumanyambita zilonda zake.

22“Nthawi inafika imene wopemphayo anamwalira ndipo angelo anamunyamula nakamuyika mʼmanja mwa Abrahamu. Munthu wolemerayo anamwaliranso ndipo anayikidwa mʼmanda. 23Ali mʼgehena kuzunzika, anakweza maso ake ndipo anaona Abrahamu ali ndi Lazaro pambali pake. 24Ndipo anafuwula kwa iye kuti, ‘Abambo Abrahamu, mundimvere chisoni ine ndipo mutumeni Lazaroyo kuti aviyike msonga ya chala chake mʼmadzi kuti aziziritse lilime langa, chifukwa ndikumva ululu mʼmoto muno.’

25“Koma Abrahamu anayankha kuti, ‘Mwanawe kumbukira kuti nthawi yamoyo wako unalandira zinthu zako zabwino, pamene Lazaro analandira zinthu zoyipa, koma tsopano akusangalatsidwa kuno ndipo iwe uli mʼmazunzo. 26Ndipo kuwonjezera pa zonsezi, pakati pa inu ndi ife pali chiphompho chachikulu chimene chinayikidwa, kotero kuti amene akufuna kubwera kumeneko sangathe, kapena palibe amene angawoloke kuchokera kumeneko kudzafika kuno.’

27“Iye anayankha kuti, ‘Ndipo ndikupemphani inu, abambo, mutumeni Lazaro ku nyumba ya abambo anga, 28pakuti ine ndili ndi abale asanu. Lolani iye akawachenjeze kotero kuti asadzabwere kumalo ano amazunzo.’

29“Abrahamu anayankha kuti, ‘Ali ndi Mose ndi Aneneri; aleke amvere iwo.’

30“Iye anati, ‘Ayi, bambo Abrahamu, koma ngati wina ochokera kwa akufa adzapita kwa iwo, adzatembenuka mtima.’

31“Anati kwa iye, ‘Ngati iwo samvera Mose ndi Aneneri, sadzakhulupirira ngakhale wina atauka kwa akufa.’ ”

Священное Писание

Лука 16:1-31

Притча о нечестном управителе

1Иса сказал Своим ученикам:

– Управляющий одного богатого человека был обвинён в растрате имущества своего хозяина. 2Хозяин вызвал его к себе и сказал: «Что это я слышу о тебе? Предоставь мне отчёт о своём управлении, потому что ты больше не можешь занимать эту должность».

3Управляющий подумал: «Что же мне теперь делать? Хозяин увольняет меня. Идти копать у меня нет сил, просить милостыню – стыдно… 4Но я знаю, что мне сделать, чтобы, когда меня отсюда уволят, нашлись люди, которые бы приняли меня к себе». 5И он стал звать одного за другим должников своего хозяина. Первого он спросил: «Сколько ты должен моему хозяину?» 6«Четыре тысячи литров оливкового масла», – ответил тот. Управляющий сказал ему: «Возьми свою расписку, быстро садись и переделай на две тысячи»16:6 Букв.: «сто батов… пятьдесят».. 7Затем он спросил второго должника: «А ты сколько должен?» – «Тридцать тонн пшеницы», – ответил тот. Управляющий говорит ему: «Возьми свою расписку и переделай на двадцать четыре»16:7 Букв.: «сто ко́ров… восемьдесят»..

8И хозяин похвалил нечестного управляющего за его находчивость, ведь люди этого мира сообразительнее в делах с себе подобными, чем те, кто встал на путь Всевышнего. 9И Я говорю вам, приобретайте себе друзей с помощью богатства этого неправедного мира, чтобы, когда оно иссякнет, вы были приняты в вечные обители.

10Кто верен в малом, тот верен и в большом, а кто не верен в малом, тот не верен и в большом. 11Поэтому, если вы не были честными в обращении с земным богатством, то кто доверит вам истинное? 12Если с земным вы не могли управиться, то кто вам доверит небесное?16:12 Букв.: «Если вы не были верны в чужом, то кто вам даст ваше?»

13Ни один слуга не может служить двум господам. Он или одного будет ненавидеть, а другого любить, или же одному будет предан, а другим станет пренебрегать. Вы не можете служить одновременно и Всевышнему, и богатству.

14Блюстители Закона, которые любили деньги, слышали всё это и посмеивались над Исой. 15Иса же сказал им:

– Вы умеете изображать себя праведными перед людьми, но Всевышний знает ваши сердца. То, что ценят люди, – мерзость в глазах Всевышнего.

Дополнительные поучения

(Мат. 11:12-13; 5:18, 31-32)

16– Время Таурата и Книги Пророков было до Яхии, сейчас же возвещается Радостная Весть о Царстве Всевышнего, и каждый прилагает усилия, чтобы попасть в него16:16 Или: «и каждый побуждаем войти в него».. 17Но скорее небо и земля исчезнут, чем из Священного Писания пропадёт хотя бы одна чёрточка!

18– Каждый, кто разводится со своей женой и женится на другой, нарушает супружескую верность, и тот, кто женится на женщине, разведённой со своим мужем, также нарушает супружескую верность.

Нищий Элеазар и богач

19– Жил один богатый человек. Он одевался в самую дорогую и изысканную одежду и каждый день устраивал великолепные пиры. 20А у его ворот лежал нищий по имени Элеазар. Он был весь покрыт язвами 21и был бы рад даже объедкам, падающим со стола богача. Собаки подходили и лизали его язвы. 22Но вот нищий умер, и ангелы отнесли его на почётное место рядом с пророком Ибрахимом. Умер и богач, и его похоронили. 23В аду16:23 Букв.: «в мире мёртвых»., где богач терпел мучения, он как-то поднял глаза и увидел вдали Ибрахима, а рядом с ним Элеазара. 24Он позвал: «Отец мой Ибрахим, сжалься надо мной и пошли Элеазара, чтобы тот обмакнул в воду кончик пальца и охладил мой язык, потому что я ужасно мучаюсь в этом огне». 25Но Ибрахим ответил: «Дитя, вспомни, что ты получил в своей жизни доброе, а Элеазар получал только плохое. Сейчас же он здесь получает утешение, а ты страдаешь. 26И кроме того, между нами и вами – огромная пропасть, так что даже если бы кто и захотел отсюда пойти к вам, он не смог бы, и никто оттуда не может перейти к нам». 27Богач сказал: «Тогда прошу тебя, отец, пошли Элеазара в дом моего отца. 28Ведь у меня пятеро братьев, пусть он предупредит их, чтобы и они не попали в это место мучений». 29Ибрахим ответил: «У них есть Таурат16:29 Букв.: «У них есть Муса». и Книга Пророков, пусть их слушают». 30«Нет, отец Ибрахим, – сказал богач, – вот если бы кто-то из мёртвых пришёл к ним, тогда бы они покаялись». 31На это Ибрахим ему ответил: «Если они Мусу и других пророков не слушают, то даже если кто-то воскреснет из мёртвых, их и это не убедит».