Luka 15 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 15:1-32

Fanizo la Nkhosa Yotayika

1Tsopano amisonkho ndi “ochimwa” ankasonkhana kudzamvera mawu ake. 2Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amangʼungʼudza nati, “Munthu uyu amalandira ochimwa ndi kudya nawo.”

3Ndipo Yesu anawawuza fanizo ili: 4“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi yatayika, kodi iye sangasiye 99 zija kutchire ndi kupita kukafuna yotayikayo mpaka atayipeza? 5Ndipo iye akayipeza, amayinyamula pa phewa lake mwachimwemwe 6ndi kupita kwawo. Kenaka amayitana anzake ndi anansi pamodzi, ndi kuti, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza nkhosa yanga yotayika ija.’ 7Ine ndikukuwuzani kuti momwemonso kudzakhala chikondwerero chachikulu kumwamba chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima kusiyana ndi anthu olungama 99 amene ali otembenuka mtima kale.”

Fanizo la Ndalama Yotayika

8“Kapena tiyeni tifanizire mayi amene anali ndi ndalama zasiliva khumi ndipo imodzi nʼkutayika, kodi sayatsa nyale ndi kusesa mʼnyumba ndi kufuna mosamalitsa mpaka atayipeza? 9Ndipo pamene wayipeza, amayitana anzake, ndi anansi pamodzi nati, ‘Kondwerani nane; ine ndayipeza ndalama yanga yotayika ija.’ 10Momwemonso, Ine ndikukuwuzani kuti angelo a Mulungu amakondwera kwambiri chifukwa cha wochimwa mmodzi amene watembenuka mtima.”

Fanizo la Mwana Wolowerera

11Yesu anapitiriza kunena kuti, “Panali munthu amene anali ndi ana aamuna awiri. 12Wamngʼonoyo anati kwa abambo ake, ‘Abambo, patseni gawo langa la chuma chanu.’ Ndipo iye anawagawira awiriwo chuma chawo.

13“Pasanapite nthawi, wamngʼonoyo anasonkhanitsa chuma chake chonse, napita ku dziko lakutali ndipo kumeneko anayamba kumwaza chuma chake mʼnjira zachitayiko. 14Iye atawononga zonse, kunagwa njala yoopsa mʼdziko lonselo ndipo anayamba kusauka. 15Iye anapita kwa nzika ina ya dzikolo nakakhala naye ndi kumagwira ntchito, amene anamutumiza ku munda kukadyetsa nkhumba. 16Iye analakalaka atakhutitsa mimba yake ndi makoko amene nkhumbazo zinkadya, koma panalibe wina amene anamupatsa kanthu.

17“Maganizo ake atabweramo, iye anati, ‘Ndi antchito angati a abambo anga amene ali ndi chakudya chimene amadya nʼkutsalako ndipo ine ndili pano kufa ndi njala! 18Ine ndinyamuka ndi kubwerera kwa abambo anga ndipo ndikati kwa iwo: abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi kwa inu. 19Ndine wosayeneranso kutchedwa mwana wanu; munditenge ngati mmodzi wa antchito anu.’ 20Ndipo iye ananyamuka ndi kupita kwa abambo ake.

“Koma iye akanali patali, abambo ake anamuona ndipo anamvera chisoni; anathamangira mwanayo, namukumbatira ndi kupsompsona.

21“Mwanayo anati, ‘Abambo, ine ndachimwira kumwamba ndi inunso. Ine sindiyenera konse kutchedwa mwana wanu.’

22“Koma abambowo anati kwa antchito ake, ‘Fulumirani! Bweretsani mkanjo wabwino kwambiri ndipo mumuveke. Muvekeni mphete ndi nsapato. 23Bweretsani mwana wangʼombe wonenepa ndipo iphani. Tiyeni tikhale ndi phwando ndi kukondwerera. 24Pakuti mwana wangayu anali wakufa, ndipo ali ndi moyonso; iye anatayika ndipo wapezeka.’ Chomwecho anayamba kukondwerera.

25“Nthawi imeneyi, mwana wake wamkulu uja anali ku munda. Iye atafika pafupi ndi nyumba, anamva anthu akuyimba ndi kuvina. 26Ndipo iye anayitana mmodzi wa antchito, namufunsa chimene chimachitika. 27Iye anayankha kuti, ‘Mʼbale wako wabwera ndipo abambo ako apha mwana wangʼombe wonenepa chifukwa wabwera wamoyo ndipo ali bwino.’

28“Mwana wamkulu anakwiya ndipo anakana kulowa. Chomwecho abambo ake anatuluka ndi kumudandaulira. 29Koma iye anayankha abambo ake kuti, ‘Taonani! Zaka zonsezi ndakhala ndikukutumikirani kugwira ntchito yowawa ndipo palibe pamene sindinamvere malamulo anu. Koma inu simunandipatse ngakhale mwana wambuzi kuti ine ndichite phwando ndi anzanga. 30Koma pamene mwana wanu uyu amene wawononga chuma chanu ndi achiwerewere wabwera ku nyumba, inu mwamuphera mwana wangʼombe wonenepa.’ ”

31Abambowo anati, “Mwana wanga, iwe umakhala ndi ine nthawi zonse ndipo zonse ndili nazo ndi zako. 32Koma tinayenera kukondwera ndi kusangalala, chifukwa mʼbale wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyonso; iye anali wotayika ndipo wapezeka.”

Thai New Contemporary Bible

ลูกา 15:1-32

คำอุปมาเรื่องแกะหลงหาย

(มธ.18:12-14)

1ครั้งนั้นคนเก็บภาษีและ “คนบาป” มาชุมนุมกันเพื่อฟังพระเยซู 2แต่พวกฟาริสีและธรรมาจารย์บ่นพึมพำว่า “ชายคนนี้ต้อนรับคนบาปและร่วมรับประทานกับพวกเขา”

3พระเยซูจึงตรัสคำอุปมาให้พวกเขาฟังว่า 4“สมมุติว่าพวกท่านคนหนึ่งมีแกะหนึ่งร้อยตัวและตัวหนึ่งหายไป เขาจะไม่ละแกะทั้งเก้าสิบเก้าตัวไว้กลางทุ่ง แล้วไปตามหาแกะตัวที่หายไปนั้นจนกว่าจะพบหรือ? 5เมื่อเขาพบแล้วก็แบกแกะนั้นใส่บ่าด้วยความชื่นชมยินดี 6และกลับบ้าน จากนั้นเขาก็เรียกมิตรสหายและเพื่อนบ้านมาพร้อมกัน และกล่าวว่า ‘มาร่วมยินดีกับเราเถิด เรา ได้พบแกะตัวที่หายไปนั้นแล้ว’ 7เราบอกท่านว่าทำนองเดียวกัน ในสวรรค์จะมีความชื่นชมยินดีในคนบาปคนหนึ่งซึ่งกลับใจใหม่ มากยิ่งกว่าในคนชอบธรรมเก้าสิบเก้าคนซึ่งไม่ต้องการกลับใจใหม่”

คำอุปมาเรื่องเหรียญหาย

8“หรือสมมุติว่าหญิงคนหนึ่งมีเหรียญเงินสิบเหรียญ15:8 ภาษากรีกว่า10 แดรกมา(1 แดรกมามีค่าเท่ากับค่าแรง 1 วัน) และหายไปเหรียญหนึ่ง หญิงนั้นจะไม่จุดตะเกียงกวาดเรือนและค้นหาอย่างถี่ถ้วนจนกว่าจะพบหรือ? 9และเมื่อพบแล้ว นางก็เรียกมิตรสหายและเพื่อนบ้านมาพร้อมหน้ากันและกล่าวว่า ‘มาร่วมยินดีกับเราเถิด เราได้พบเหรียญที่หายไปนั้นแล้ว’ 10เราบอกท่านว่าในทำนองเดียวกัน จะมีความชื่นชมยินดีท่ามกลางเหล่าทูตสวรรค์ของพระเจ้าในคนบาปคนเดียวซึ่งกลับใจใหม่”

คำอุปมาเรื่องบุตรที่หลงหาย

11พระเยซูตรัสต่อไปว่า “ชายคนหนึ่งมีบุตรชายสองคน 12บุตรชายคนเล็กพูดกับบิดาว่า ‘บิดาเจ้าข้า ขอยกสมบัติส่วนของข้าพเจ้าให้ข้าพเจ้าเถิด’ ดังนั้นบิดาจึงแบ่งทรัพย์สมบัติของตนให้บุตรทั้งสอง

13“ต่อมาไม่นาน บุตรชายคนเล็กนี้ก็รวบรวมสมบัติทั้งหมดของตนแล้วไปเมืองไกล และผลาญทรัพย์ของตนด้วยการใช้ชีวิตเสเพล 14พอเขาหมดตัว ก็เกิดการกันดารอาหารอย่างหนักทั่วแถบนั้น และเขาเริ่มขัดสน 15ดังนั้นเขาจึงไปรับจ้างชาวเมืองคนหนึ่ง และคนนั้นใช้เขาออกไปเลี้ยงหมูในทุ่งนา 16เขาอยากจะอิ่มท้องด้วยฝักถั่วที่หมูกิน แต่ไม่มีใครให้อะไรเขากิน

17“เมื่อเขาคิดขึ้นได้จึงกล่าวว่า ‘บิดาของเรามีลูกจ้างหลายคน พวกเขามีอาหารเหลือเฟือ แต่นี่เรากำลังจะอดตาย! 18เราจะกลับไปหาบิดาของเราและกล่าวกับท่านว่า บิดาเจ้าข้า ข้าพเจ้าทำบาปต่อสวรรค์และต่อท่านด้วย 19ข้าพเจ้าไม่คู่ควรจะได้ชื่อว่าเป็นบุตรของท่านอีกต่อไป ให้ข้าพเจ้าเป็นเหมือนลูกจ้างคนหนึ่งของท่านเถิด’ 20ดังนั้นเขาจึงลุกขึ้น กลับไปหาบิดาของเขา

“แต่เมื่อเขายังอยู่แต่ไกล บิดาเห็นเขาก็สงสาร จึงวิ่งมาหาบุตรชายแล้วสวมกอดและจูบเขา

21“เขากล่าวกับบิดาว่า ‘บิดาเจ้าข้า ข้าพเจ้าทำบาปต่อสวรรค์และต่อท่านด้วย ข้าพเจ้าไม่คู่ควรจะได้ชื่อว่าเป็นบุตรของท่านอีกต่อไป15:21 สำเนาต้นฉบับเก่าแก่บางสำเนาว่าบุตรของท่านอีกต่อไป ให้ข้าพเจ้าเป็นเหมือนลูกจ้างคนหนึ่งของท่านเถิด

22“แต่บิดาสั่งคนรับใช้ว่า ‘เร็วเข้า! จงนำเสื้อผ้าที่ดีที่สุดมาให้เขาสวมใส่ เอาแหวนมาสวมนิ้วของเขา และเอารองเท้ามาสวมให้เขา 23จงนำลูกวัวขุนมาฆ่า ให้เราจัดงานเลี้ยงฉลอง 24เพราะบุตรชายคนนี้ของเราได้ตายไปแล้วและกลับเป็นขึ้นมาอีก เขาหายไปแล้วและได้พบกันอีก’ ดังนั้นเขาทั้งหลายจึงเริ่มเฉลิมฉลองกัน

25“ฝ่ายบุตรคนโตอยู่ที่ทุ่งนา เมื่อกลับมาใกล้ถึงบ้าน เขาได้ยินเสียงดนตรีและเสียงเต้นรำ 26ดังนั้นเขาจึงเรียกคนรับใช้คนหนึ่งมาถามว่ามีอะไร 27คนรับใช้ตอบว่า ‘น้องชายของท่านกลับมาแล้ว บิดาของท่านจึงให้ฆ่าลูกวัวขุน เพราะท่านได้เขากลับมาโดยสวัสดิภาพ’

28“บุตรคนโตก็โกรธและไม่ยอมเข้าบ้าน บิดาจึงออกมาขอร้องเขา 29แต่เขาตอบบิดาว่า ‘ดูเถิด! หลายปีมานี้ข้าพเจ้าตรากตรำรับใช้ท่าน และไม่เคยขัดคำสั่งของท่านเลย แต่ลูกแพะสักตัวท่านก็ยังไม่เคยยกให้ข้าพเจ้าเพื่อเลี้ยงฉลองกับเพื่อนๆ 30แต่เมื่อลูกคนนี้ของท่านกลับมาบ้านทั้งๆ ที่ได้ผลาญสมบัติของท่านหมดไปกับหญิงโสเภณี ท่านยังฆ่าลูกวัวขุนให้เขา!’

31“บิดากล่าวว่า ‘ลูกเอ๋ย เจ้าอยู่กับพ่อตลอดมา และทุกสิ่งที่พ่อมีก็เป็นของเจ้า 32แต่ที่เราต้องเฉลิมฉลองและยินดีกัน เพราะน้องคนนี้ของเจ้าได้ตายไปแล้วและกลับเป็นขึ้นมาอีก เขาหายไปแล้วและได้พบกันอีก’ ”