Luka 11 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 11:1-54

Yesu Aphunzitsa za ku Pemphera

1Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”

2Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti:

“ ‘Atate,

dzina lanu lilemekezedwe,

ufumu wanu ubwere.

3Mutipatse chakudya chathu chalero,

4mutikhululukire machimo athu,

monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira.

Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’ ”

5Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi, 6chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’

7“Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’ 8Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.

9“Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani. 10Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.

11“Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka? 12Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira? 13Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”

Yesu ndi Belezebabu

14Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa. 15Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.” 16Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.

17Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka. 18Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu. 19Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu. 20Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.

21“Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa. 22Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.

23“Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.

Za Mzimu Woyipa

24“Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’ 25Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza. 26Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”

Munthu Wodala

27Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”

28Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”

Chizindikiro cha Yona

29Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona. 30Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno. 31Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni. 32Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.

Nyale ndi Thupi

33“Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika. 34Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima. 35Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima. 36Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”

Tsoka la Afarisi ndi Alembi Amalamulo

37Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera. 38Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.

39Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa. 40Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja? 41Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.

42“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.

43“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.

44“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”

45Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”

46Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.

47“Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha. 48Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo. 49Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’ 50Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko, 51kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.

52“Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”

53Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso, 54pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.

Священное Писание

Лука 11:1-54

Иса Масих учит учеников молиться

(Мат. 6:9-13; 7:7-11)

1Однажды Иса молился, и когда Он закончил, один из учеников попросил Его:

– Повелитель, научи нас молиться, как и Яхия научил своих учеников.

2Он сказал им:

– Когда вы молитесь, говорите так:

Небесный Отец,

пусть прославится имя Твоё!

Пусть наступит Царство Твоё!

3Хлеб наш насущный давай нам каждый день,

4и прости нам грехи наши,

ведь и мы прощаем всем должникам нашим.

Не дай нам поддаться искушению11:4 В некоторых рукописях присутствуют слова: «…но защити нас от зла»..

5Потом Иса сказал им:

– Предположим, что у кого-то из вас есть друг, и ты, придя к нему в полночь, попросишь: «Друг, одолжи мне три лепёшки. 6Ко мне с дороги заехал гость, и мне нечего ему предложить». 7А тот, находясь в доме, ответит: «Не беспокой меня. Дверь уже заперта, дети мои со мною в постели, не могу я сейчас встать и дать тебе хлеба». 8Говорю вам, что даже если он не встанет и не даст тебе по дружбе, то ему всё-таки придётся сделать то, о чём ты его попросил, из-за твоей назойливости11:8 Или: «…только чтобы не осрамиться». Смысл притчи в следующем: если даже человек из-за назойливости своего товарища (или чтобы избежать позора) ответил на его просьбу, то насколько больше Всевышний желает ответить на молитвы Своих детей..

9Поэтому Я говорю вам: просите – и вам дадут, ищите – и найдёте, стучите – и вам откроют. 10Потому что каждый, кто просит, получает, и кто ищет, находит, и тому, кто стучит, откроют.

11Есть ли среди вас такой отец, который даст своему сыну змею, когда тот попросит рыбы? 12Или, если тот попросит яйцо, даст ему скорпиона? 13Если вы, будучи злы, умеете давать своим детям благие дары, то тем более Небесный Отец даст Святого Духа тем, кто просит у Него!

Иса Масих изгоняет демонов силой Всевышнего

(Мат. 12:22-30; Мк. 3:22-27)

14Однажды Иса изгнал демона немоты. И когда демон вышел, человек, который был нем, заговорил. Люди удивлялись. 15Но некоторые говорили:

– Он изгоняет демонов силой Баал-Зевула (сатаны), повелителя демонов.

16Другие, желая испытать Ису, попросили, чтобы Он показал им знамение с неба. 17Но Иса, зная их мысли, сказал им:

– Любое царство, разделившееся на враждующие части, приходит в запустение, и дом, где есть распря, рушится. 18И если сатана враждует против самого себя, то как устоит его царство? Я говорю это потому, что вы заявляете, будто Я изгоняю демонов силой Баал-Зевула. 19Обвиняя Меня в том, что Я изгоняю демонов силой Баал-Зевула, вы, тем самым, обвиняете и ваших последователей, которые также изгоняют демонов. Так что они будут вам судьями. 20Но если Я изгоняю демонов властью Всевышнего, то это значит, что Всевышний уже устанавливает среди вас Своё Царство.

21Когда сильный и хорошо вооружённый человек охраняет свой дом, то его имущество в безопасности. 22Но если кто-то более сильный нападёт и одолеет его, то он заберёт оружие, на которое полагался хозяин, и разделит добычу.

23Кто не со Мной, тот против Меня, и кто не собирает со Мной, тот растрачивает.

Возвращение нечистого духа

(Мат. 12:43-45)

24– Когда нечистый дух выходит из человека, то он скитается по безводным местам, ища место для отдыха, и не находит его. Тогда он говорит: «Возвращусь-ка я в дом, из которого вышел». 25Когда он возвращается, то находит дом чисто выметенным и убранным. 26Тогда он идёт и берёт семь других духов, ещё более злых, чем он сам, и они приходят и поселяются там. И это для человека ещё хуже того, что было вначале.

Истинное благословение

27Иса ещё говорил, когда одна женщина из толпы крикнула:

– Благословенна та мать, что родила Тебя и выкормила!

28Иса ответил:

– Благословеннее те, кто слышит слово Всевышнего и исполняет его.

Знамение пророка Юнуса

(Мат. 12:39-42)

29Когда людей собралось ещё больше, Иса начал говорить:

– Это поколение – злое. Оно ищет знамения, но им не будет дано никакого знамения, кроме знамения пророка Юнуса. 30И как Юнус стал знамением для жителей Ниневии, так и Ниспосланный как Человек станет знамением для этого поколения11:30 История пророка Юнуса находится в Книге Пророков. То, что пророк Юнус три дня провёл в желудке огромной рыбы, а затем чудным образом был освобождён Всевышним, было прообразом того, что Исе предстояло три дня провести в могильной пещере, а затем воскреснуть (см. Мат. 12:40).. 31Царица Юга11:31 Царица Юга – т. е. царица Шевы (Шева – современная юго-западная Аравия). Её встреча с царём Сулейманом описана в 3 Цар. 10:1-13. встанет в Судный день и обвинит людей этого поколения, потому что она приходила с другого конца света послушать мудрость царя Сулеймана. Сейчас же с вами Тот, Кто больше Сулеймана. 32Жители Ниневии встанут в Судный день и обвинят это поколение, потому что они покаялись от проповеди Юнуса11:32 См. Юнус 3:6-9.. Сейчас же с вами Тот, Кто больше Юнуса.

О внутреннем свете

(Мат. 6:22-23)

33– Никто, зажёгши светильник, не ставит его в погреб или под горшок, наоборот, его ставят на подставку, чтобы все входящие видели свет. 34Твой глаз – светильник твоего тела. Когда твой глаз ясен11:34 Это был фразеологический оборот, обозначающий человека щедрого, в отличие от человека скупого, имеющего «дурной глаз»., тогда и всё твоё тело полно света. Если же у тебя глаз замутнён11:34 Букв.: «если он дурной». Выражение «дурной глаз» было фразеологическим оборотом, обозначающим жадного или завистливого человека (см. Мат. 20:15)., то и всё твоё тело темно. 35Так что смотри, не тьма ли тот свет, который внутри тебя. 36Итак, если всё твоё тело полно света и в нём нет ни одной тёмной части, то оно всё будет светло, как бывает, когда светильник освещает тебя сиянием.

Обличение религиозных вождей

(Мат. 23:1-36)

37Когда Иса так говорил, один блюститель Закона пригласил Его к себе на обед. Иса пришёл и возлёг у стола. 38Блюстителя Закона удивило, что Он не совершил перед едой ритуального омовения11:38 У древних иудеев существовал особый ритуал омовения рук перед приёмом пищи, подобный тому, что можно наблюдать среди народов Востока.. 39Но Повелитель сказал ему:

– Вот вы, блюстители Закона, очищаете чаши и тарелки только снаружи, в то время как внутри вы полны алчности и злобы. 40Глупцы! Разве Тот, Кто сотворил внешнее, не сотворил и внутреннее? 41Что же касается внутреннего, то давайте милостыню11:41 Или: «Но давайте милостыню от всего сердца»; или: «Но давайте милостыню из того, что внутри чаши и тарелки»., и тогда всё у вас будет чисто.

42– Но горе вам, блюстители Закона, потому что вы даёте десятую часть с мяты, руты и других трав, а справедливостью и любовью Всевышнего вы пренебрегаете. И то нужно делать, и другого не оставлять.

43– Горе вам, блюстители Закона, потому что вы любите занимать почётные места в молитвенных домах и любите, когда вас приветствуют в людных местах.

44– Горе вам, вы подобны никак не обозначенным могилам, по которым люди ходят, даже не подозревая об их существовании.

45Один из учителей Таурата сказал Ему:

– Учитель, говоря это, Ты и нас обижаешь.

46Иса ответил:

– Горе и вам, учители Таурата, потому что вы взваливаете на людей ноши, которые невозможно нести, а сами и пальцем не шевельнёте, чтобы помочь им.

47– Горе вам, потому что вы строите надгробные памятники пророкам, которых убили ваши предки. 48Вы сами свидетельствуете о том, что одобряете действия ваших предков: те убивали пророков, а вы строите им надгробные памятники. 49Поэтому и Мудрость Всевышнего11:49 Мудрость Всевышнего – многие толкователи видят здесь указание на Ису Масиха (ср. Мат. 23:34; 1 Кор. 1:24). сказала: «Я пошлю к ним пророков и посланников, но они одних убьют, а других будут преследовать». 50Поэтому нынешнее поколение понесёт ответственность за кровь всех пророков, пролитую от создания мира, 51от крови Авеля и до крови Закарии, убитого во дворе храма, возле жертвенника11:51 У иудеев был другой порядок книг Священного Писания. И согласно ему убийство Закарии последнее из упоминаемых там (см. 2 Лет. 24:20-22). Смерть же Авеля была первым убийством на земле (см. Нач. 4:1-10).. Да, говорю вам, это поколение ответит за всё.

52– Горе вам, учители Таурата, потому что вы присвоили ключ знания. Но и сами не вошли, и тем, кто хотел войти, воспрепятствовали.

53Когда Иса вышел из дома, учители Таурата и блюстители Закона обрушились на Него с яростными обвинениями и каверзными вопросами. 54Они ставили Ему ловушки, пытаясь поймать на слове.